< Micheasza 6 >

1 Słuchajcie, proszę, co mówi Pan: Wstań, rozpieraj się z temi górami, a niech słuchają pagórki głosu twego.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Słuchajcie góry sporu Pańskiego, i najmocniejsze grunty ziemi; bo Pan ma spór z ludem swoim, a z Jeruzalemem prawo wiedzie.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 Ludu mój! cóżem ci uczynił, a w czemem ci się uprzykrzył? Odłóż świadectwo przeciwko mnie.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Wszakiem cię wywiódł z ziemi Egipskiej, a z domu niewolników odkupiłem cię, i posłałem przed obliczem twojem Mojżesza, Aarona i Maryję.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Ludu mój! Wspomnij teraz, co za radę uczynił Balak, król Moabski, a co mu odpowiedział Balaam, syn Beorowy; wspomnij też, coć się działo od Syttym aż do Galgal, abyś poznał sprawiedliwości Pańskie.
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 Ale mówisz: Z czemże się stawię przed Panem, a pokłonię się Bogu najwyższemu? Izali się przedeń stawię z ofiarami całopalonemi, z cielcami rocznemi?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Izali się Pan kocha w tysiącach baranów, i w tysiącu tysięcy strumieni oliwy? Izali dam pierworodnego swego za przestępstwo moje? albo owoc żywota mego za grzech duszy mojej?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Oznajmił ci człowiecze, co jest dobrego, i czegoż Pan chce po tobie; tylko abyś czynił sąd, a miłował miłosierdzie i pokornie chodził z Bogiem twoim.
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 Głos Pański na miasto woła: (ale roztropny sam się ogląda na imię twoje, o Boże!) Słuchajcież o rózdze, i kto ją postanowił.
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Izali jeszcze są w domu niezbożnego skarby niesprawiedliwe, i miara niesprawiedliwa i obrzydła?
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Izali mam usprawiedliwić szale niesprawiedliwe, i w worku gwichty fałszywe?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Bogacze jego pełni są zdzierstwa, a obywatele jego mówią kłamstwa, i język ich kłamliwy jest w ustach ich;
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Przetoż i Ja cię też nawiedzę chorobą, uderzę cię, i zniszczę cię dla grzechów twoich.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Jeść będziesz, a nie nasycisz się, i poniżenie twoje będzie w pośrodku ciebie: pochwycisz ale nie wyniesiesz; a co wyniesiesz, na miecz podam.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Ty będziesz siał, ale nie będziesz żął; ty będziesz tłoczył oliwki, ale nie będziesz się oliwą mazał, i moszcz, ale nie będziesz pił wina.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Bo to miasto pilnie przestrzega ustaw Amrego, i wszelakiej sprawy domu Achabowego, i sprawujecie się radami ich, tak abym cię wydał na spustoszenie, i obywateli jego na pośmiech; przetoż hańbę ludu mego nosić będziecie.
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

< Micheasza 6 >