< Księga Sędziów 6 >

1 Potem czynili synowie Izraelscy złe przed oczyma Pańskiemi, i podał je Pan w ręce Madyjanitów przez siedem lat.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
2 A zmocniła się ręka Madyjanitów nad Izraelem, tak iż przed Madyjanitami kopali sobie synowie Izraelscy lochy, które były w górach, i jaskinie i twierdze.
Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
3 A bywało, gdy czego nasiał Izrael, że przychodził Madyjan i Amalek, i ludzie ze wschodu słońca, a najeżdżali go;
Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
4 I położywszy się obozem przeciwko nim, psowali zboża ziemi, aż gdzie chodzą do Gazy, nic nie zostawując na pożywienie Izraelczykom, ani owiec, ani wołów, ani osłów.
Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
5 Albowiem oni i stada ich przyciągali, i namioty ich, a przychodzili jako szarańcza w mnóstwie, i nie było im i wielbłądom ich liczby; tak przychodząc do ziemi spustoszyli ją.
Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
6 Tedy znędzony był Izrael bardzo od Madyjanitów, i wołali synowie Izraelscy do Pana.
Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
7 A gdy wołali synowie Izraelscy do Pana z przyczyny Madyjanitów.
Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
8 Posłał Pan męża proroka do synów Izraelskich, i mówił do nich: Tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Jam was wywiódł z ziemi Egipskiej, a wywiodłem was z domu niewoli.
Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
9 I wyrwałem was z ręki Egipczanów, i z ręki wszystkich, którzy was trapili, którem przed wami wygnał, i dałem wam ziemię ich;
Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
10 A powiedziałem wam: Jam Pan, Bóg wasz, nie bójcież się bogów Amorejskich, w których ziemi wy mieszkacie; aleście nie usłuchali głosu mego.
Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
11 Przyszedł potem Anioł Pański i stanął pod dębem, który był w Efra, w dziedzictwie Joasa, ojca Esrowego. A Giedeon, syn jego, młócił zboże na bojewisku, aby z niem uciekł przed Madyjanitami.
Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
12 Tedy mu się ukazał Anioł Pański, i rzekł do niego: Pan z tobą, mężu waleczny.
Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
13 I odpowiedział mu Giedeon: Proszę Panie mój, jeźli Pan jest z nami, a czemuż na nas przyszło to wszystko? gdzież teraz są wszystkie cuda jego, które nam opowiadali ojcowie nasi, mówiąc: Izali z Egiptu nie wywiódł nas Pan? a teraz opuścił nas Pan, i podał nas w ręce Madyjanitów.
Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
14 Tedy wejrzawszy nań Pan rzekł: Idźże z tą twoją mocą, a wybawisz Izraela z ręki Madyjańczyków; izalim cię nie posłał?
Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
15 A on rzekł do niego: Proszę Panie mój, czemże wybawię Izraela? oto naród mój podły jest w Manase, a jam najmniejszy w domu ojca mego.
Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
16 I rzekł do niego Pan: Ponieważ Ja będę z tobą, przetoż porazisz Madyjanity, jako męża jednego.
Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
17 A on mu odpowiedział: Jeźliżem proszę znalazł łaskę przed oczyma twemi, daj mi znak, że ty mówisz ze mną.
Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
18 Nie odchodź proszę stąd, aż zaś przyjdę do ciebie, a przyniosęć ofiarę moję, i położę ją przed tobą. I odpowiedział: Ja poczekam, aż się wrócisz.
Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
19 Odszedłszy tedy Giedeon zgotował koźlątko z stada a z miary mąki przaśne chleby, a mięso włożył w kosz, a polewkę mięsną wlał w garnek, i przyniósł to do niego pod dąb, i ofiarował.
Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
20 I rzekł do niego Anioł Boży: Weźmij to mięso i te chleby niekwaszone, a połóż na onej skale polewką polawszy; i uczynił tak.
Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
21 Zatem ściągnął Anioł Pański koniec laski, którą miał w ręce swojej, i dotknął się mięsa i przaśników, i wyszedł ogień z skały, a spalił mięso i chleby przaśne; a między tem Anioł Pański odszedł od oczu jego.
Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
22 A widząc Giedeon, iż to był Anioł Pański, rzekł: Ach, Panie Boże, czemużem widział Anioła Pańskiego twarzą w twarz?
Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
23 I rzekł mu Pan: Pokój z tobą; nie bój się, nie umrzesz.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
24 Przetoż zbudował tam Giedeon ołtarz Panu, i nazwał go: Pan pokoju; aż do dnia tego ten jeszcze jest w Efracie, ojca Esrowego.
Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
25 I stało się onej nocy, że mu rzekł Pan: Weźmij cielca dorosłego, który jest ojca twego, tego cielca drugiego siedmioletniego, a rozwal ołtarz Baalów, który jest ojca twego, i gaj, który jest około niego, wysiecz;
Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
26 A zbuduj ołtarz Panu, Bogu twemu, na wierzchu tej skały na równinie, a weźmij tego cielca drugiego, i uczyń z niego całopalenie przy drwach z gaju, który wysieczesz.
Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
27 Wziąwszy tedy Giedeon dziesięć mężów z sług swoich, uczynił jako mu rozkazał Pan; a iż się bał domu ojca swego i mężów miasta, nie uczynił tego we dnie, ale uczynił w nocy.
Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
28 A gdy wstali mężowie miasta rano, ujrzeli rozwalony ołtarz Baalów, i gaj, który był podle niego, wyrąbany, i cielca onego drugiego ofiarowanego na całopalenie na ołtarzu zbudowanym.
Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
29 Zatem rzekł jeden do drugiego: Któż to wżdy uczynił? A gdy się pytali i dowiadowali, powiedziano: Giedeon, syn Joasów, uczynił to.
Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
30 Tedy rzekli mężowie miasta do Joasa: Wywiedź syna twego, niech umrze, iż rozrzucił ołtarz Baalów, a iż wyciął gaj, który był około niego.
Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
31 I odpowiedział Joas wszystkim, którzy stali około niego: A wyż się to swarzyć macie o Baala? Izali wy go wybawicie? Kto by się oń zastawiał, niech umrze tegoż poranku; jeźli bogiem jest, niech się mści tego, że rozwalono ołtarz jego.
Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
32 I nazwano go onegoż dnia Jerubaal, mówiąc: Niech się mści nad nim Baal, iż rozwalił ołtarz jego.
Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
33 Tedy wszyscy Madyjanitowie, i Amalekitowie, i ludzie od wschodu słońca zebrali się wespół, a przeprawiwszy się przez Jordan, położyli się obozem w dolinie Jezreel.
Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
34 Ale Duch Pański przyoblókł Giedeona, który zatrąbiwszy w trąbę zwołał domu Abiezerowego do siebie.
Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
35 I wyprawił posły do wszystkiego pokolenia Manasesowego, i zebrali się do niego; posły też posłał do Asera, i do Zabulona, i do Neftalima, i zajechali im.
Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
36 Tedy rzekł Giedeon do Boga: Jeźli wybawisz przez rękę moję Izraela, jakoś powiedział.
Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
37 Oto, ja położę runo wełny na bojewisku; jeźliż rosa tylko na runo upadnie, a wszystka ziemia sucha będzie, tedy będę wiedział, iż wybawisz przez rękę moję Izraela, jakoś powiedział.
onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
38 I stało się tak; bo wstawszy nazajutrz, ścisnął runo, i wyżdżął rosy z runa pełną czaszę wody.
Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
39 Nadto rzekł Giedeon do Boga: Niech się nie wzrusza gniew twój przeciwko mnie, że przemówię jeszcze raz. Niech doświadczę proszę jeszcze raz na tem runie; niech będzie, proszę, suche samo runo tylko, a na wszystkiej ziemi niech będzie rosa.
Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
40 I uczynił tak Bóg onej nocy, że było samo runo suche, a na wszystkiej ziemi była rosa.
Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.

< Księga Sędziów 6 >