< Księga Sędziów 8 >

1 I rzekli do niego mężowie z Efraim: Przeczżeś to nam uczynił, iżeś nas nie wezwał, gdyś szedł walczyć przeciwko Madyjanitom? i swarzyli się z nim srodze.
Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
2 A on rzekł: Cóżem ja takiego uczynił, jako wy? izali nie lepsze jest poślednie zbieranie wina Efraimowe, niż pierwsze zbieranie Abieserowe?
Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
3 W rękę waszą podał Bóg książęta Madyjańskie, Oreba i Zeba; i cóżem mógł takiego uczynić, jako wy? Tedy się uśmierzył duch ich przeciw niemu, gdy mówił te słowa.
Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
4 A gdy przyszedł Giedeon do Jordanu, przeprawił się przezeń sam, i trzy sta mężów, którzy z nim byli spracowani w pogoni.
Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
5 I rzekł do mieszczan w Sokot: Dajcie proszę po bochenku chleba ludowi, który idzie za mną, bo są spracowani, a ja będę gonił Zebeę i Salmana, króle Madyjańskie.
Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
6 Ale mu rzekli przedniejsi z Sokot: Izali już moc Zeby i Salmana jest w rękach twoich, żebyśmy dać mieli wojsku twemu chleba?
Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
7 Którym rzekł Giedeon: Więc kiedy poda Pan Zebeę i Salmana w rękę moję, tedy będę młócił ciała wasze cierniem z tej puszczy i ostem.
Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
8 Szedł zasię stamtąd do Fanuel, i mówił także do nich; ale mu odpowiedzieli mężowie z Fanuel, jako odpowiedzieli mężowie w Sokot.
Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
9 Tedy też powiedział mężom z Fanuel, mówiąc: Gdy się wrócę w pokoju, rozwalę tę wieżę.
Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
10 Ale Zebee i Salmana byli w Karkor, i wojska ich z nimi około piętnastu tysięcy, wszyscy, którzy byli pozostali ze wszystkiego wojska z ludzi od wschodu słońca; a pobitych było sto i dwadzieścia tysięcy mężów walecznych.
Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
11 Tedy ciągnął Giedeon drogą tych, co mieszkali w namiociech, od wschodu słońca Nobe i Jegbaa, i uderzył na obóz, (a obóz się był ubezpieczył, )
Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
12 A uciekli Zebee i Salmana, i gonił je, i pojmał onych dwóch królów Madyjańskich, Zebeę i Salmana, i wszystko wojsko ich strwożył.
Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
13 Potem się wrócił Giedeon, syn Joasów, z bitwy, niż weszło słońce;
Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
14 A pojmawszy młodzieńca z mężów Sokot, wypytał go, który spisał mu przedniejszych w Sokot i starszych jego, siedemdziesiąt i siedem mężów.
Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
15 A przyszedłszy do mężów Sokot, rzekł: Otóż Zebeę i Salmana, którymiście mi urągali, mówiąc: Izali moc Zeby i Salmana jest w rękach twoich, abyśmy mieli dać mężom twoim spracowanym chleba?
Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
16 Przetoż wziąwszy starsze miasta onego, i ciernia z onej pustyni i ostu, dał na nich przykład innym mężom Sokot.
Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
17 Wieżę też Fanuel rozwalił, i pobił męże miasta.
Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
18 Rzekł potem do Zeby i do Salmana: Co zacz byli mężowie oni, któreście pobili w Tabor? A oni odpowiedzieli: Takowi byli jakoś ty; każdy z nich na wejrzeniu był, jako syn królewski.
Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
19 I rzekł: Braciać to moi, synowie matki mojej byli; żywie Pan, byście je byli żywo zachowali, nie pobiłbym was.
Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
20 I rzekł do Jetra, pierworodnego swego: Wstań, a pobij je. Ale nie dobył młodzieńczyk miecza swego, przeto iż się bał; bo jeszcze był pacholęciem.
Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
21 Tedy rzekli Zebee i Salmana: Wstań ty, a rzuć się na nas; bo jaki mąż, taka siła jego. A tak wstawszy Giedeon, zabił Zebeę i Salmana, i pobrał klejnoty, które były na szyjach wielbłądów ich.
Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
22 I rzekli Izraelczycy do Giedeona: Panuj nad nami, i ty, i syn twój, i syn syna twego; boś nas wybawił z ręki Madyjańczyków.
Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
23 Na to odpowiedział im Giedeon: Nie będę ja panował nad wami, ani będzie panował syn mój nad wami; Pan panować będzie nad wami.
Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
24 Nadto rzekł do nich Giedeon: Będę was prosił o jednę rzecz, aby mi każdy z was dał nausznicę z łupu swego; (bo nausznice złote mieli, będąc Ismaelczykami.)
Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
25 I rzekli: Radzić damy; i rozpostarłszy szatę rzucali na nię każdy nausznicę z łupów swoich.
Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
26 I była waga nausznic onych złotych, które sobie uprosił, tysiąc i siedemset syklów złota, oprócz klejnotów i zawieszenia i szat szarłatowych, które były na królach Madyjańskich, i oprócz łańcuchów, które były na szyjach wielbłądów ich.
Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
27 I sprawił z tego Giedeon Efod, a położył go w mieście swem w Efra; i scudzołożył się tam wszystek Izrael, chodząc za nim, a było to Giedeonowi i domowi jego sidłem.
Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
28 A tak byli poniżeni Madyjańczycy przed synami Izraelskimi, i nie podnieśli więcej głowy swojej; i była w pokoju ziemia przez czterdzieści lat za dni Giedeona.
Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
29 Wrócił się tedy Jerobaal, syn Joasów, i mieszkał w domu swoim.
Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
30 A miał Giedeon siedmdziesiąt synów, którzy poszli z biódr jego; albowiem miał wiele żon.
Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
31 Miał też założnicę, która była z Sychem, a ta mu urodziła syna, i dała mu imię Abimelech.
Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
32 Umarł potem Giedeon, syn Joasów, w starości dobrej, a pogrzebion jest w grobie Joasa, ojca swego w Efra, które jest ojca Esrowego.
Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
33 A gdy umarł Giedeon, odwrócili się synowie Izraelscy, i scudzołożyli się, idąc za Baalem, i postawili sobie Baalberyt za boga.
Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
34 I nie pamiętali synowie Izraelscy na Pana, Boga swego, który je wyrwał z rąk wszystkich nieprzyjaciół ich okolicznych;
Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
35 I nie uczynili miłosierdzia z domem Jerobaala Giedeona według wszystkich dobrodziejstw, które on był uczynił Izraelowi.
Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.

< Księga Sędziów 8 >