< Kapłańska 7 >

1 Tać jest ustawa ofiary za występek, która jest najświętsza.
“‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
2 Na miejscu, gdzie biją ofiary całopalenia, zabiją ofiarę za występek, a krwią jej pokropią ołtarz z wierzchu w około.
Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
3 A wszystkę tłustość jej ofiarować będzie z niej, ogon i tłustość okrywającą wnętrzności;
Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
4 Obiedwie też nerki z tłustością, która jest na nich, i na polędwicach, i odzieczkę, która jest na wątrobie i na nerkach, odejmie.
Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 I spali to kapłan na ołtarzu na ofiarę ognistą Panu; ofiara to jest za występek.
Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
6 Wszelki mężczyzna z kapłanów będzie ją jadł, na miejscu świętem jedzona będzie; rzecz to najświętsza.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
7 Jako ofiara za grzech, tak ofiara za występek jednaką ustawę mają; kapłanowi, który by go oczyszczał, należeć będzie.
“‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
8 Kapłanowi, który by czyję ofiarę całopaloną ofiarował, skóra tejże ofiary, którą ofiarował, należeć będzie.
Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
9 Także każda ofiara śniedna w piecu upieczona, i wszystko, co na pańwi albo w kotle gotowane będzie, kapłanowi, który to ofiaruje, należeć będzie.
Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
10 Przytem wszelaka ofiara śniedna, zagnieciona z oliwą albo prażona, wszystkim synom Aaronowym należeć będzie, tak jednemu, jako drugiemu.
Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
11 Tać też jest ustawa ofiary spokojnej, którą będą ofiarowali Panu.
“‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
12 Jeźliby kto ofiarował na ofiarę dziękczynienia, tedy ofiarować będzie na ofiarę dziękczynienia placki przaśne, zagniatane z oliwą, i kreple przaśne, pomazane oliwą, i mąkę pszenną, smażoną z temi plackami w oliwie zagniecionemi.
“‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
13 Przy tych plackach będzie też chleb kwaszony ofiarował na ofiarę swoję z ofiarą dziękczynienia spokojnych ofiar swoich.
Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
14 I będzie ofiarował z niego jeden chleb z każdej ofiary na podnoszenie Panu. Kapłanowi, który kropi krwią ofiar spokojnych, należeć to będzie.
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
15 Mięso zaś ofiary dziękczynienia, która jest spokojna, w dzień ofiarowania ofiary jego jedzone będzie; nie zostawią z niego nic do jutra.
Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
16 A jeźliby kto ślubną albo dobrowolną przyniósł ofiarę swoją, w dzień ofiarowania ofiary jego jedzone będzie; a nazajutrz, coby zostało z niej, zjedzą.
“‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
17 Ale jeźliby co zostało mięsa z tej ofiary do trzeciego dnia, ogniem spalone będzie.
Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
18 A jeźliby kto przecię jadł mięso tej ofiary spokojnej dnia trzeciego, nie będzie przyjemny ten, który ją ofiarował; nie będzie mu płatna, owszem obrzydliwością będzie; a kto by jadł z niej, nieprawość swoję poniesie.
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
19 Mięso też, które by się dotknęło czego nieczystego, nie będzie jedzone, ale ogniem spalone będzie; mięso zaś inne, każdy czysty jeść je będzie.
“‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
20 A ktobykolwiek jadł mięso z ofiary spokojnej, ofiarowanej Panu, a byłby nieczysty, wytracony będzie człowiek ten z ludu swego.
Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
21 Jeźliby się też kto dotknął czego nieczystego, bądź nieczystości człowieczej, bądź nieczystości bydlęcej, bądź jakiejkolwiek obrzydliwości nieczystej, a jadłby mięso z ofiary spokojnej, ofiarowanej Panu, tedy wytracony będzie człowiek ten z ludu swego.
Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
22 Rzekł jeszcze Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
23 Powiedz synom Izraelskim, i rzecz: Żadnej tłustości z wołu, ani z owiec, ani z kozy, nie będziesz jadł,
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
24 Aczkolwiek tłustość bydlęcia zdechłego, albo tłustość rozszarpanego może być do wszelakiej potrzeby; ale jeść jej żadnym sposobem nie będziecie.
Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
25 Albowiem ktobykolwiek jadł tłustość z bydlęcia, które ofiarować będzie człowiek na ofiarę ognistą Panu, niechaj wytracony będzie człowiek ten, który jadł, z ludu swego.
Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
26 Także żadnej krwi jeść nie będziecie we wszystkich mieszkaniach waszych, tak z ptaków, jako i z bydląt.
Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
27 Wszelki człowiek, który by jadł jakąkolwiek krew, wytracony będzie człowiek on z ludu swego.
Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
28 Rzekł jeszcze Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
29 Mów do synów Izraelskich, a rzecz im: Kto by ofiarował ofiarę spokojną swoję Panu, przyniesie ofiarę swoję Panu z ofiary spokojnej swojej.
“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
30 Ręka jego przyniesie ofiarę ognistą Panu; tłustość z mostkiem przyniesie, a mostek niech będzie tam i sam obracany na ofiarę przed Panem.
Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
31 Potem spali kapłan tłustość na ołtarzu; ale mostek zostanie Aaronowi i synom jego.
Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
32 A łopatkę prawą oddacie na podnoszenie kapłanowi z ofiar spokojnych waszych.
Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
33 Kto też z synów Aaronowych ofiarować będzie krew ofiar spokojnych i tłustość, temu się dostanie łopatka prawa działem.
Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
34 Albowiem mostek sam i tam obracania, i łopatkę podnoszenia, wziąłem od synów Izraelskich z ofiar ich spokojnych, i dałem je Aaronowi kapłanowi, i synom jego prawem wiecznem od synów Izraelskich.
Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
35 Toć jest dział pomazanego Aarona, i pomazanych synów jego z ofiar ognistych Pańskich, od dnia, któregom im przystąpić rozkazał ku sprawowaniu urzędu kapłańskiego Panu.
Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
36 I rozkazał Pan, aby im to dawano było od dnia, którego je pomazał, od synów Izraelskich prawem wiecznem w narodziech ich.
Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
37 Tać jest ustawa ofiary całopalenia, ofiary śniednej, i ofiary za grzech, i za występek, i poświęcenia, i ofiary spokojnej.
Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
38 Którą rozkazał Pan Mojżeszowi na górze Synaj, dnia, którego przykazywał synom Izraelskim, aby ofiarowali ofiary swe Panu na puszczy Synaj.
Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.

< Kapłańska 7 >