< Przysłów 18 >
1 Człowiek swej myśli, szuka tego, co mu się podoba, a w każdą rzecz wtrąca się.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Nie kocha się głupi w roztropności, ale w tem, co mu objawia serce jego.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Gdy przychodzi niezbożny, przychodzi też wzgarda, a z mężem lekkomyślnym urąganie.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Słowa ust męża mądrego są jako wody głębokie, a źródło mądrości jako potok wylewający.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Nie dobra to, mieć wzgląd na osobę niezbożnego, aby był podwrócony sprawiedliwy w sądzie.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Wargi głupiego zmierzają do swaru, a usta jego do bitwy wyzywają.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 Usta głupiego są upadkiem jego, a wargi jego sidłem duszy jego.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Słowa obmówcy są jako słowa zranionych, a wszakże przenikają do wnętrzności żywota.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Kto niedbały w sprawach swoich, bratem jest utratnika.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Imię Pańskie jest mocną wieżą; sprawiedliwy się do niej uciecze, a wywyższony będzie.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 Majętność bogatego jest miastem jego mocnem, a jako mur wysoki w myśli jego.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Przed upadkiem podnosi się serce człowiecze, a sławę uprzedza poniżenie.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Kto odpowiada, pierwej niż wysłucha, głupstwo to jego i zelżywość.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 Duch męża znosi niemoc swoję; ale ducha utrapionego któż zniesie?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 Serce rozumne nabywa umiejętności, a ucho mądrych szuka jej.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Dar człowieczy plac mu czyni, i przed wielmożnych przywodzi go.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Sprawiedliwym zda się ten, kto pierwszy w sprawie swojej; ale gdy przychodzi bliźni jego, dochodzi go.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 Los uśmierza zwady, i między możnymi rozsądek czyni.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Brat krzywdą urażony trudniejszy nad miasto niedobyte, a swary są jako zawory u pałacu.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 Z owocu ust każdego nasycon bywa żywot jego; urodzajem warg swych będzie nasycony.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 Śmierć i żywot jest w mocy języka, a kto go miłuje, będzie jadł owoce jego.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Kto znalazł żonę, znalazł rzecz dobrą, i dostąpił łaski od Pana.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 Ubogi pokornie mówi; ale bogaty odpowiada surowie.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 Człowiek, który ma przyjaciół, ma się obchodzić po przyjacielsku, ponieważ przyjaciel bywa przychylniejszy nad brata.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.