< Przysłów 3 >

1 Synu mój! nie zapominaj zakonu mego, a przykazań moich niech strzeże serce twoje.
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Boć długości dni i lat żywota, i pokoju przyczynią.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Miłosierdzie i prawda niech cię nie opuszczają; uwiąż je u szyi twojej, napisz je na tablicy serca twojego.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Tedy znajdziesz łaskę i rozum dobry przed oczyma Bożemi i ludzkiemi.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Ufaj w Panu ze wszystkiego serca twego, a na rozumie twoim nie spolegaj.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 We wszystkich drogach twoich znaj go, a on prostować będzie ścieszki twoje.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Nie bądź mądrym sam u siebie; ale się bój Pana, a odstąp od złego.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 To będzie zdrowiem żywotowi twemu, a odwilżeniem kościom twoim.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Czcij Pana z majętności twojej, i z pierwiastek wszystkich dochodów twoich.
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 A gumna twoje napełnione będą obfitością, i od wina nowego prasy twoje rozpadać się będą.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Synu mój! karania Pańskiego nie odrzucaj, i nie uprzykrzaj sobie ćwiczenia jego.
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Bo kogo Pan miłuje, tego karze, a to jako ojciec, który się w synu kocha.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Błogosławiony człowiek, który znajduje mądrość, i człowiek, który dostanie roztropności.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Bo lepiej nią kupczyć, niżeli kupczyć srebrem: owszem pożyteczniejszy nad złoto dochód jej.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Droższa jest nad perły, a wszystkie najmilsze rzeczy twoje nie zrównają się z nią.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Przedłużenie dni w prawicy jej, a w lewicy jej bogactwa i zacność.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Drogi jej rozkoszne, i wszystkie ścieszki jej spokojne.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Drzewem żywota jest tym, którzyby się jej chwycili; a którzy się jej trzymają, są błogosławionymi.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Pan mądrością ugruntował ziemię, a roztropnością umocnił niebiosa.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Umiejętnością jego rozstąpiły się przepaści, a obłoki rosą kropią.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Synu mój! niech to nie odstępuje od oczów twych: strzeż prawdziwej mądrości i roztropności;
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 I będą żywotem duszy twojej, a ozdobą szyi twojej.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Tedy będziesz chodził bezpiecznie droga twoją, a noga twoja nie potknie się.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Jeźli się układziesz, nie będziesz się lękał; a gdy się uspokoisz, wdzięczny będzie sen twój.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Nie ulękniesz się strachu nagłego, ani spustoszenia bezbożników, gdy przyjdzie.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Albowiem Pan będzie ufaniem twojem, a nogi twojej będzie strzegł od samołówki.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Nie zbraniaj się dobrze czynić potrzebującemu, gdy cię na to stanie, abyś dobrze czynił.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Nie mów bliźniemu twemu: Idź, a wróć się, a jutroć dam; gdyż to masz u siebie.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Nie knuj złego przeciwko bliźniemu twemu, gdyż on z tobą dowiernie mieszka.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Nie wadź się z człowiekiem bez przyczyny, jeźliżeć nic złego nie wyrządził.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Nie zajrzyj mężowi gwałt czyniącemu, a nie obieraj żadnej drogi jego.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Albowiem przewrotny jest obrzydliwością przed Panem; ale z szczerymi tajemnica jego;
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Przeklęstwo Pańskie jest w domu niezbożnika; ale przybytkowi sprawiedliwych błogosławi,
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Ponieważ on szydzi z pośmiewców, ale pokornym łaskę daje.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Mądrzy dziedzicznie sławę osiędą, ale głupi odniosą zelżywość.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Przysłów 3 >