< Nahuma 3 >

1 Biada miastu krwawemu; wszystko kłamstwa i łupiestwa pełne jest, a ździerstwo z niego nie wychodzi.
Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
2 Tam będzie słyszane trzaskanie biczów, i grzmot kół, i tupanie koni, i skakanie wozów.
Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
3 Jezdny dobędzie błyszczącego miecza swego, i lśniącego oszczepa; tam będzie wiele pobitych i wielkie gromady trupów, tak, że nie będzie liczby trupów, a przez ciała pobitych walić się będą:
Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
4 Dla wielkości wszeteczeństw nierządnicy rozkosznej, która się bawiła czarami, a zaprzedawała narody wszeteczeństwami swemi, i ludzi gusłami swemi.
Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
5 Otom Ja przeciwko tobie, mówi Pan zastępów, i odkryję podołek twój na twarz twoję, a okażę narodom sprosność twoję, a królestwom hańbę twoję:
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
6 I wyrzucę na cię obrzydliwości i zelżę cię, i wystawię cię za dziw,
Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
7 Tak, że ktokolwiek cię ujrzy, oddali się od ciebie i rzecze: Zburzone jest Niniwe, któżby się go użalił? Gdzieżbym szukał tych, którzyby cię cieszyli?
Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
8 Izaliś ty lepsza, niż ludne miasto No, które leżało między rzekami, wodami otoczone będąc; którego wałem było morze, i od morza mur jego?
Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
9 Murzyńska ziemia i Egipt były siłą jego, i narody niezliczone, Putczycy i Lubimczycy, były mu na pomocy;
Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
10 Wszakże i to w zaprowadzenie i w pojmanie przyszło; maluczkie jego na rogach wszystkich ulic roztrącano a o najsławniejszych jego losy miotano, nawet wszyscy przedniejsi jego okowani są w pęta.
Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
11 Takżeć i ty opojona będziesz, i skryć się musisz, i ty szukać będziesz pomocy przeciwko nieprzyjacielowi.
Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
12 Wszystkie twierdze twoje są jako figowe drzewo z owocem rannym, którym gdy kto zatrząśnie, zaraz wpadają w usta tego, co je jeść chce.
Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
13 Oto lud twój są niewiastami w pośród ciebie; nieprzyjaciołom twoim szeroko otworzone będą bramy ziemi twojej, a ogień pożre zawory twoje.
Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
14 Naczerpaj sobie wody do oblężenia, zmacniaj twierdze twoje, wleź w błoto, i depcz glinę, oprawiwszy cegielnicę;
Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
15 Tam cię pożre ogień, wytnie cię miecz, pożre cię jako chrząszcze; zgromadź się jako chrząszcze, zbierz się jako szarańcza.
Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
16 Rozmnożyłeś kupców twoich nad gwiazdy niebieskie; ale jako chrząszcze przypadają i odlatują, tak i ci.
Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
17 Panowie twoi są jako szarańcza, a hetmani twoi jako wielcy chrząszcze, którzy się kładą obozami na płotach czasu zimna, jedno słońce weszło, alić odlatują, i nie znać miejsca ich, gdzie byli.
Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
18 Zdrzemią się pasterze twoi, o królu Assyryjski! leżeć będą sławni twoi; obfitość ludu twego będzie po górach, ale nie będzie, ktoby go zgromadził.
Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
19 Niemasz lekarstwa na ranę twoję, nieuleczona jest plaga twoja; wszyscy, którzy powieść o tobie usłyszą, klaskać będą rękoma nad tobą; bo na kogoż ustawicznie nie przychodziło okrucieństwo twoje?
Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?

< Nahuma 3 >