< Przysłów 10 >
1 Syn mądry rozwesela ojca: ale syn głupi smutkiem jest matki swojej.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Nie pomogą skarby niezbożności; ale sprawiedliwość wyrywa od śmierci.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Nie dopuści Pan łaknąć duszy sprawiedliwego; ale majętność niezbożników rozproszy.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 Do nędzy przywodzi ręka zdradliwa; ale ręka pracowita ubogaca.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Kto zbiera w lecie, jest syn roztropny; kto dosypia we żniwa, jest syn pohańbienia.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Błogosławieństwo jest nad głową sprawiedliwego; ale usta bezbożnych pokrywają nieprawość.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 Błogosławiona jest pamiątka sprawiedliwego; ale imię niezbożnych śmierdzi.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Mądre serce przyjmuje przykazanie; ale głupi od warg swoich upadnie.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Kto chodzi w szczerości, chodzi bezpiecznie; ale kto jest przewrotnym w drogach swoich, wyjawion będzie.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Kto mruga okiem, przynosi frasunek, ale głupi od warg swoich upadnie.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 Usta sprawiedliwego są źródło żywota; ale usta niezbożników pokrywają nieprawość.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Nienawiść wzbudza swary; ale miłość wszystkie przestępstwa pokrywa.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 W wargach roztropnego znajduje się mądrość; ale kij na grzbiecie szalonego.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Mądrzy tają umiejętność; ale usta głupiego bliskie upadku.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Majętność bogatego jest miastem jego mocnem; ale nędza jest ubogich zniszczeniem.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 Praca sprawiedliwego jest ku żywotowi; ale dochód niepobożnych jest ku grzechowi.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Ścieszką żywota idzie, kto przyjmuje karność; ale kto gardzi strofowaniem, w błąd się zawodzi.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Kto pokrywa nienawiść wargami kłamliwemi, i kto rozgłasza hańbę, głupi jest.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 Wielomowność nie bywa bez grzechu; ale kto powściąga wargi swoje, ostrożny jest.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Srebro wyborne jest język sprawiedliwego; ale serce niezbożnych za nic nie stoi.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Wargi sprawiedliwego wiele ich żywią; ale głupi dla głupstwa umierają.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 Błogosławieństwo Pańskie ubogaca, a nie przynosi z sobą utrapienia.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Za śmiech sobie ma głupi, popełnić niecnotę, ale mąż roztropny dzierży się mądrości.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Czego się boi niezbożnik, to nań przychodzi; ale czego żądają sprawiedliwi, Bóg im daje.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Jako przemija wicher, tak się niepobożni nie ostoją; ale sprawiedliwy ma grunt wieczny.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Jako ocet zębom, i jako dym oczom, tak jest leniwy tym, którzy go posyłają.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 Bojaźń Pańska dni przyczynia; ale lata niezbożnego ukrócone bywają.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Oczekiwanie sprawiedliwych jest wesele, ale nadzieja niezbożnych zginie.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 Droga Pańska jest mocą szczeremu; ale strachem tym, którzy broją złości.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Sprawiedliwy się na wieki nie poruszy; ale niezbożnicy nie będą mieszkali na ziemi.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Usta sprawiedliwego rozmnażają mądrość; ale język przewrotny będzie wycięty.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Wargi sprawiedliwego znają, co się Bogu podoba; ale usta niepobożnych są przewrotne.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.