< Nehemiasza 6 >

1 A gdy usłyszał Sanballat, i Tobijasz, i Giesem Arabczyk, i inni nieprzyjaciele nasi, żem zbudował mur, a że w nim nie zostawało żadnej rozwaliny, chociażem jeszcze wtenczas nie był przyprawił wrót do bram:
Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
2 Tedy posłał Sanballat, i Giesem do mnie mówiąc: Przyjdź, a zejdźmy się społem we wsiach, które są na polu Ono. Ale oni myślili uczynić mi co złego.
Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
3 Przetoż posłałem do nich posłów, wskazując: Zacząłem robotę wielką, przetoż nie mogę zjechać; bo przeczżeby miała ustać ta robota, gdybym jej zaniechawszy jechał do was?
Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
4 Tedy posłali do mnie w tejże sprawie po cztery kroć. A jam im odpowiedział temiż słowy.
Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
5 Potem Sanballat posłał do mnie w tejże sprawie piąty raz sługę swego i list otwarty, w ręce jego,
Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
6 W którym to było napisane: Jest posłuch między narodami, jako Gasmus powiada, że ty i Żydowie myślicie się z mocy wybić, a że ty dlatego budujesz mur, abyś był nad nimi królem ich, jako się to pokazuje.
Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
7 Do tego, żeś i proroków postanowił, aby powiadali o tobie w Jeruzalemie, mówiąc: On jest królem w Judzie. Teraz tedy dojdzie to króla; przetoż przyjdź, a naradzimy się spółecznie.
Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
8 Alem posłał do niego, mówiąc: Nie jest to, co powiadasz; ale sam sobie to wymyślasz.
Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
9 Albowiem oni wszyscy straszyli nas, mówiąc: Osłabieją ręce ich przy robocie, i nie dokonają; prztoż teraz, o Boże! zmocnij ręce moje.
Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
10 A gdym wszedł w dom Semejasza, syna Delajaszowego, syna Mehetabelowego, który był w zawarciu, rzekł mi: Zejdźmy się do domu Bożego, w pośród kościoła, i zamknijmy drzwi kościelne; bo przyjdą, chcąc cię zabić, a w nocy przyjdą, aby cię zabili.
Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
11 Któremum rzekł: Takowyżby mąż, jakim ja jest, miał uciekać? Któż takowy, jakom ja, coby wszedłszy do kościoła, żyw został? Nie wnijdę.
Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
12 I poznałem, że go Bóg nie posłał ale proroctwo mówił przeciwko mnie, bo go Tobijasz i Sanballat byli przenajęli.
Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
13 Przeto bowiem przenajęty był, abym się uląkł, i tak uczynił, i zgrzeszył, ażeby mi to u nich było na złe imię, czemby mi urągali.
Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
14 Pomnijże, o Boże mój! na Tobijasza i Sanballata, według takowych uczynków ich: także na Noadyję prorokinię, i na innych proroków, którzy mię straszyli.
Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
15 A tak dokonany jest on mur dwudziestego i piątego dnia miesiąca Elul, pięćdziesiątego i drugiego dnia.
Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
16 A gdy to usłyszeli wszyscy nieprzyjaciele nasi, i widzieli to wszyscy narodowie, którzy byli około nas, upadło im bardzo serce;
Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
17 Bo poznali, że się ta sprawa od Boga naszego stała. W oneż dni wiele przedniejszych z Judy listy swe często posyłali do Tobijasza, także od Tobijasza przychodziły do nich.
Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
18 Bo wiele ich było w Judzie, co się z nim sprzysięgli, gdyż on był zięciem Sechanijasza, syna Arachowego; a Jochanan, syn jego, pojął był córkę Mesullama, syna Barachyjaszowego.
pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
19 Nadto i dobroczynność jego opowiadali przedemną, i słowa moje odnosili mu; a listy posyłał Tobijasz, aby mię straszył.
Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.

< Nehemiasza 6 >