< Malachiasza 1 >

1 Brzemię słowa Pańskiego przeciwko Izraelowi, przez Malachyjasza.
Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
2 Umiłowałem was, mówi Pan, a wy mówicie: W czemżeś nas umiłował? Izali Ezaw nie był bratem Jakóbowi? mówi Pan; wszakżem umiłował Jakóba,
Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
3 A Ezawa miałem w nienawiści, i podałem góry jego na spustoszenie, a dziedzictwo jego smokom na pustyni.
koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
4 Jeźliby rzekła ziemia Edomska: Staliśmy się ubogimi, ale wrócimy się, i pobudujemy miejsca popustoszone, tedy tak mówi Pan zastępów: Niechaj oni budują, a Ja rozwalę; i nazwię ich granicą niepobożności i ludem, który sobie zbrzydził Pan aż na wiek i.
Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
5 To oglądają oczy wasze, a wy rzeczecie: Niech będzie Pan uwielbiony w granicach Izraelskich.
Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
6 Syn ma w uczciwości ojca, a sługa pana swego; jaźlim tedy Ja ojcem, gdzież jest cześć moja? i jeźliżem Ja panem, gdzież jest bojaźń moja? mówi Pan zastępów wam, o kapłani! którzy lekce poważacie imię moje, a wszakże mówicie: W czemże lekce poważamy imię twoje?
“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
7 Którzy przynosząc na ołtarz mój ofiarę splugawioną, mówicie: Czemżeśmy cię splugawili? Tem, że mówicie: Stół Pański splugawiony jest.
“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
8 Bo gdy przywodzicie, co ślepego jest, na ofiarę, izali to nie zła rzecz? I gdy przywodzicie chrome i chore, izali to nie zła rzecz? Ofiaruj to jedno książęciu twemu, obaczysz, jeżeli mu się to podobać będzie, a przyjmieli twarz twoję, mówi Pan zas tępów.
Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Przetoż teraz błagajcie, proszę, oblicze Boże, aby się zmiłował nad nami; ale póki się to dzieje z ręki waszej, izali przyjmie oblicze którego z was? mówi Pan zastępów.
“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
10 Owszem, kto jest między wami, aby zawarł drzwi, albo darmo zapalił na ołtarzu moim? Nie mam chęci do was, mówi Pan zastępów, i ofiary nie przyjmię z ręki waszej.
“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
11 Albowiem od wschodu słońca aż do zachodu jego wielkie jest imię moje między narodami, a na wszelkiem miejscu przyniesione będzie kadzenie imieniowi memu i ofiara czysta; wielkie zaiste imię moje będzie między narodami, mówi Pan zastępów.
Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Lecz wy plugawicie je, gdy mówicie: Stół Pański splugawiony jest; a co nań kładą, jest wzgardzonym pokarmem.
“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
13 Mówicie też: O jakaż to praca! choćbyście to zdmuchnąć mogli mówi Pan zastępów; bo przynosicie to, co jest wydartego, i chromego i schorzałego, a przynosicie to na ofiarę: izali to przyjmę z ręki waszej? mówi Pan.
Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
14 I owszem przeklęty jest zdradliwy, który mając w trzodzie swej samca, a przecię czyniąc śluby ofiaruje Panu to, co jest ułomnego; bom Ja królem wielkim mówi Pan zastępów, a imię moje straszne jest między narody.
“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”

< Malachiasza 1 >