< Przysłów 21 >

1 Serce królewskie jest w ręce Pańskiej jako potoki wód; kędy chce, nakłoni je.
Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
2 Wszelka droga człowieka prosta jest przed oczyma jego; ale Pan, jest który serca waży.
Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
3 Czynić sprawiedliwość i sąd, bardziej się Panu podoba, niżeli ofiara.
Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
4 Wyniosłość oczu i nadętość serca, i oranie niepobożnych są grzechem.
Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
5 Myśli pracowitego pewne dostatki przynoszą; ale każdego skwapliwego przynoszą pewną nędzę.
Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 Zebrane skarby językiem kłamliwym są marnością pomijającą tych, którzy szukają śmierci.
Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
7 Drapiestwo niezbożnych potrwoży ich; bo nie chcieli czynić to, co było sprawiedliwego.
Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
8 Mąż, którego droga przewrotna, obcym jest; ale sprawa czystego jest prosta.
Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
9 Lepiej jest mieszkać w kącie pod dachem, niżeli z żoną swarliwą w domu przestronnym.
Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
10 Dusza niezbożnego pragnie złego, a przyjaciel jego nie bywa wdzięczny w oczach jego.
Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
11 Gdy karzą naśmiewcę, prostak mędrszym bywa; a gdy roztropnie postępują z mądrym, przyjmuje naukę.
Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
12 Bóg daje przestrogę sprawiedliwemu na domie niezbożnika, który podwraca niezbożnych dla złości ich.
Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
13 Kto zatula ucho swe na wołanie ubogiego, i on sam będzie wołał, a nie będzie wysłuchany.
Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
14 Dar potajemnie dany uśmierza zapalczywość, i upominek w zanadrza włożony gniew wielki uspokaja.
Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
15 Radość się mnoży sprawiedliwemu, gdy się sąd odprawuje; ale strach tym, którzy czynią nieprawość.
Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
16 Człowiek błądzący z drogi mądrości w zebraniu umarłych odpoczywać będzie.
Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
17 Mąż, który dobrą myśl miłuje, staje się ubogim; a kto miłuje wino i olejki, nie zbogaci się.
Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18 Niezbożnik będzie okupem za sprawiedliwego, a za uprzejmych przewrotnik.
Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
19 Lepiej mieszkać w ziemi pustej, niż z żoną swarliwą i gniewliwą.
Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
20 Skarb pożądany i olej są w przybytku mądrego; ale głupi człowiek pożera go.
Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
21 Kto naśladuje sprawiedliwości i miłosierdzia, znajduje żywot, sprawiedliwość i sławę.
Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
22 Mądry ubiega miasto mocarzy, a burzy potęgę ufności ich.
Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
23 Kto strzeże ust swoich i języka swego, strzeże od ucisków duszy swojej.
Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
24 Hardego i pysznego imię jest naśmiewca, który wszysko poniewoli i z pychą czyni.
Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
25 Leniwego żądość zabija; bo ręce jego robić nie chcą.
Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
26 Każdego dnia pała pożądliwością; ale sprawiedliwy udziela, a nie szczędzi.
Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
27 Ofiara niepobożnych jest obrzydliwością, a dopieroż gdyby ją w grzechu ofiarował.
Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
28 Świadek fałszywy zaginie; ale mąż dobry to, co słyszy, statecznie mówić będzie.
Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
29 Mąż niezbożny zatwardza twarz swoję; ale uprzejmy sam sprawuje drogę swoję.
Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
30 Niemasz mądrości, ani rozumu, ani rady przeciwko Panu.
Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
31 Konia gotują na dzień bitwy; ale od Pana jest wybawienie.
Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

< Przysłów 21 >