< Liczb 34 >
1 Potem rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Rozkaż synom Izraelskim, a powiedz im: Gdy wnijdziecie do ziemi Chananejskiej, (tać jest ziemia, która się wam dostanie za dziedzictwo, ziemia Chananejska z granicami swemi.)
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 Tedy będzie granica wasza ku południowi, od puszczy Syn aż do granic Edomskich, która granica południowa pójdzie od brzegu morza słonego na wschód słońca.
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 I okrąży ta granica od południa do Maaleakrabim, i pójdzie aż ku puszczy Syn, i pójdzie od południa do Kades Barne; a stamtąd wynijdzie do wsi Addar, i pójdzie aż do Asmon.
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 A zakrąży ta granica od Asmon aż do rzeki Egipskiej, a skończy się na zachód.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 Zachodnią zaś granicę będziecie mieli morze wielkie; to wam będzie granicą od zachodu.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 To zaś wasza będzie granica północna; od morza wielkiego wymierzycie sobie do góry Hor.
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 Potem od góry Hor wymierzycie granice, aż gdzie wchodzą do Hemat; a będą się kończyć granice aż do Sedada.
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 I pójdzie ta granica aż do Zefronu, a skończy się u wsi Enan; tę będziecie mieć granice północną.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 Granicę też od wschodu wymierzycie od wsi Enan aż do Sefama.
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 A pójdzie ta granica od Sefama aż do Reblat, od wschodu miasta Ain; i uda się ta granica i dojdzie do brzegu morza Cyneret na wschód słońca.
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 A przyjdzie ta granica aż ku Jordanu, a skończy się u morza słonego. Tać będzie ziemia wasza w granicach swoich w około.
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 Tedy oznajmił Mojżesz synom Izraelskim, mówiąc: Tać jest ziemia, którą dziedzicznie otrzymacie losem, jako rozkazał Pan, abym ją dał dziewięciorgu pokoleniu, i połowie pokolenia Manasesowego.
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 Bo wzięło pokolenie synów Rubenowych według domów ojców swych, i pokolenie synów Gadowych według domów ojców swych, i połowa pokolenia Manasesowego wzięli dziedzictwo swoje.
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 Dwa pokolenia, i pół pokolenia, wzięły dziedzictwo swoje z tej strony Jordanu przeciw Jerychu, ku stronie na wschód słońca.
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 I rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Teć są imiona mężów, którzy wam podzielą w dziedzictwo ziemię: Eleazar kapłan, i Jozue, syn Nunów.
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 Księcia także jednego z każdego pokolenia weźmiecie dla podzielenia w dziedzictwo ziemi.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 A teć są imiona tych mężów: z pokolenia Juda Kaleb, syn Jefunów;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 A z pokolenia synów Symeonowych Samuel, syn Ammiudów.
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 Z pokolenia Benjamin Eliad, syn Chaselenów.
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 A z pokolenia synów Danowych książę Buki, syn Jogolów.
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 Z synów Józefowych z pokolenia synów Manasesowych książę Haniel, syn Efodów.
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 A z pokolenia synów Efraimowych książę Chemuel, syn Seftanów.
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 Z pokolenia zaś Zabulonowego książę Elisafan, syn Farnatów.
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 A z pokolenia synów Isascharowych książę Faltijel, syn Ozanów.
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 Z pokolenia synów Aserowych książę Ahiud, syn Salomiego.
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 A z pokolenia synów Neftalimowych książę Fedael, syn Ammiudów.
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 Cić są, którym rozkazał Pan, aby dali dziedzictwo synom Izraelskim w ziemi Chananejskiej.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.