< Księga Sędziów 14 >

1 Szedł tedy Samson do Tamnaty, a ujrzał tam niewiastę z córek Filistyńskich.
Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
2 A przyszedłszy oznajmił ojcu swemu i matce swojej, mówiąc; Niewiastem widział w Tamnacie z córek Filistyńskich; przetoż teraz weźmijcie mi ją za żonę.
Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
3 I rzekł mu ojciec jego, i matka jego; Azaż nie masz między córkami braci twych, i we wszystkim ludu moim niewiasty, że chcesz iść a wziąć sobie żonę z Filistynów nieobrzezanych? Odpowiedział Samson ojcu swemu: Tę mi weźmijcie, bo się podobała oczom moim.
Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
4 A ojciec jego i matka jego nie wiedzieli, że to było od Pana; bo on przyczyny szukał na Filistyny, gdy na on czas Filistyni panowali nad Izraelem.
(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
5 Tedy szedł Samson z ojcem swym i z matką swoją do Tamnaty, a przychodząc ku winnicom Tamnaty, oto, lew młody ryczący zabieżał mu.
Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
6 I przypadł nań Duch Pański, a rozdarł go, jakoby rozdarł koźlę, choć nic nie miał w rękach swych; i nie oznajmił ojcu swemu i matce swojej, co uczynił.
Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
7 Przyszedłszy tedy mówił z oną niewiastą, a podobała się oczom Samsonowym.
Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
8 A wróciwszy się po kilku dniach, aby ją pojął, zstąpił, aby oglądał on ścierw lwi, a oto, rój pszczół był w ścierwie lwim, i miód.
Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
9 A wziąwszy go w ręce swoje szedł drogą i jadł, a przyszedłszy do ojca swego i do matki swojej, dał im, i jedli; ale im nie powiedział, że z ścierwu lwiego nabrał miodu.
Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
10 tedy szedł ojciec jego do onej niewiasty, i sprawił tam Samson wesele; bo tak czyniwali młodzieńcy.
Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
11 A gdy go ujrzeli Filistyni, wzięli trzydzieści towarzyszów, aby byli przy nim.
Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
12 Do których rzekł Samson: Zadam wam zagadkę, a jeźli ją zgadniecie przez siedem dni wesela i wyłożycie mi ją, tedy wam dam trzydzieści prześcieradeł, i trzydzieści szat odmiennych.
Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
13 A jeźliż mi jej nie zgadniecie, tedy wy mnie dacie trzydzieści prześcieradeł, i trzydzieści szat odmiennych; którzy mu odpowiedzieli: Zadaj zagadkę twoję; a będziemy jej słuchali.
Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
14 I rzekł do nich: Z pożerającego wyszedł pokarm, a z mocnego wyszła słodkość; i nie mogli zgadnąć onej zagadki przez trzy dni.
Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
15 I rzekli dnia siódmego do żony Samsonowej: Namów męża twego, aby nam powiedział zagadkę, byśmy snać nie spalili ciebie, i domu ojca twego ogniem; na tożeście nas wezwali, abyście posiedli majętność naszę, czy nie na to?
Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
16 Płakała tedy żona Samsonowa nań, mówiąc: Zaprawdę mię masz w nienawiści, a nie miłujesz mię; zadałeś zagadkę synom ludu mego, a nie chcesz mi jej oznajmić. I rzekł do niej: Otom jej ojcu memu i matce mojej nie oznajmił, a tobie bym miał oznajmić?
Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
17 I płakała nań przez one siedem dni, póki mieli wesele. Stało się tedy dnia siódmego, że jej oznajmił, bo mu się uprzykrzała. A ona powiedziała onę zagadkę synom ludu swego.
Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
18 Przetoż rzekli do niego mężowie onego miasta siódmego dnia przed zachodem słońca: Cóż słodszego nad miód, a co mocniejszego nad lwa? którym on odpowiedział: Byście byli nie orali jałowicą moją, nie zgadlibyście byli zagadki mojej.
Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
19 I przypadł nań Duch Pański, a szedłszy do Aszkalonu, zabił z nich trzydzieści mężów a wziąwszy łupy z nich, dał szaty odmienne onym, którzy zgadli zagadkę, i rozgniewawszy się bardzo poszedł do domu ojca swego.
Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
20 I dostała się żona Samsonowa towarzyszowi jego, z którym miał towarzystwo.
Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

< Księga Sędziów 14 >