< Nehemiasza 2 >

1 I stało się miesiąca Nisan roku dwudziestego Artakserksesa króla, gdy było wino przed nim, że wziąwszy wino, podałem je królowi, a nie bywałem przedtem tak smutny przed nim.
Pa mwezi wa Nisani, mʼchaka cha makumi awiri cha ufumu wa Aritasasita, atabwera ndi vinyo pamaso pa mfumu ine ndinatenga vinyoyo ndi kupereka kwa mfumu. Koma ndinali ndisanakhalepo ndi nkhope yachisoni pamaso pake.
2 I rzekł mi król: Czemuż twarz twoja tak smutna, gdyż nie chorujesz? Nic to innego, jedno smutek serca. I zlękłem się nader bardzo.
Tsono mfumu inandifunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani nkhope yako ikuoneka yachisoni pamene iwe sukudwala? Ichi si chinthu china koma chisoni cha mu mtima.” Ine ndinachita mantha kwambiri.
3 I rzekłem do króla: Niech król na wiki żyje. Jakoż nie ma być smutna twarz moja, gdyż miasto, dom grobów ojców moich, zburzono, a bramy jego ogniem popalono?
Ndinawuza mfumu kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wamuyaya! Kodi nkhope yanga ilekerenji kuoneka yachisoni pamene mzinda umene kuli manda a makolo anga, wasanduka bwinja ndipo zipata zake zinawonongedwa ndi moto?”
4 Znowu rzekł do mnie król: Czegoż ty żądasz? A jam się modlił Bogu niebieskiemu.
Apo mfumu inandifunsa kuti, “Tsono ukufuna kundipempha chiyani?” Ndipo ine ndinapemphera kwa Mulungu Wakumwamba.
5 I rzekłem do króla: Zdali się to za rzecz dobrą królowi, i jeżli ma łaskę sługa twój przed obliczem twojem, proszę, abyś mię posłał do ziemi Judzkiej, do miasta grobów ojców moich, abym je pobudował.
Ndipo ndinayankha kuti, “Ngati amfumu chingakukondweretseni, ngati mungakomere mtima mtumiki wanune, mundilole kuti ndipite ku Yuda, ku mzinda kumene kuli manda a makolo anga kuti ndikawumangenso.”
6 Nadto rzekł mi król (a królowa siedziała podle niego): Długoż będziesz na tej drodze, i kiedy się wrócisz? I podobało się to królowi, i posłał mię, gdym mu zamierzył pewny czas.
Tsono mfumu, mfumukazi itakhala pambali pake, anandifunsa kuti, “Kodi kumeneko ukakhalako masiku angati ndipo udzabwera liti?” Ndinayiwuza mfumu nthawi yake ndipo inandilola kuti ndipite.
7 Zatemem rzekł do króla: Zdali się to za rzecz dobrą królowi, niech mi dadzą listy do starostów za rzeką, aby mię przeprowadzili, ażbym przyszedł do ziemi Judzkiej;
Ndipo ndinatinso kwa mfumu, “Ngati zikondweretse mfumu, mundipatse makalata oti ndikapereke kwa abwanamkubwa a ku chigawo cha Patsidya pa Yufurate, kuti akandilole kudutsa mwamtendere mpaka nditakafika ku Yuda.
8 I list do Asafa, dozorcy lasów królewskich, aby mi dał drzewa na przykrycie bram pałacu przy domu Bożym, i na mur miejski, i na dom, do którego wnijdę. I dał mi król listy według ręki Boga mego łaskawej nademną.
Mundipatsenso kalata yokapereka kwa Asafu woyangʼanira nkhalango ya mfumu, kuti akandipatse mitengo yokapangira mitanda ya zipata za nsanja yoteteza Nyumba ya Mulungu, mitanda ya khoma la mzinda ndi ya nyumba yokhalamo ine.” Mfumu indipatse zomwe ndinapempha popeza Yehova wokoma mtima anali nane.
9 A gdym przyszedł do starostów za rzeką, oddałem im listy królewskie. Posłał też był ze mną król rotmistrzów i jezdnych:
Choncho ndinanyamuka ulendo wanga ndipo ndinafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Mfumu nʼkuti itatumiza akulu ankhondo ndi okwera pa akavalo kuti atsagane nane.
10 Co gdy usłyszał Sanballat Horonitczyk, i Tobijasz, sługa Ammonitczyk, bardzo ich to mierziało, że przyszedł człowiek, który się starał o dobro synów Izraelskich.
Sanibalati wa ku Horoni ndi Tobiya wa ku Amoni atamva zimenezi, iwo anayipidwa kwambiri kuti wina wabwera kudzachitira zabwino Aisraeli.
11 Zatem przyszedłszy do Jeruzalemu, mieszkałem tam przez trzy dni.
Ndinafika ku Yerusalemu, ndipo ndinakhala kumeneko masiku atatu.
12 A wstawszy w nocy, ja i mężów trocha ze mną, nie oznajmiłem nikomu, co Bóg mój podał do serca mego, abym uczynił w Jeruzalemie; bydlęcia też nie miałem z sobą, oprócz bydlęcia, na któremem jechał.
Sindinawuze munthu aliyense za zimene Yehova anayika mu mtima mwanga kuti ndichitire mzinda wa Yerusalemu. Choncho ndinanyamuka usiku pamodzi ndi anthu ena owerengeka. Ndinalibe bulu wina aliyense kupatula amene ndinakwerapo.
13 I wyjechałem bramą nad doliną w nocy, ku żródłu smoczemu, i ku bramie gnojowej, i oglądałem mury Jeruzalemskie, które były rozwalone, i bramy jego, które były popalone ogniem.
Ndinatuluka usiku podzera ku Chipata cha ku Chigwa ndi kuyenda kupita ku Chitsime cha Chirombo Chamʼmadzi mpaka ku Chipata cha Zinyalala. Ndinayangʼana makoma a Yerusalemu, amene anagwetsedwa, ndi zipata zake, zimene zinawonongedwa ndi moto.
14 Potem jechałem ku bramie żródła, i ku sadzawce królewskiej, gdzie nie było miejsca bydlęciu, na któremem jechał, aby przejść mogło.
Kenaka ndinapita ku Chipata cha Kasupe ndi ku Dziwe la Mfumu. Koma panalibe malo okwanira akuti bulu wanga adutse.
15 Przetoż jechałem nad potokiem w nocy, a oglądałem mury; skąd wracając się, wyjechałem bramą nad doliną, i takiem powrócił.
Kotero usikuwo ndinapita ku chigwa, ndikuyangʼana khomalo. Pomaliza ndinabwerera ndi kukalowanso mu mzinda kudzera ku Chipata cha ku Chigwa.
16 Ale książęta nie wiedzieli, gdziem jeżdził, i com czynił; bom Żydom, ani kapłanom, ani książętom, ani urzędnikom, ani żadnemu rzemieślnikowi tego aż dotąd nie oznajmił.
Akuluakulu sanadziwe kumene ndinapita kapena zimene ndimachita, chifukwa pa nthawiyi nʼkuti ndisananene kalikonse kwa Ayuda kapena ansembe, anthu olemekezeka kapena akuluakulu, kapena wina aliyense amene anali woyenera kugwira ntchitoyi.
17 Przetożem rzekł do nich: Wy widzicie, w jakiemeśmy uciśnieniu, a jako Jeruzalem spustoszone, i bramy jego popalone są ogniem. Pójdżcież, a budujmy mury Jeruzalemskie, abyśmy nie byli więcej na hańbę.
Ndinawawuza kuti, “Inu mukuona mavuto amene tili nawo. Mukuona kuti mzinda wa Yerusalemu wasanduka bwinja ndipo zipata zake zatenthedwa ndi moto. Tsono tiyeni timangenso makoma a Yerusalemu ndipo sitidzachitanso manyazi.”
18 A gdym im oznajmił, że ręka Boga mego była łaskawa nademną, także i słowa królewskie, które do mnie mówił, rzekli: Wstańmyż a budujmy. I zmocnili ręce swe ku dobremu.
Ndinawawuza za mmene Yehova Mulungu wanga anandichitira zabwino ndiponso mawu amene mfumu inandiwuza. Tsono anati, “Tiyeni tiyambenso kumanga.” Kotero analimbitsana mtima kuti ayambenso ntchito yabwinoyi.
19 Co słysząc Sanballat Horonitczyk, i Tobijasz, sługa Ammonitczyk i Giesem Arabczyk, szydzili z nas, i lekce nas sobie poważyli mówiąc: Cóż to za rzecz, którą czynicie? albo się przeciw królowi buntujecie?
Koma Sanibalati wa ku Horoni, Tobiya wa ku Amoni ndi Gesemu Mwarabu atamva zimenezi, anatiseka ndi kutinyoza. Iwo anafunsa kuti, “Kodi muti ndi chiyani chimene mukuchitachi? Kodi mufuna kuwukira mfumu?”
20 I odpowiedziałem im, a rzekłem do nich: Bóg niebieski, ten nam poszczęści, a my słudzy jego, wstańmy a budujmy; ale wy nie macie działu, ani prawa, ani pamiątki w Jeruzalemie.
Koma ndinawayankha kuti, “Mulungu Wakumwamba atithandiza kuti zinthu zitiyendere bwino. Ife antchito ake tiyambapo kumanga. Koma inu mulibe gawo lanu muno mu Yerusalemu. Mulibe chokuyenerezani kulandira malo ano. Mulibenso chilichonse muno chokumbutsa za inu.”

< Nehemiasza 2 >