< Liczb 21 >

1 A gdy usłyszał Chananejczyk, król Harat, który mieszkał na południe, że Izraelczycy ciągnęli oną drogą, którą byli szpiegowie przeszli, tedy zwiódł bitwę z Izraelem, i pojmał ich wiele.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
2 Tam uczynił Izrael ślub Panu, mówiąc: Jeźliże podaż lud ten w ręce moje, do gruntu wywrócę miasta ich.
Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
3 I wysłuchał Pan głos Izraela, a podał mu Chananejczyki: i wytracił je z gruntu, i miasta ich, a nazwał imię onego miejsca Chorma.
Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
4 Potem ruszyli się od góry Hor drogą ku morzu czerwonemu, aby obeszli ziemię Edomską; i utrudził się lud bardzo w onej drodze.
Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
5 Przetoż mówił lud przeciw Bogu, i przeciw Mojżeszowi: Przeczżeście nas wywiedli z Egiptu, aby my pomarli na tej puszczy? bo nie masz chleba, ani wody, a dusza nasza obrzydziła sobie ten chleb nikczemny.
ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
6 Przetoż przypuścił Pan na lud węże ogniste, którzy kąsali lud; i pomarło wiele ludu z Izraela.
Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
7 I przyszedłszy lud do Mojżesza, rzekli: Zgrzeszyliśmy, żeśmy mówili przeciw Panu, i przeciw tobie. Módl się Panu, aby oddalił od nas te węże; i modlił się Mojżesz za ludem.
Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
8 I rzekł Pan do Mojżesza: uczyń sobie węża miedzianego, a wystaw go na drzewcu; i stanie się, ktokolwiek ukąszony będąc wejrzy nań, że żyw zostanie.
Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
9 Sprawił tedy Mojżesz węża miedzianego, i wystawił go na drzewcu; i było to, gdy kogo wąż ukąsił, a spojrzał na węża miedzianego, że żyw został.
Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
10 Zatem ruszyli się synowie Izraelscy, a stanęli obozem w Obot.
Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
11 A z Obot ruszywszy się położyli się obozem na pagórkach gór Habarym na puszczy, która jest przeciw Moabczykom od wschodu słońca.
Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
12 A odszedłszy stamtąd położyli się obozem nad potokiem Zered.
Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
13 Stamtąd odciągnąwszy położyli się obozem u brodu Arnon, który jest na puszczy, a wychodzi z granicy Amorejskiej: albowiem Arnon jest granica Moabska między Moabczykiem i Amorejczykiem.
Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
14 Przetoż mówi się w księgach wojen Pańskich: Przeciwko Wahebowi w wichrze walczył, i przy potokach Arnon.
Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
15 Bo ściekanie tych potoków, które się nachyliło (toczy) ku położeniu Har, to się ściąga ku granicy Moabskiej.
ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
16 Stamtąd potem przyszli do Beer; a tać jest ona studnia, o której mówił Pan do Mojżesza: Zgromadź lud a dam im wody.
Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
17 Tedy śpiewał Izrael tę piosnkę: Wystąp studnio; śpiewajcież o niej;
Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
18 Studnia, którą wykopali książęta, wykopali ją hetmani ludu z ustawcą zakonu, laskami swojemi. A z tej puszczy ruszyli się do Matana;
chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
19 A z Matana do Nahalijelu, a z Nahalijelu do Bamotu;
Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
20 A z Bamotu ku Hagaj, które jest w polach Moabskich, na wierzchu pagórka, który leży ku puszczy.
ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
21 I posłał Izrael posły do Sehona, króla Amorejskiego, mówiąc:
Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
22 Niech przejdziemy przez ziemię twoję; nie pójdziemy ani przez pola ani przez winnice; nie będziemy pić wód z studzien twoich; gościńcem pójdziemy, aż przejdziemy granice twoje.
“Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
23 Ale nie pozwolił Sehon Izraelowi iść przez granice swoje; i zebrawszy Sehon wszystek lud swój, wyciągnął przeciw Izraelowi na puszczę, a gdy przyszedł do Jahazy, zwiódł bitwę z Izraelem.
Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
24 I poraził go Izrael ostrzem miecza, i odziedziczył ziemię jego od Arnonu aż do Jaboku, i aż do ziemi synów Ammonowych; albowiem opatrzone były granice Ammonitów.
Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
25 Tedy pobrał Izrael wszystkie miasta one, i mieszkał we wszystkich miastach Amorejskich, w Hesebon, i we wszystkich wsiach jego.
Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
26 Bo Hesebon było miasto Sehona, króla Amorejskiego, który, gdy pierwej walczył z królem Moabskim, wziął mu był wszystkę ziemię jego z rąk jego aż po Arnon.
Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
27 Dla tegoż mówią w przypowieści: Pójdźcie do Hesebon, a niech zbudują i naprawią miasto Sechonowe.
Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
28 Albowiem wyszedł ogień z Hesebon, a płomień z miasta Sechonowego, i popalił Ar Moabskie, i obywatele wysokich miejsc Arnon.
“Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
29 Biada tobie Moab, zginąłeś o ludu Chamos! podał syny swoje na uciekanie, i córki swoje do więzienia królowi Amorejskiemu Sehonowi.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
30 A zaginęło panowanie ich od Hesebona aż do Dybona; a poburzyliśmy je aż do Nofe, które idzie aż do Medady.
“Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
31 I mieszkał Izrael w ziemi Amorejskiej.
“Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
32 Tedy posłał Mojżesz na szpiegi do Jazer, którego wsi pobrali, wypędziwszy Amorejczyki, którzy tam byli.
Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
33 Potem obróciwszy się szli ku Basan; gdzie wyciągnął Og, król Basański, przeciwko nim, sam i wszystek lud jego, aby z nimi stoczył bitwę w Edrej.
Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
34 Tedy rzekł Pan do Mojżesza: Nie bój się go; bo w ręce twoje podałem go, i wszystek lud jego, i ziemię jego, i uczynisz mu, jakoś uczynił Sehonowi, królowi Amorejskiemu, który mieszkał w Hesebon.
Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
35 I porazili go, i syny jego, ze wszystkim ludem jego, tak iż nikogo z niego nie zostawili, i posiedli dziedzicznie ziemię jego.
Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.

< Liczb 21 >