< Księga Sędziów 21 >

1 Nadto przysięgli mężowie Izraelscy w Masfa, mówiąc: Żaden z nas nie da córki swej Benjaminczykom za żonę.
Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
2 A tak poszedł lud do domu Bożego, i trwali tam aż do wieczora przed Bogiem, a podniósłszy głos swój, płakali płaczem wielkim.
Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
3 I rzekli: O Panie, Boże Izraelski, czemuż się to stało w Izraelu, że ubyło dzisiaj z Izraela jedno pokolenie?
Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
4 Tedy nazajutrz wstawszy rano lud zbudowali tam ołtarz, a sprawowali całopalone i spokojne ofiary.
Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
5 Zatem rzekli synowie Izraelscy: Któż jest, co nie przyszedł do zgromadzenia ze wszystkich pokoleń Izraelskich do Pana? (Bo się byli wielką przysięgą zawiązali przeciw temu, któryby nie przyszedł do Pana do Masfa, mówiąc: Śmiercią umrze.
Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
6 I żałowali synowie Izraelscy Benjamina, brata swego, a mówili: Wygładzone jest dziś pokolenie jedno z Izraela.
Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
7 Cóż uczynimy tym, co pozostali, aby mieli żony, gdyżeśmy przysięgli przez Pana, że im nie mamy dać córek naszych za żony?)
Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
8 Rzekli tedy: Jestże kto z pokoleń Izraelskich, coby nie przyszedł do Pana do Masfa? a oto, nie przyszedł był nikt do obozu z Jabes Galaad do zgromadzenia.
Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
9 Bo gdy liczono lud, tedy nikogo tam nie było z obywateli Jabes Galaad.
Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
10 I posłało tam zgromadzenie dwanaście tysięcy mężów walecznych, rozkazując im i mówiąc: Idźcie, a pobijcie obywatele Jabes Galaad ostrzem miecza, i niewiasty i dzieci.
Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
11 A tak sobie postąpicie: Każdego mężczyznę, i każdą niewiastę, która męża uznała, zabijecie.
Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
12 Naleźli tedy z obywateli Jabes Galaad cztery sta dzieweczek, panien, które nie uznały męża obcując z nim, i przywiedli je do obozu do Sylo, które było w ziemi Chananejskiej.
Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
13 Potem posłało wszystko zgromadzenie, a mówiło do synów Benjaminowych, którzy byli na skale Remmon, i przyzwali ich w pokoju.
Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
14 Przetoż wrócił się Benjamin onego czasu, i dali im żony, które byli żywo zachowali z niewiast Jabes Galaad, ale im się ich jeszcze nie dostawało.
Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
15 A lud żałował Benjamina, iż uczynił Pan przerwę w pokoleniach Izraelskich.
Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
16 Tedy rzekli starsi zgromadzenia tego: A z tymi drugimi cóż uczynimy, aby mieli żony, gdyż niewiasty wygładzone są z Benjamina?
Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
17 Nadto rzekli: Dziedzictwo Benjamina pozostałym należy, aby nie zaginęło pokolenie z Izraela.
Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
18 A my nie możemy im dać żon z córek naszych, (gdyż byli przysięgli synowie Izraelscy, mówiąc: Przeklęty, kto da żonę Benjaminczykowi.)
Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
19 Potem rzekli: Oto święto Pańskie uroczyste bywa na każdy rok w Sylo, które jest ku północy od Betel, a na wschód słońca ku drodze, która idzie od Betel ku Sychem, a pod południa leży ku Lebnie.
Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
20 A tak rozkazali synom Benjaminowym, mówiąc: Idźcie, a zasadźcie się w winnicach,
Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
21 A patrzajcie, gdy córki Sylo wynijdą gromadą do tańca; tam wyszedłszy z winnic, porwij każdy z was sobie żonę z córek Sylo, a potem idźcie do ziemi Benjamin.
ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
22 A gdy przyjdą ojcowie ich, albo bracia ich skarżyć się przed nami, tedy im rzeczemy: Zmiłujcie się nad nimi dla nas; bośmy nie wzięli dla każdego z nich żony na wojnie, a wyście im ich też nie dali; przetoż nie jesteście winni.
Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
23 Tedy uczynili tak synowie Benjamin, i nabrali żon według liczby swojej z onych co tańcowały, które porwawszy odeszli, i wrócili się do dziedzictwa swego, a pobudowawszy miasta mieszkali w nich.
Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
24 A tak rozeszli się stamtąd synowie Izraelscy onego czasu, każdy do pokolenia swego i do domu swego, a szedł stamtąd każdy do dziedzictwa swego.
Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
25 W one dni nie było króla w Izraelu; każdy, co mu się dobrego zdało to czynił.
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.

< Księga Sędziów 21 >