< Kapłańska 16 >

1 Potem mówił Pan do Mojżesza po śmierci dwu synów Aaronowych, którzy ofiarując przed Panem, pomarli;
Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
2 I rzekł Pan do Mojżesza: Mów do Aarona, brata twego, niech nie wchodzi każdego czasu do świątnicy wewnątrz za zasłonę przed ubłagalnią, która jest na skrzyni, aby nie umarł, bo w obłoku okazować się będę nad ubłagalnią.
Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
3 Ale tak wchodzić będzie Aaron do świątnicy z cielcem na ofiarę za grzech, a z baranem na ofiarę całopalenia.
“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
4 W szatę lnianą poświęconą oblecze się, a ubiory lniane będą na ciele jego; i pasem lnianym opasze się, i czapkę lnianą włoży na głowę; szaty święte są; i umyje wodą ciało swe, a oblecze się w nie.
Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
5 A od zgromadzenia synów Izraelskich weźmie dwu kozłów na ofiarę za grzech, i jednego baranka na całopalenie.
Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
6 I będzie ofiarował Aaron cielca swego na ofiarę za grzech, i uczyni oczyszczenie za się, i za dom swój.
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
7 Weźmie też dwu kozłów, a postawi je przed Panem u drzwi namiotu zgromadzenia.
Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
8 I rzuci Aaron na oba kozły losy, los jeden Panu, a los drugi Azazelowi.
Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
9 I będzie ofiarował Aaron onego kozła, na którego padł los Panu, i ofiarować go będzie za grzech.
Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
10 Ale kozła, na którego padł los Azazela, postawi żywego przed Panem, aby oczyszczenie uczynił przezeń, a wypuścił go do Azazela na puszczę.
Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
11 I będzie ofiarował Aaron cielca, na ofiarę za grzech twój, a oczyszczenie uczyni za się, i za dom swój, i zabije cielca na ofiarę za grzech swój.
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
12 Tedy weźmie pełną kadzielnicę węgla rozpalonego z ołtarza przed oblicznością Pańską, i pełne garści swe kadzenia wonnego utłuczonego i wniesie za zasłonę.
Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
13 A włoży ono kadzenie na ogień przed Panem, aby okrył dym kadzenia ubłagalnią, która jest nad świadectwem, a nie umrze.
Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
14 Potem wziąwszy ze krwi cielca onego, kropić będzie palcem swym na ubłagalni ku wschodowi słońca; także przed ubłagalnią kropić będzie siedem kroć tą krwią palcem swym.
Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
15 Zabije też kozła na ofiarę za grzech ludu, a wniesie wewnątrz krew jego za zasłonę; i uczyni ze krwią jego, jako uczynił ze krwią cielca, i kropić będzie nią nad ubłagalnią i przed ubłagalnią.
“Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
16 Tak oczyści świątnicę od nieczystot synów Izraelskich, i od przestępstw ich, i od wszystkich grzechów ich; toż też uczyni namiotowi zgromadzenia, który jest między nimi, w pośrodku nieczystot ich.
Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
17 A żaden człowiek niech nie będzie w namiocie zgromadzenia, gdy on wchodzić będzie ku oczyszczaniu do świątnicy, aż wynijdzie i wykona oczyszczenie sam za się i za dom swój, i za wszystko zgromadzenie Izraelskie.
Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
18 I wynijdzie do ołtarza, który jest przed Panem, a oczyści go; i wziąwszy krwi cielcowej i krwi kozłowej, pomaże rogi ołtarza w około;
“Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
19 A pokropi go z wierzchu tąż krwią palcem swym siedem kroć, a oczyści go, i poświęci go od nieczystot synów Izraelskich.
Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
20 Potem gdy odprawi oczyszczenie świątnicy i namiotu zgromadzenia i ołtarza, ofiarować będzie kozła żywego.
“Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
21 A włożywszy Aaron obie ręce swe na głowę kozła żywego, wyznawać będzie nad nim wszystkie nieprawości synów Izraelskich, i wszystkie przestępstwa ich ze wszystkiemi grzechami ich, a włoży je na głowę kozła onego, i wypuści go przez człowieka na to obranego na puszczą.
Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
22 A tak poniesie on kozieł na sobie wszystkie nieprawości ich do ziemi pustej; i wypuści kozła onego na puszczą.
Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
23 Potem wróciwszy się Aaron do namiotu zgromadzenia, złoży z siebie szaty lniane, w które się był oblekł, wchodząc do świątnicy, i zostawi je tam.
“Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
24 Omyje też ciało swoje wodą, na miejscu świętem, i oblecze się w szaty swe; a wyszedłszy sprawować będzie ofiarę całopalenia swego, i ofiarę całopalenia ludu, i uczyni oczyszczenie za się, i za lud.
Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
25 A tłustość ofiary za grzech spali na ołtarzu.
Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
26 A ten, który zawiódł kozła do Azazela, upierze szaty swe; a omywszy ciało swoje wodą, potem wnijdzie do obozu.
“Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
27 Cielca zaś ofiarowanego za grzech, i kozła za grzech, których krew wniesiona była ku sprawowaniu oczyszczenia do świątnicy, wyniosą precz za obóz, i spalą ogniem skóry ich, i mięso ich, i gnój ich.
Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
28 A ten, co je palić będzie, upierze szaty swoje, a omywszy ciało swoje wodą, potem wnijdzie do obozu.
Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
29 To też będzie wam za ustawę wieczną: Miesiąca siódmego, dziesiątego dnia tegoż miesiąca, trapić będziecie dusze wasze, i żadnej roboty nie będziecie robić, tak w domu zrodzony, jako przychodzień, który gościem jest między wami;
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
30 Bo w ten dzień oczyści was kapłan, abyście oczyszczeni byli od wszystkich grzechów waszych przed Panem oczyszczeni będziecie.
chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
31 Sabatem odpocznienia będzie wam to, w który trapić będziecie dusze wasze ustawą wieczną.
Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
32 A oczyszczać będzie kapłan, który jest pomazany, a którego poświęcone są ręce ku sprawowaniu urzędu miasto ojca jego, a oblecze się w szaty lniane, w szaty święte;
Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
33 I oczyści świątnicę świętobliwości, i namiot zgromadzenia; i ołtarz oczyści, i kapłany, i wszystek lud zgromadzony oczyści.
Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
34 I będzie to wam za ustawę wieczną ku oczyszczaniu synów Izraelskich od wszystkich grzechów ich raz w rok. I uczynił Mojżesz, jako mu był rozkazał Pan.
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.

< Kapłańska 16 >