< Liczb 6 >

1 I rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Powiedz synom Izraelskim, a mów do nich: Mąż albo niewiasta, gdy się odłączy, czyniąc ślub Nazarejstwa, aby byli odłączeni Panu,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
3 Od wina i mocnego napoju wstrzymywać się będzie; octu z wina, i octu z mocnego napoju pić nie będzie, i wszystkiego, co się z jagód wytłacza, nie będzie pił; także jagód winnych, świeżych ani suchych, jeść nie będzie.
sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
4 Po wszystkie dni Nazarejstwa swego ze wszystkiego, co wyrasta z macicy winnej, od ziarnka aż do łupiny, jeść nie będzie.
Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
5 Po wszystkie dni ślubu Nazarejstwa swego brzytwa nie postoi na głowie jego, aż wynijdzie czas, do którego się poświęcił Panu; będzie świętym, a zapuści włos na głowie swojej.
“‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
6 Po wszystkie dni, których się odłączy Panu, do umarłego nie wnijdzie.
Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
7 Nad ojcem swym, i nad matką swą, nad bratem swym, i nad siostrą swą, nie splugawi się, gdyby zmarli; albowiem poświęcenie Boga swego ma na głowie swojej.
Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
8 Po wszystkie dni Nazarejstwa swego świętym będzie Panu.
Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
9 I gdyby kto umarł przy nim z prędka a nagle, i splugawiłby głowę poświęcenia jego, ogoli głowę swoję w dzień oczyszczenia swego; dnia siódmego ogoli ją.
“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
10 A dnia ósmego przyniesie dwie synogarlice, albo dwoje gołąbiąt do kapłana ku drzwiom namiotu zgromadzenia;
Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
11 I będzie kapłan ofiarował jedno za grzech, a drugie na ofiarę całopalenia, i oczyści go od tego, czem zgrzeszył nad umarłym, a poświęci głowę jego dnia onego.
Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
12 Potem odłączy Panu dni Nazarejstwa swego, ofiarując baranka rocznego za występek; a dni one pierwsze daremne będą, gdyż splugawione było Nazarejstwo jego.
Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
13 A toć jest prawo Nazarejczyka: Gdy się wypełnią dni Nazarejstwa jego, przyjdzie do drzwi namiotu zgromadzenia,
“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
14 I ofiarować będzie ofiarę swą Panu, baranka rocznego, zupełnego jednego na ofiarę całopalenia, i owcę jednę roczną i zdrową na ofiarę za grzech, i barana jednego zupełnego na ofiarę spokojną;
Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
15 Przytem kosz chlebów przaśnych, z mąki pszennej, placki zagniatane z oliwą, i kreple przaśne oliwą namazane, z ofiarą ich śniedną, i z ofiarą ich mokrą.
ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
16 I będzie ofiarował kapłan przed Panem, i uczyni ofiarę za grzech jego, i całopalenie jego.
“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
17 Barana także ofiarować będzie na spokojną ofiarę Panu z koszem chlebów przaśnych; także ofiarować będzie kapłan ofiarę jego śniedną i ofiarę jego mokrą.
Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
18 I ogoli Nazarejczyk przede drzwiami namiotu zgromadzenia głowę Nazarejstwa swego, a wziąwszy włosy z głowy Nazarejstwa swego, włoży je na ogień, który jest pod ofiarą spokojną.
“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
19 Przytem weźmie kapłan łopatkę warzoną baranią, i jeden placek przaśny z kosza, i jeden krepel niekwaszony, a da w ręce Nazarejczykowe po ogoleniu Nazarejstwa jego;
“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
20 I będzie to tam i sam obracał kapłan na ofiarę obracania przed Panem; a rzecz ta poświęcona dostanie się kapłanowi, tak piersi obracania, jako i łopatka podnoszenia; a potem będzie mógł Nazarejczyk pić wino.
Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
21 Toć jest prawo Nazarejczyka, któryby ślub uczynił, i ta ofiara jego Panu za Nazarejstwo jego, okrom tego, coby więcej uczynić mógł; według ślubu swego, który uczynił, tak uczyni według prawa Nazarejstwa swego.
“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
22 Potem rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
23 Mów do Aarona i do synów jego, a rzecz: Tak błogosławić będziecie synom Izraelskim, mówiąc do nich:
“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
24 Niech ci błogosławi Pan, a niechaj cię strzeże;
“‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
25 Niech rozjaśni Pan oblicze swoje nad tobą, a niech ci miłościw będzie;
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
26 Niech obróci Pan twarz swoję ku tobie, a niechaj ci da pokój.
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
27 I będą wzywać imienia mego nad synami Izraelskimi, a Ja im błogosławić będę.
Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

< Liczb 6 >