< Przysłów 28 >

1 Uciekają niezbożni, choć ich nikt nie goni: ale sprawiedliwi jako lwię młode są bez bojaźni.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 Dla przestępstwa ziemi wiele bywa książąt jej; ale dla człowieka roztropnego i umiejętnego trwałe bywa państwo.
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 Mąż ubogi, który uciska nędznych, podobny jest dżdżowi gwałtownemu, po którym chleba nie bywa.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Którzy opuszczają zakon, chwalą niezbożnika; ale ci, którzy strzegą zakonu, są im odpornymi.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Ludzie źli nie zrozumiewają sądu; ale którzy Pana szukają, rozumieją wszystko.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Lepszy jest ubogi, który chodzi w uprzejmości swojej, niżeli przewrotny na drogach swych, chociaż jest bogaty.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Kto strzeże zakonu, jest synem roztropnym; ale kto karmi obżercę, czyni zelżywość ojcu swemu.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 Kto rozmnaża majętność swoję z lichwy i z płatu, temu ją zbiera, który ubogiemu szczodrze będzie dawał.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 Kto odwraca ucho swe, aby nie słuchał zakonu, i modlitwa jego jest obrzydliwością.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Kto zawodzi uprzejmych na drogę złą, w dół swój sam wpadnie; ale uprzejmi odziedziczą rzeczy dobre.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 Mąż bogaty zda się sobie być mądrym; ale ubogi roztropny dochodzi go.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 Gdy się radują sprawiedliwi, wielka jest sława; ale gdy powstawają niepobożni, kryje się człowiek.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 Kto pokrywa przestępstwa swe, nie poszczęści mu się; ale kto je wyznaje i opuszcza, miłosierdzia dostąpi.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Błogosławiony człowiek, który się zawsze boi; ale kto zatwardza serce swoje, wpada w złe.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 Pan niezbożny, panujący nad ludem ubogim jest jako lew ryczący, i jako niedźwiedź głodny.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 Książę bezrozumny wielkim jest drapieżcą: ale kto nienawidzi łakomstwa, przedłuży dni swoje.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 Człowieka, który gwałt czyni krwi ludzkiej, choćby i do dołu uciekał, nikt nie zatrzyma.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Kto chodzi w uprzejmości, zachowany będzie; ale przewrotny na drogach swoich oraz upadnie.
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Kto sprawuje ziemię swoję, chlebem nasycony bywa; ale kto naśladuje próżnujących, ubóstwem nasycony bywa.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 Mąż wierny przyczyni błogosławieństwa; ale kto się prędko chce zbogacić, nie bywa bez winy.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 Mieć wzgląd na osobę, rzecz niedobra; bo nie jeden dla kęsa chleba staje się przewrotnym.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 Prędko chce człowiek zazdrościwy zbogatnieć, a nie wie, iż nać niedostatek przyjdzie.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 Kto strofuje człowieka, większą potem łaskę znajduje, niż ten, co pochlebia językiem.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 Kto łupi ojca swego, albo matkę swoją, a mówi, iż to nie grzech: towarzyszem jest mężobójcy.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 Wysokomyślny wszczyna zwadę; ale kto nadzieję ma w Panu, dostatek mieć będzie.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 Kto ufa w sercu swem, głupi jest; ale kto sobie mądrze poczyna, ten ujdzie nieszczęścia.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 Kto daje ubogiemu, nie będzie miał niedostatku; ale kto od niego odwraca oczy swe, wielkie przeklęstwa nań przyjdą.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 Gdy niepobożni powstawają, kryje się człowiek; ale gdy giną, sprawiedliwi się rozmnażają.
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Przysłów 28 >