< Przysłów 22 >

1 Lepsze jest dobre imię, niż bogactwa wielkie; a przyjaźń lepsza, niż srebro i złoto.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 Bogaty i ubogi spotkali się z sobą; ale Pan jest obydwóch stworzycielem.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 Ostrożny widząc złe ukrywa się; ale prostacy wprost idąc wpadają w szkodę.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 Pokory i bojaźni Pańskiej nagrodą jest bogactwo, i sława i żywot.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Ciernie i sidła są na drodze przewrotnego; kto strzeże duszy swej, oddala się od nich.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Ćwicz młodego według potrzeby drogi jego; bo gdy się zstarzeje, nie odstąpi od niej.
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 Bogaty nad ubogimi panuje; ale ten, co pożycza, sługą bywa tego, który mu pożycza.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 Kto sieje nieprawość, żąć będzie utrapienie, a rózga gniewu jego ustanie.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 Oko dobrotliwe, toć będzie ubłogosławione; bo udziela chleba swego ubogiemu.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Wyrzuć naśmiewcę, a ustanie zwada; owszem uspokoi się swar i pohańbienie.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Kto miłuje czystość serca, a jest wdzięczność w wargach jego, temu król przyjacielem będzie.
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Oczy Pańskie strzegą umiejętności; ale przedsięwzięcia przewrotnego podwraca.
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Leniwiec mówi: Lew na dworzu, w pośród ulicy bym był zabity.
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 Usta obcych niewiast są dół głęboki; na kogo się Pan gniewa, wpadnie tam.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 Głupstwo przywiązane jest do serca młodego; ale rózga karności oddali je od niego.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Kto ciemięży ubogiego, aby sobie przysporzył, także kto daje bogatemu: pewnie zubożeje.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Nakłoń ucha twego, a słuchaj słów mądrych, a serce twoje przyłóż ku nauce mojej;
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 Boć to będzie uciechą, gdy je zachowasz w sercu twojem, gdy będą społem sporządzone w wargach twoich;
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 Aby było w Panu ufanie twoje; oznajmujęć to dziś, a ty tak czyń.
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Izalim ci nie napisał znamienitych rzeczy z strony rad i umiejętności,
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 Abym ci do wiadomości podał pewność powieści prawdziwych, abyś umiał odnosić słowa prawdy tym, którzy cię posłali.
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Nie odzieraj nędznego, przeto że nędzny jest; ani ubogiego w bramie uciskaj.
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 Albowiem Pan się podejmie sprawy ich, i wydrze duszę tym, którzy im wydzierają.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Nie bądź przyjacielem gniewliwemu, a z mężem popędliwym nie obcuj,
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 Byś snać nie przywykł ścieszkom jego, a nie włożył sidła na duszę swoję.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Nie bywaj między tymi, którzy ręczą; ani między rękojmiami za długi;
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 Bo jeźlibyś nie miał czem zapłacić, przeczżeby kto miał brać pościel twoją pod tobą?
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Nie przenoś starej granicy, którą uczynili ojcowie twoi.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 Widziałżeś męża rątszego w sprawach swoich? Takowyć przed królami staje, a nie staje przed podłymi.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.

< Przysłów 22 >