< Filipian 1 >

1 Paweł i Tymoteusz, słudzy Jezusa Chrystusa, wszystkim świętym w Chrystusie Jezusie, którzy są w mieście Filipis, z biskupami i z dyjakonami.
Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
2 Łaska wam i pokój niech będzie od Boga, Ojca naszego, i od Pana Jezusa Chrystusa.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
3 Dziękuję Bogu memu, ilekroć na was wspominam,
Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
4 (Zawsze w każdej modlitwie mojej za wszystkich was z radością prośbę czyniąc).
Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
5 Za społeczność waszę w Ewangielii, od pierwszego dnia aż dotąd;
chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
6 Pewien tego będąc, iż ten, który począł w was dobrą sprawę, dokona aż do dnia Jezusa Chrystusa.
Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
7 Jakoż sprwiedliwa jest, abym ja to rozumiał o was wszystkich, dlatego iż was mam w sercu mojem i w więzieniu mojem, i w obronie, i w utwierdzeniu Ewangielii, was, mówię, wszystkich, którzy jesteście ze mną uczestnikami łaski.
Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
8 Albowiem świadkiem mi jest Bóg, jako was wszystkich pragnę we wnętrznościach Jezusa Chrystusa.
Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
9 I o to się modlę, aby miłość wasza im dalej tem więcej pomnażała się w znajomości i we wszelkim zmyśle,
Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
10 Abyście mogli rozeznać rzeczy różne, żebyście byli szczerymi i bez obrażenia na dzień Chrystusowy,
kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
11 Będąc napełnieni owocami sprawiedliwości, które przynosicie przez Jezusa Chrystusa ku sławie i chwale Bożej.
Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
12 A chcę, bracia! abyście wiedzieli, iż to, co się ze mną dzieje, na większe pomnożenie Ewangielii wyszło.
Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
13 Tak iż związki moje dla Chrystusa rozgłoszone są po wszystkim pałacu cesarskim i u wszystkich inszych.
Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
14 A wiele ich z braci w Panu serca nabywszy z moich związek, śmielszymi są, bez bojaźni mówić słowo.
Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
15 Wszakże niektórzy z zazdrości i z sporu, a niektórzy też z dobrej woli Chrystusa każą.
Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
16 A ci, którzy z sporu Chrystusa opowiadają nieszczerze, mniemają, iż przydawają ucisku związkom moim;
Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
17 A którzy z miłości, wiedzą, żem jest wystawiony ku obronie Ewangielii,
Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
18 Ale cóż na tem? Owszem jakimkolwiek sposobem, lub postawnie, lub w prawdzie Chrystus bywa opowiadany, i z tego się raduję, i jeszcze się radować będę;
Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
19 Gdyż wiem, iż mi to wynijdzie na zbawienie przez modlitwę waszę i pomoc Ducha Jezusa Chrystusa,
pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
20 Według troskliwego oczekiwania i nadziei mojej, iż się w niczem nie zawstydzę; ale z wszelakiem bezpieczeństwem, jako zawsze, tak i teraz, uwielbionym będzie Chrystus w ciele mojem, lub przez żywot, lub przez śmierć.
Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
21 Albowiem mnie życiem jest Chrystus, a umrzeć zysk.
Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
22 A jeźliż żyć w ciele jest mi to owocem pracy mojej, jednak nie wiem, co bym obrać miał.
Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
23 Albowiem jestem ściśniony od tego obojga, pragnąc być rozwiązany, a być z Chrystusem, bo to daleko lepiej:
Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
24 Ale zostać w ciele potrzebniej jest dla was.
Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
25 A będąc tego pewien, wiem, iż zostanę i z wami wszystkimi pomieszkam ku waszemu pomnożeniu i weselu wiary,
Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
26 Aby obfitowała chluba wasza w Chrystusie Jezusie ze mnie, gdy do was zasię przybędę.
kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
27 Tylko się tak sprawujcie, jako przystoi Ewangielii Chrystusowej, abym, lub przyjdę i oglądam was, lub nie przyjdę, słyszał o was, iż stoicie w jednym duchu, jednomyślnie bojując w wierze Ewangielii.
Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
28 Ani w czem nie strachając się przeciwników, co onym jest pewnym znakiem zginienia, a wam zbawienia, a to od Boga;
osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
29 Gdyż wam to dane dla Chrystusa, abyście nie tylko weń wierzyli, ale abyście też dla niego cierpieli,
Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
30 Tenże bój mając, jakiście widzieli we mnie, i jaki teraz o mnie słyszycie.
Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.

< Filipian 1 >