< Kapłańska 14 >

1 Potem rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Tać jest ustawa około trędowatego w dzień oczyszczenia jego: przywiedziony będzie do kapłana.
“Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
3 A wynijdzie kapłan precz za obóz: a obaczyli kapłan, że oto uleczona jest zaraza trądu, trądem zarażonego,
Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
4 Tedy rozkaże kapłan temu, który się oczyszcza, aby wziął dwa wróble żywe i zdrowe, i drzewo cedrowe, i jedwabiu karmazynowego, i hizopu.
wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
5 I rozkaże kapłan zabić jednego wróbla nad naczyniem glinianem, nad wodą żywą.
Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
6 Wróbla tedy żywego weźmie, i drzewo cedrowe, i jedwab karmazynowy i hizop, a omoczy to wszystko z wróblem żywym we krwi wróbla zabitego nad wodą żywą.
Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
7 I pokropi tego, który się oczyszcza od trądu, siedem kroć, i ogłosi go być czystym, a puści wróbla żywego w pole.
Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
8 A ten, który się oczyszcza, upierze szaty swoje, i ogoli wszystkie włosy swoje, a umyje się wodą, i czystym będzie. Potem wnijdzie do obozu, a będzie mieszkał przed namiotem swoim przez siedem dni.
“Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
9 Potem dnia siódmego ogoli wszystkie włosy swe, głowę swą, i brodę swą, i brwi nad oczyma swemi, i wszystkie inne włosy swe ogoli; przytem upierze szaty swe, i ciało swe omyje wodą, a tak oczyszczon będzie.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
10 A dnia ósmego weźmie dwu baranków zupełnych, i owcę jednę roczną, zupełną, i trzy dziesiąte części efy mąki pszennej na ofiarę śniedną, zmieszaną z oliwą, i miarkę oliwy,
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
11 Tedy kapłan, który oczyszcza człowieka, który ma być oczyszczony, postawi z temi rzeczami przed Panem, u drzwi namiotu zgromadzenia.
Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 Potem weźmie kapłan barana jednego, i będzie go ofiarował na ofiarę za występek, z oną miarką oliwy, i będzie to tam i sam obracał na ofiarę obracania przed obliczem Pańskiem.
“Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
13 Zabije też baranka onego na miejscu, gdzie biją ofiary za grzech i ofiarę całopalenia, na miejscu świętem; bo jako ofiara za grzech tak ofiara za występek należy kapłanowi; rzecz najświętsza jest.
Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
14 I weźmie kapłan krwi z ofiary za występek, i pomaże kapłan koniec ucha prawego onemu, który się oczyszcza; także palec wielki u prawej ręki jego i palec wielki u prawej nogi jego.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
15 Weźmie też kapłan z onej miarki oliwy, a naleje na dłoń swoję lewą;
Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
16 A omoczy palec swój prawy w oliwie, która jest na lewej dłoni jego, i pokropi oliwą z palca swego siedem kroć przed obliczem Pańskiem.
aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
17 A z ostatku oliwy, która jest na dłoni jego, pomaże kapłan koniec ucha prawego onemu, który się oczyszcza, i wielki palec prawej ręki jego, także wielki palec prawej nogi jego z onejże krwi, która jest ofiarą za występek.
Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
18 A coby zostało oliwy, która jest na dłoni kapłanowej, pomaże tem głowę onego, który się oczyszcza; i tak go oczyści kapłan przed obliczem Pańskiem.
Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
19 Uczyni także kapłan ofiarę za grzech, i oczyści tego, który się oczyszcza, od nieczystości jego, a potem zabije ofiarę całopalenia.
“Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
20 I ofiarować będzie kapłan ofiarę całopalenia, i ofiarę śniedną na ołtarzu; tak oczyści go kapłan, i czystym będzie.
ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
21 A jeźliby kto był tak ubogi, iżby tego nie przemógł, tedy weźmie baranka jednego na ofiarę za występek na podnoszenie dla oczyszczenia swego, i jednę dziesiątą część efy mąki pszennej zagniecionej z oliwą na ofiarę śniedną i miarkę oliwy.
“Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
22 Nad to dwie synogarlice, albo dwoje gołąbiąt, czego dostać może, z których jedno będzie na ofiarę za grzech, a drugie na ofiarę całopalenia;
Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
23 I przyniesie je w ósmy dzień oczyszczenia swego do kapłana, do drzwi namiotu zgromadzenia, przed obliczność Pańską.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
24 Weźmie tedy kapłan baranka ofiary za występek, i miarkę oliwy; i będzie to obracał tam i sam kapłan na ofiarę obracania przed Panem.
Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
25 A zabije baranka na ofiarę za występek: a wziąwszy kapłan ze krwi ofiary za występek, pomaże koniec ucha prawego temu, który się oczyszcza; i palec wielki prawej ręki jego, i palec wielki prawej nogi jego.
Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
26 Oliwy także naleje kapłan na lewą dłoń swoję.
Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
27 I kropić będzie kapłan palcem swoim prawym z oliwy, która jest na lewej ręce jego siedem kroć przed obliczem Pańskiem.
ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
28 Pomaże też kapłan oną oliwą, która jest na dłoni jego, koniec ucha prawego temu, który się oczyszcza; także wielki palec prawej ręki jego, i wielki palec prawej nogi jego na miejscu krwi z ofiary za występek;
Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
29 A ostatkiem oliwy, która jest na dłoni kapłana, pomaże głowę onego, który się oczyszcza, aby go oczyścił przed Panem.
Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
30 Także uczyni z jedną synogarlicą, albo z jednem gołębięciem, czegokolwiek z tych dostać może.
Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
31 Czego dostać mógł, jedno z tych będzie ofiarą za grzech, a drugie na ofiarę całopalenia z ofiarą śniedną; a tak oczyści kapłan tego, który się oczyszcza przed obliczem Pańskiem.
imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
32 A tać jest ustawa o tym, na którym by była zaraza trądu, który wszystkiego mieć nie może ku oczyszczeniu swemu.
“Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
33 Rzekł potem Pan do Mojżesza i do Aarona, mówiąc:
“Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
34 Gdy wnijdziecie do ziemi Chananejskiej, którą Ja wam dawam w osiadłość, a dopuściłbym zarazę trądu na który dom osiadłości waszej:
Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
35 Tedy on, którego dom jest, przyjdzie i opowie to kapłanowi, mówiąc: Jakoby zaraza trądu zda mi się być w domu moim,
mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
36 Rozkaże tedy kapłan wyprzątnąć dom pierwej niż sam wnijdzie, aby oglądał zarazę onę, iżby się nic nie splugawiło, coby było w domu, a potem kapłan wnijdzie, aby oglądał on dom.
Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
37 A oglądając onę zarazę, ujrzeli zarazę na ścianie domu, jakoby dołki czarne, przyzieleńszym, albo przyczerwieńszym, a na spojrzeniu byłoby głębsze niż ściana.
Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
38 Tedy wynijdzie kapłan z domu onego przede drzwi, i zamknie on dom przez siedem dni.
wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
39 Wróci się potem kapłan dnia siódmego i obejrzy; a jeźli się rozszerzyła zaraza na ścianach domu onego,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
40 Rozkaże kapłan wyłamać ono kamienie, na którem by była zaraza, i wyrzucić je precz za miasto na miejsce nieczyste;
wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
41 A dom rozkaże wewnątrz oskrobać wszędy w około; i wyrzucą on proch który oskrobali, precz za miasto na miejsce nieczyste;
Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
42 I wezmą kamienie insze i wprawią na miejsce innych kamieni; i wapna też inszego wezmą a potynkują dom.
Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
43 A jeźliby się odnowiła ona zaraza, i rozszerzyła się po domu po wyrzuceniu kamienia, i po wyskrobaniu domu i po tynkowaniu jego:
“Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
44 Tedy wnijdzie kapłan; a ujrzeli, że się rozszerzyła ona zaraza po domu, trąd jest jadowity w domu onym, nieczysty jest.
wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
45 Zatem rozwalą on dom, kamienie jego, i drzewo jego i wszystko wapno domu onego, a wyniosą precz za miasto na miejsce nieczyste.
Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
46 A ten kto by wszedł do domu onego, po wszystkie dni, póki był zawarty, nieczystym będzie aż do wieczora.
“Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
47 A kto by spał w onym domu, upierze szaty swoje; także kto by jadł w tymże domu, upierze szaty swoje.
Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
48 Lecz jeźliby wyszedłszy kapłan obaczył, iż się nie szerzy zaraza po domu po tynkowaniu jego, tedy osądzi kapłan, że dom on jest czysty; bo uleczona jest zaraza ona.
“Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
49 A weźmie na oczyszczenie onego domu dwu wróblów, i drzewo cedrowe, i jedwabiu, karmazynu, i hizopu;
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
50 I zabije wróbla jednego nad naczyniem glinianem, nad wodą żywą;
Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
51 A wziąwszy drzewo cedrowe i hizop, i jedwab karmazynowy, i wróbla żywego, omoczy to wszystko we krwi wróbla zabitego i w wodzie żywej, a pokropi ten dom siedem kroć.
Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
52 I tak oczyści on dom krwią wróbla onego, i wodą żywą i wróblem żywym i drzewem cedrowem, i hizopem, i jedwabiem czerwonym.
Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
53 Potem puści wróbla żywego precz za miasto w pole; tak oczyści on dom, i czystym będzie.
Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
54 Tać jest ustawa o każdej zarazie trądu, i plamy czarnej:
Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
55 I o trądzie na szacie i na domu;
nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
56 I o sadzelu, i o świerzbie, i o białej plamie,
khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
57 Żeby poznać, gdy kto jest nieczystym, i gdy kto czystym. Tać jest ustawa około trądu.
kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.

< Kapłańska 14 >