< Przysłów 13 >
1 Syn mądry przyjmuje ćwiczenie ojcowskie, ale naśmiewca nie słucha strofowania.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 Każdy będzie pożywał dobrego z owocu ust swoich; ale dusza przewrotnych krzywdy pożywać będzie.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 Kto strzeże ust swych, strzeże duszy swojej; kto lekkomyślnie otwiera wargi swe, będzie starty.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 Dusza leniwego żąda, a nic nie ma; ale dusza pracowitych zbogaci się.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 Słowa kłamliwego nienawidzi sprawiedliwy; ale niezbożny staje się obrzydliwym i shańbionym.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 Sprawiedliwość strzeże tego, który żyje bez zmazy; ale niezbożność podwraca grzesznika.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 Znajduje się taki co się czyni bogatym, a nie ma nic; i taki, co się czyni ubogim, choć ma wiele bogactw.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 Okup żywota człowieczego jest bogactwo jego; ale ubogi nie słucha łajania.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 Światłość sprawiedliwych jasna: ale pochodnia bezbożnych zgaśnie.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Samą tylko pychą człowiek zwady wszczyna, ale przy tych, co radę przyjmują, jest mądrość.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Bogactwa źle nabyte umniejszą się; ale kto je zgromadza ręką swą, przyczynia ich.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 Nadzieja długa wątli serce; ale żądość wypełniona jest drzewem żywota.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Kto gardzi słowem Bożem, sam sobie szkodzi; ale kto się boi przykazania jego, odniesie nagrodę.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 Nauka mądrego jest źródłem żywota ku ochronieniu się sideł śmierci.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Rozum dobry daje łaskę; ale droga przewrotnych jest przykra.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Każdy ostrożny umiejętnie sobie poczyna; ale głupi rozpościera głupstwo.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 Poseł niezbożny upada we złe; ale poseł wierny jest lekarstwem.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Ubóstwo i zelżywość przyjdzie na tego, który się wyłamuje z karności; ale kto przestrzega upominania, wysławiony będzie.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Żądność wypełniona słodka jest duszy; ale odstąpić od złego, głupim jest obrzydliwością.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Kto chodzi z mądrymi, mądrym będzie; ale kto towarzyszy z głupimi, startym będzie.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Nieszczęście grzeszników ściga; ale sprawiedliwym Bóg dobrem nagrodzi.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 Dobry człowiek zostawia dziedzictwo synom synów swoich; ale majętność grzesznika sprawiedliwemu zachowana bywa.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 Obfita żywność na roli ubogich, a drugi ginie przez nieroztropność.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 Kto zawściąga rózgi swej, ma w nienawiści syna swego; ale kto go miłuje, wczas go karze.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 Sprawiedliwy je, i nasyca duszę swoję; ale żołądek niezbożnych niedostatek cierpi.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.