< Księga Sędziów 19 >

1 I stało się w one dni, gdy króla nie było w Izraelu, że mąż niektóry Lewita, mieszkający przy stronie góry Efraim, pojął sobie żonę założnicę z Betlehem Juda.
Pa nthawi imeneyo ku Israeli kunalibe mfumu. Mlevi wina ankakhala kutali ku dziko lamapiri la Efereimu. Iyeyu anatenga mzikazi wa ku Betelehemu, mʼdziko la Yuda.
2 A bawiła się nierządem przy nim założnica jego; potem odeszła od niego do domu ojca swego, do Betlehem Juda; i była tam u niego przez cztery miesiące.
Tsiku lina mzikazi uja anakwiyira mwamuna wake ndipo anamuchokera kupita kwa abambo ake ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Anakakhala kumeneko miyezi inayi.
3 Wstawszy tedy mąż jej, szedł za nią, aby ją ubłagawszy zasię ją przywiódł, mając z sobą sługę swego, i parę osłów. Tedy ona wwiodła go w dom ojca swego, którego gdy ujrzał ojciec onej dziewki, radował się z przyjścia jego.
Mwamuna wake anamulondola kuti akayankhule naye mofatsa kumupempha kuti abwerere. Iye anali ndi antchito ake ndi abulu ake awiri. Anafika ku nyumba kwa mkazi uja ndipo iye anamulowetsa mʼnyumba ya abambo ake. Abambo aja atamuona mnyamata uja anamulandira mwachimwemwe.
4 I przyjął go wdzięcznie świekier jego, ojciec dziewki onej, a mieszkał u niego, przez trzy dni, i jedli i pili i nocowali tam.
Mpongozi wake, yemwe anali abambo a mtsikanayo, anamupempha kuti aswere. Choncho anakhalako masiku atatu. Ankadya, kumwa ndi kugona komweko.
5 A dnia czwartego, gdy wstali bardzo rano, wstał i on, aby odszedł. Ale rzekł ojciec onej dziewki do zięcia swego: Posil serce twoje trochą chleba, a potem pójdziecie.
Tsiku lachinayi anadzuka mʼmamawa kukonzekera kuti azipita kwawo, koma abambo ake a mtsikanayo anawuza mkamwini wawo uja kuti, “Yambani mwadya chakudya, ndipo kenaka mutha kupita.”
6 Tedy siedli i jedli oboje wespół, i napili się. Zatem rzekł ojciec onej dziewki do męża jej: Zostań proszę, a przenocuj tu, i bądź dobrej myśli.
Choncho onse awiri anakhala pansi ndi kudya ndi kumwa pamodzi. Atadya, abambo a mtsikanayo anati, “Chonde mugonenso konkuno musangalale.”
7 A gdy wstał on mąż, chcąc przecię iść w drogę, gwałtem przymusił go świekier jego, iż się wróciwszy został tam na noc.
Ndipo pamene mwamunayo anakonzeka kuti azipita, apongozi ake anamuwumirizanso kuti asapite. Choncho anagona komweko usiku umenewo.
8 Wstał potem bardzo rano dnia piątego, chcąc iść; ale mówił ojciec onej dziewki: Posil proszę serce twoje; i zabawili się, aż się dzień nachylił, a jedli oba społu.
Mmawa wa tsiku lachisanu, atadzuka kuti azipita abambo ake a mtsikanayo anamuwuza kuti, “Yambani mwadya chakudya ndipo mutandale mpaka madzulo.” Choncho awiriwo anadya pamodzi.
9 Wstał tedy on mąż, aby szedł sam i założnica jego, i sługa jego, któremu rzekł świekier jego, ojciec onej dziewki: Oto się już dzień nachylił ku wieczorowi, przenocujcież tu proszę; oto schodzi dzień, przenocuje tu, a bądź dobrej myśli, a jutro rano wyprawicie się w drogę swą, i pójdziesz do przybytku twego.
Pambuyo pake munthu uja pamodzi ndi mzikazi wake ndiponso mtumiki anakonzeka kuti azipita. Koma abambo a mtsikana uja anatinso kwa iye, “Onani tsopano kukuda. Gonani konkuno pakuti tsiku latha kale. Gonani ndipo musangalale. Mawa mudzuka mʼmamawa ndi kumapita kwanu.”
10 Tedy on mąż nie chciał zostać na noc, ale wstał i odszedł, a przyszedł aż ku Jebus, (które jest Jeruzalem) mając z sobą dwóch osłów z brzemiony, i założnicę swoję.
Koma munthuyo sanafune kugonanso tsiku limenelo. Choncho ananyamuka kumapita, ndipo anakafika ku malo oyangʼanana ndi Yebusi (ndiye kuti Yerusalemu). Iyeyo anali atatenga abulu ake awiri okhala ndi zokhalira zake, ndipo mzikazi wake uja anali naye limodzi.
11 A gdy byli blisko Jebus, a dzień się już bardzo nachylił, tedy rzekł sługa do pana swego: Pójdź proszę, a wstąpmy do tego miasta Jebuzejczyków, i przenocujmy w niem.
Akuyandikira ku Yebusi nʼkuti kutada ndithu. Tsono mtumiki uja anawuza mbuye wake kuti, “Tiyeni, tipatukire ku mzinda wa Ayebusiwa ndipo tigone.”
12 Któremu odpowiedział pan jego: Nie wstępujmy do miasta cudzoziemców, które nie jest z synów Izraelskich, ale idźmy aż do Gabaa.
Mbuye wake anamuyankha kuti, “Ayi, tisapatukire ku mzinda wa alendo, anthu amene sali Aisraeli. Koma tipitirire mpaka ku Gibeya.”
13 Nadto rzekł do sługi swego: Pójdź, abyśmy przyszli na jedno z tych miejsc, i przenocowali albo w Gabaa albo w Rama.
Tsono anamuwuza mtumiki wake uja kuti, “Tiye tipite ku amodzi a malo awa, ku Gibeya kapena ku Rama ndipo tikagone kumeneko.”
14 A minąwszy poszli: i zaszło im słońce u Gabaa, które jest pokolenia Benjaminowego.
Choncho nayenda ulendo wawo, ndipo dzuwa linawalowera akuyandikira ku Gibeya mʼdziko la Benjamini.
15 I udali się tam, aby wszedłszy przenocowali w Gabaa; a gdy wszedł, usiadł na ulicy w mieście, przeto że nie był, kto by je przyjął w dom i przenocował.
Ndipo anapatukira kumeneko kuti alowe mu mzinda wa Gibeya kukagona usiku umenewo. Anakalowa mu mzindamo ndi kukakhala pabwalo popeza panalibe munthu amene anawalandira ku nyumba kwake kuti akagone.
16 A oto, mąż stary szedł od roboty swojej z pola w wieczór; a ten mąż był z góry Efraim, będąc przychodniem w Gabaa, ale ludzie miejsca onego byli synowie Jemini.
Pambuyo pake anangoona munthu wina wokalamba akuchokera ku ntchito ya ku munda kwake madzulo. Iyeyu anali wa ku dziko la mapiri ku Efereimu, koma ankakhala ku Gibeya. Koma anthu a kumeneko anali a fuko la Benjamini.
17 Ten podniósłszy oczy swe ujrzał męża onego podróżnego na ulicy miasta, i rzekł do niego starzec: Dokąd idziesz, i skądeś przyszedł?
Munthu wokalamba uja anakweza maso ndipo anaona munthu wa paulendo uja atakhala pabwalo la mzindawo, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukupita kuti? Nanga mukuchokera kuti?”
18 Któremu on odpowiedział: Idziemy z Betlehem Juda aż ku stronie góry Efraimowej, skądem jest; bom chodził do Betlehem Judskiego; a teraz idę do domu Pańskiego, ale nie masz nikogo, coby mię przyjął w dom;
Iye anayankha kuti, “Tikuchokera ku Betelehemu ku dziko la Yuda ndipo tikupita kutali ku dziko lamapiri la Efereimu kumene ndimakhala. Ndinapita ku Betelehemu mʼdziko la Yuda ndipo tsopano ndikubwerera kwathu. Koma palibe aliyense amene wanditengera ku nyumba yake.
19 Choć i plewy i siano mam dla osłów naszych, także chleb i wino mam dla siebie i dla służebnicy twej i dla sługi, który jest ze mną, sługą twoim; nie mam niedostatku z żadnej rzeczy.
Tili ndi udzu ndi chakudya cha abulu athu. Tilinso ndi buledi ndi vinyo wokwanira ifeyo: ine, mdzakazi wanuyu, ndi mtumiki amene ali nafeyu. Palibe chimene tikusowa.”
20 Tedy mu rzekł on mąż stary: Nie frasuj się; czegoćkolwiek nie dostanie, to ja opatrzę; tylko na ulicy nie zostawaj przez noc.
Munthu wokalambayo anati, “Mtendere ukhale nanu. Ine ndikuthandizani pa zosowa zanu zonse, koma musagone pabwalo usiku uno.”
21 Wwiódł go tedy do domu swego, i dał osłom obrok; potem umywszy nogi swoje, jedli i pili.
Choncho anapita nawo ku nyumba yake, ndipo anawapatsa abulu ake chakudya. Alendo aja anasamba mapazi awo, nalandira chakudya ndi chakumwa.
22 A gdy rozweselili serce swoje, oto, mężowie miasta tego, mężowie niepobożni, obstąpili dom, kołacąc we drzwi, i rzekli do gospodarza domu onego, do męża starego, mówiąc: Wywiedź męża, który wszedł w dom twój, abyśmy go poznali.
Pamene ankadya mosangalala, anangoona anthu ena achabechabe a mu mzindawo azungulira nyumba ija nʼkumamenya chitseko. Tsono anawuza mwini nyumbayo, munthu wokalamba uja kuti, “Mutulutse munthu amene wabwera mʼnyumba yakoyu kuti tigone naye.”
23 A wyszedłszy do nich on mąż, gospodarz domu, rzekł im: Nie tak bracia moi: nie czyńcie proszę tej złości, gdyż wszedł ten mąż do domu mego, nie czyńcież tej sprosności.
Koma mwini nyumba uja anatuluka ku bwalo nawawuza kuti, “Ayi, abale anga musachite zoyipa zotere. Popeza munthu uyu walowa mʼnyumba mwanga muno, musachite chinthu chonyansa chotere.
24 Oto córka moja panna, i założnica jego, wywiodę je zaraz, że je obelżycie, a uczynicie z niemi, co się wam będzie dobrego zdało; tylko mężowi temu nie czyńcie tej zelżywości.
Onani, pano pali mwana wanga wamkazi wosadziwa mwamuna pamodzi ndi mzikazi wa mlendoyu. Ndikutulutsirani amenewa tsopano ndipo atengeni ndi kuchita nawo chomwe chikukomerani. Koma musachite chinthu chonyansa ndi munthuyu.”
25 Ale nie chcieli oni mężowie słuchać głosu jego; przetoż wziąwszy on mąż założnicę swoję, wywiódł ją do nich na dwór; i poznali ją, a czynili jej gwałt przez całą noc aż do zaranku, a potem puścili ją, gdy wschodziła zorza.
Koma anthuwo sanafune kumumvera. Choncho mlendo uja anagwira mzikazi wake namutulutsa kuja kumene kunali iwo. Tsono iwowo anagona naye ndi kuchita naye zonyansa usiku wonse mpaka mmawa. Mʼbandakucha anamulola kuti apite.
26 A przyszedłszy ona niewiasta na świtaniu, upadła u drzwi domu onegoż męża, gdzie był pan jej, aż się rozedniało.
Ndipo mmawa kukucha mzikazi uja anabwerera nakagwa pansi pa khomo pa nyumba imene mwamuna wake anali, ndipo anakhala pomwepo mpaka kunayera.
27 Potem wstawszy pan jej rano, otworzył drzwi u domu, i wyszedł, chcąc iść w drogę swoję, a oto, ona niewiasta, założnica jego, leżała u drzwi domu, a ręce jej był na progu.
Mwamuna wake anadzuka mʼmamawa, natsekula chitseko cha nyumba kuti atuluke ndi kumapita. Koma anangoona mzikazi wake uja ali thapsa pa khomo la nyumbayo, manja ake ali pa khonde.
28 I rzekł do niej: Wstań a pójdźmy; ale nic nie odpowiedziała. Wziąwszy ją tedy na osła, wstał on mąż, i szedł do miejsca swego.
Iye anati kwa mkaziyo, “Dzuka tizipita.” Koma sanayankhe kanthu. Kenaka anamukweza pa bulu wake ndipo ananyamuka kumapita kwawo.
29 Tam przyszedłszy w dom swój, porwał miecz, a zdjąwszy założnicę swoję rozrąbał ją z kościami jej na dwanaście sztuk, i rozesłał ją po wszystkich granicach Izraelskich.
Atafika ku nyumba yake, anatenga mpeni, nagwira mzikazi wake uja ndi kuduladula thupi lake nthuli khumi ndi ziwiri. Kenaka anazitumiza ku zigawo zonse za Israeli.
30 A ktokolwiek to widział, mówił: Nigdy się to nie stało, ani co takowego widziano od onego dnia, jako wyszli synowie Izraelscy z ziemi Egipskiej, aż do tego dnia; uważajcież to z pilnością, a radźcie i mówcie o tem.
Aliyense amene anaona zimenezi ankanena kuti, “Zoterezi sizinaonekepo kuyambira pamene Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ganizirani bwino chinthu chimenechi ndipo tiwuzeni zoyenera kuchita!”

< Księga Sędziów 19 >