< Liczb 14 >

1 Tedy wzruszywszy się wszystko mnóstwo krzyczeli i płakał lud przez onę noc.
Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
2 I szemrali przeciwko Mojżeszowi, i przeciwko Aaronowi wszyscy synowie Izraelscy; i mówiło do nich wszystko mnóstwo: Obyśmy byli pomarli w ziemi Egipskiej, albo na tej puszczy!
Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
3 Obyśmy byli pomarli! Czemuż wżdy Pan prowadzi nas do tej ziemi, abyśmy padli od miecza? żony nasze, i dziatki nasze aby były na łup? Izali nam nie lepiej wrócić się do Egiptu?
Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
4 I mówili między sobą: Postanówmy sobie wodza, a wróćmy się do Egiptu.
Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
5 Tedy upadł Mojżesz i Aaron na oblicze swoje przed wszystkiem zgromadzeniem synów Izraelskich.
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
6 A Jozue, syn Nunów, i Kaleb, syn Jefunów, którzy szpiegowali ziemię, rozdarli szaty swoje;
Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
7 I rzekli do wszystkiego zgromadzenia synów Izraelskich, mówiąc: Ziemia, którąśmy przeszli, i przeszpiegowali ją, ziemia jest bardzo dobra.
ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
8 Będzieli nam Pan miłościw, tedy nas wprowadzi do tej ziemi, a da ją nam, ziemię tę, która opływa mlekiem i miodem.
Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
9 Jedno Panu nie bądźcie odpornymi, ani się wy bójcie ludu onej ziemi, bo jako chleb pojeść je możemy; odstąpiła obrona ich od nich, ale Pan jest z nami; nie bójcież się ich.
koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
10 I mówiło wszystko zgromadzenie, aby je ukamionowano; ale chwała Pańska okazała się nad namiotem zgromadzenia wszystkim synom Izraelskim.
Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
11 I rzekł Pan do Mojżesza: Dokądże mię draźnić będzie ten lud? I dokądże mi wierzyć nie będą dla tych wszystkich znaków, którem czynił między nimi?
Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
12 Porażę je morem, i rozproszę je; a ciebie uczynię w naród wielki i możniejszy, niż ten jest.
Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
13 Ale rzekł Mojżesz do Pana: Oto, usłyszą Egipczanie, z których pośrodku wywiodłeś mocą swoją ten lud;
Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
14 I mówić będą z obywatelami ziemi tej, bo słyszeli, żeś ty Panie był w pośrodku ludu tego; żeś okiem w oko widziany był, o Panie, a obłok twój stawał nad nimi, a iż w słupie obłokowym chodziłeś przed nimi we dnie, a w słupie ognistym w nocy.
Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
15 Gdybyś tedy pobił lud ten wszystek aż do jednego, rzekliby poganie, którzy o twej sławie słychali, mówiąc:
Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
16 Iż nie mógł wprowadzić Pan ludu tego do ziemi, o którą im przysiągł: przeto je pobił na puszczy.
‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
17 A tak teraz niech proszę uwielbiona będzie moc Pańska, jakoś rzekł, mówiąc:
“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
18 Pan nie rychły ku gniewowi a wielki w miłosierdziu, znosząc nieprawość i przestępstwo, który winnego nie czyni niewinnym, karząc nieprawość ojców w synach do trzeciego i do czwartego pokolenia;
‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
19 Odpuść proszę nieprawość ludu tego według wielkości miłosierdzia twego, tak jakoś odpuszczał ludowi temu z Egiptu aż dotąd.
Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
20 Tedy rzekł Pan: Odpuściłem według słowa twego.
Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
21 A wszakże, jako Ja żyję, i napełniona jest chwałą Pańską wszystka ziemia:
Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
22 Tak wszyscy, którzy widzieli chwałę moję, i znaki moje, którem czynił w Egipcie, i na puszczy, a kusili mię już po dziesięć kroć, ani byli posłuszni głosowi memu,
palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
23 Nie oglądają ziemi tej, o którąm przysiągł ojcom ich, a żaden z tych, którzy mię draźnili, nie oglądają jej.
palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
24 Ale sługę mego Kaleba, gdyż był w nim duch inakszy, i trwał statecznie przy mnie, wprowadzę do ziemi, do której chodził, a nasienie jego odziedziczy ją.
Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
25 Ale ponieważ Amalekita i Chananejczyk mieszkają w dolinie, przetoż jutro obróćcie się, a idźcie na puszczą, drogą ku morzu czerwonemu.
Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
26 Nad to rzekł Pan do Mojżesza i do Aarona, mówiąc:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
27 I dokądże znosić mam ten zły lud, który szemrze przeciwko mnie? długoż szemrania synów Izraelskich, którzy szemrzą przeciwko mnie, słuchać będę?
“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
28 Mów do nich: Żyję Ja, mówi Pan, że jakoście mówili w uszy moje, tak uczynię wam.
Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
29 Na tej puszczy polegą ciała wasze, i wszyscy policzeni wasi według wszystkiej liczby waszej od dwudziestego roku i wyżej, którzyście szemrali przeciwko mnie.
Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
30 A wy nie wnijdziecie do ziemi tej, o którąm podniósł rękę moję, abym ją wam dał na mieszkanie, okrom Kaleba, syna Jefunowego, i Jozuego, syna Nunowego;
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
31 A dziatki wasze, o którycheście mówili, że będą na łup, te wprowadzę, i oglądają tę ziemię, którąście wy wzgardzili.
Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
32 Ale trupy wasze, wasze trupy mówię, polegą na tej puszczy;
Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
33 A synowie wasi będą się tułali po tej puszczy przez czterdzieści lat, i poniosą karanie za cudzołóstwa wasze, aż wyginą trupy wasze na puszczy.
Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
34 Według liczby dni, w którycheście szpiegowali ziemię, to jest czterdzieści dni, dzień każdy za rok licząc, poniesiecie nieprawości wasze czterdzieści lat, i poznacie pomstę swego odstąpienia ode mnie.
Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
35 Ja Pan mówiłem, że to uczynię temu wszystkiemu zgromadzeniu złemu, które się spiknęło przeciwko mnie; na tej puszczy poginą, i tu pomrą.
Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
36 Oni tedy mężowie, których słał Mojżesz na przeszpiegowanie ziemi, którzy wróciwszy się pobudzili do szemrania przeciwko niemu wszystek lud, puszczając złą sławę o ziemi onej;
Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
37 Pomarli mężowie oni, którzy puszczali sławę złą o ziemi, srogą plaga przed Panem.
Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
38 Ale Jozue, syn Nunów, i Kaleb, syn Jefunów, zostali żywi z mężów onych, którzy chodzili ku przeszpiegowaniu ziemi.
Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
39 I opowiedział Mojżesz te słowa wszystkim synom Izraelskim, i płakał lud bardzo.
Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
40 Tedy rano wstawszy wstąpili na wierzch góry, mówiąc: Oto my pójdziemy na to miejsce, o którem nam Pan powiedział; bośmy zgrzeszyli.
Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
41 Ale im powiedział Mojżesz: Przeczże wy przestępujecie słowo Pańskie? to się wam nie nada.
Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
42 Nie chodźcie; bo nie masz Pana między wami, abyście nie byli pobici od nieprzyjaciół waszych.
Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
43 Bo Amalekita i Chananejczyk tuż przed wami są, i polężecie od miecza; bo dla tego, żeście się odwrócili od Pana, nie będzie Pan z wami.
chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
44 A oni przecię kusili się wnijść na wierzch góry; lecz skrzynia przymierza Pańskiego i Mojżesz nie odchodzili od obozu.
Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
45 Tedy zstąpił Amalekita i Chananejczyk, mieszkający na onej górze, a porazili je, i gonili je aż do Hormy.
Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.

< Liczb 14 >