< Przysłów 17 >

1 Lepszy jest kęs suchego chleba a w pokoju, niżeli pełen dom nabitego bydła ze swarem.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 Sługa roztropny będzie panował nad synem, który jest ku hańbie; a między braćmi będzie dzielił dziedzictwo.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 Tygiel srebra a piec złota doświadcza; ale Pan serc dośwadcza.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 Zły pilnuje warg złośliwych, a kłamca słucha języka przewrotnego.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Kto się naśmiewa z ubogiego, uwłacza stworzycielowi jego; a kto się raduje z upadku czyjego, nie ujdzie pomsty.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Korona starców są synowie synów ich, a ozdoba synów są ojcowie ich.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Nie przystoi mowa poważna głupiemu, dopieroż księciu usta kłamliwe.
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 Jako kamień drogi, tak bywa dar wdzięczny temu, który go bierze; do czegokolwiek zmierzy, zdarzy mu się.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 Kto pokrywa przestępstwo, szuka łaski; ale kto wznawia rzeczy, rozłącza przyjaciół.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 Więcej waży gromienie u roztropnego, niżeli sto plag u głupiego.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 Uporny tylko złego szuka, dla tego poseł okrutny będzie nań zesłany.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 Lepiej jest człowiekowi spotkać się z niedźwiedzicą osierociałą, niżeli z głupim w głupstwie jego.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Kto oddaje złem za dobre, nie wynijdzie złe z domu jego.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 Kto zaczyna zwadę, jest jako ten, co przekopuje wodę; przetoż niż się zwada rozsili, zaniechaj go.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 Kto usprawiedliwia niezbożnego, a winnym czyni sprawiedliwego, oba jednako są obrzydliwością Panu.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 Cóż po dostatku w ręku głupiego, ponieważ do nabycia mądrości rozumu nie ma?
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 Wszelkiego czasu miłuje przyjaciel, a w ucisku stawia się jako brat.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 Człowiek głupi daje rękę, czyniąc rękojemstwo przed twarzą przyjaciela swego.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 Kto miłuje zwadę, miłuje grzech; a kto wynosi usta swe, szuka upadku.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 Przewrotny w sercu nie znajduje dobrego; a kto jest przewrotnego języka, wpadnie we złe.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 Kto spłodził głupiego, na smutek swój spłodził go, ani się rozweseli ojciec niemądrego.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 Serce wesołe oczerstwia jako lekarstwo; ale duch sfrasowany wysusza kości.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 Niezbożny potajemnie dar bierze, aby podwrócił ścieszki sądu.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 Na twarzy roztropnego znać mądrość; ale oczy głupiego aż na kraju ziemi.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 Syn głupi żałością jest ojcu swemu, a gorzkością rodzicielce swojej.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 Zaiste nie dobra, winować sprawiedliwego, albo żeby przełożeni kogo dla cnoty bić mieli.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 Kto zawściąga mowy swe, jest umiejętnym; drogiego ducha jest mąż rozumny.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Gdy głupi milczy, za mądrego poczytany bywa; a który zatula wargi swoje, za rozumnego.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

< Przysłów 17 >