< Micheasza 1 >

1 Słowo Pańskie, które się stało do Micheasza Morastytczyka za dni Joatama, Achaza, i Ezechyjasza, królów Judzkich, które w widzeniu słyszał o Samaryi i o Jeruzalemie.
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Słuchajcie wszystkie narody! niech słucha ziemia, i wszystko, co na niej jest, a niech będzie panujący Pan przeciwko wam świadkiem, panujący z kościoła świętobliwości swojej.
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
3 Bo oto Pan wyjdzie z miejsca swojego, a zstąpiwszy deptać będzie po wysokościach ziemi;
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 I rozpłyną się góry pod nim, a doliny popadają się, tak jako wosk od ognia, i jako wody, które spadają na dół.
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 To wszystko się stanie dla przestępstwa Jakóbowego, i dla grzechów domu Izraelskiego. Któż jest przyczyną przestępstwa Jakóbowego? izali nie Samaryja? i któż wyżyn Judzkich? izali nie Jeruzalem?
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
6 Przetoż obrócę Samaryję w gromadę gruzu, jako bywa na polu około winnic, i powrzucam w dolinę kamienie jej, a grunty jej odkryję.
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
7 I wszystkie obrazy jej ryte będą potłuczone, i wszystkie jej dary ogniem spalone, i wszystkie jej bałwany obrócę w pustynię; bo to z zapłaty nierządnicy zgromadziła, przetoż się to zaś na zapłatę nierządnicy obróci.
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
8 Nad tem kwilić i narzekać będę, chodząc zewleczony i nagi; uczynię lament jako smoki i narzekanie jako młode strusięta;
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
9 Przeto, że nieuleczone są rany jej, gdyż doszły aż do Judy, a dosięgły do bramy ludu mego aż do Jeruzalemu.
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 W Giet tego nie opowiadajcie, ani kwiląc płaczcie; walaj się w prochu w domu Orfa;
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
11 Przejdziesz ty, która mieszkasz na miejscu pięknem, obnażoną mając hańbę; nie wnijdzie ta, która mieszka na miejscu w bydło obfitem; płacz będzie w miejscach okolicznych, które od was mają żywność swoję.
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
12 Będzie bowiem bolesna dla dobrych rzeczy ta, która mieszka na miejscach przykrych, przeto, że zstąpi złe od Pana aż do bramy Jeruzalemskiej.
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Zaprzęż w wóz prędkie konie, obywatelko Lachys! któraś powodem grzechu córki Syońskiej, gdyż w tobie znalezione są przestępstwa Izraelskie.
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
14 Przetoż poślę upominki swe do Moreset w Giet; domy Achzyb na oszukanie będą królom Izraelskim.
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
15 Jeszczeć dziedzice przywiodę, o obywatelko Maresy! przyjdzie aż do Odollam, i aż do chwały Izraelskiej.
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
16 Obłyś się i ostrzyż się dla synów rozkoszy twoich; rozszerz łysinę twoję jako orzeł, bo się prowadzą od ciebie.
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

< Micheasza 1 >