< Przysłów 30 >

1 Te są słowa Agóra, syna Jakiego, i zebranie mów tegoż męża do Ityjela, do Ityjela i Uchala.
Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
2 Zaistem jest głupszy nad innych, a rozumu człowieczego nie mam.
“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
3 I nie nauczyłem się mądrości, a umiejętności świętych nie umiem.
Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
4 Któż wstąpił na niebo, i zasię zstąpił? któż zgromadził wiatr do garści swych? Któż zagarnął wody do szaty swej? któż utwierdził wszystkie kończyny ziemi? Cóż za imię jego? i co za imię syna jego? Wieszże?
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
5 Wszelka mowa Boża jest czysta; on jest tarczą tym, którzy ufają w nim.
“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
6 Nie przydawaj do słów jego, aby cię nie karał, a byłbyś znaleziony w kłamstwie.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
7 Dwóch rzecz żądam od ciebie, nie odmawiajże mi pierwej niż umrę.
“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
8 Marność i słowo kłamliwe oddal odemnie; ubóstwa i bogactwa nie dawaj mi; żyw mię tylko pokarmem według potrzeby mojej;
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
9 Abym snać nasyconym będąc nie zaprzał się ciebie, i nie rzekł: Któż jest Pan? Albo zubożawszy żebym nie kradł, i nie brał nadaremno imienia Boga mego.
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
10 Nie podwodź na sługę przed Panem jego, być snać nie złorzeczył, a ty abyś nie zgrzeszył.
“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
11 Jest rodzaj, który ojcu swemu złorzeczy, a matce swojej nie błogosławi.
“Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
12 Jest rodzaj, który się zda sobie być czystym, choć od plugastwa swego nie jest omyty.
Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 Jest rodzaj, którego są wyniosłe oczy, i powieki jego wywyższone są.
Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
14 Jest rodzaj, którego zęby są jako miecze, a trzonowe zęby jego jako noże na pożarcie ubogich na ziemi, a nędzników między ludźmi.
Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
15 Pijawka ma dwie córki, które mówią: Przynieś, przynieś. Trzy rzeczy są, które nie bywają nasycone, owszem cztery, które nie mówią: Dosyć.
“Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 Grób, i żywot niepłodny, ziemia też nie bywa nasycona wodą, a ogień nie mówi: Dosyć. (Sheol h7585)
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
17 Oko, które się naśmiewa z ojca, i wzgardza posłuszeństwem macierzyńskiem, wykłują kruki u potoków, i orlęta je wyjedzą.
Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
18 Te trzy rzeczy są ukryte przedemną, owszem cztery, których nie wiem:
Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 Drogi orlej na powietrzu, drogi wężowej na skale, drogi okrętowej w pośród morza, i drogi mężowej z panną.
Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 Takać jest droga niewiasty cudzołożącej: je, a uciera usta swoje, i mówi: Nie popełniłam złego uczynku.
Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 Dla trzech rzeczy porusza się ziemia, owszem dla czterech, których znieść nie może:
Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 Dla sługi, kiedy panuje, i dla głupiego, kiedy się nasyci chleba;
Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
23 Dla przemierzłej niewiasty, kiedy za mąż idzie, i dla dziewki, kiedy dziedziczy po pani swojej.
mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 Teć są cztery rzeczy najmniejsze na ziemi, wszakże są mędrsze nad mędrców:
Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 Mrówki, huf słaby, które sobie jednak w lecie gotują pokarm swój;
Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 Króliki, twór słaby, którzy jednak budują w skale dom swój;
mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 Szarańcze króla nie mają, a wszakże wszystkie hufami wychodzą;
dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 Pająk rękoma robi, a bywa w pałacach królewskich.
Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 Te trzy rzeczy są, które wspaniale chodzą, owszem cztery, które zmężyle chodzą:
“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 Lew najmocniejszy między zwierzętami, który przed nikim nie ustępuje:
Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 Koń na biodrach przepasany, i kozieł, i król, przeciw któremu żaden nie powstaje.
Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 Jeźliś głupio uczynił, gdyś się wynosił, albo jeźliś źle myślił, połóżże rękę na usta.
“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 Kto tłucze śmietanę, wybija masło; a kto bardzo nos wyciera, wyciska krew; tak kto wzbudza gniew, wszczyna zwadę.
Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

< Przysłów 30 >