< Księga Sędziów 13 >

1 Potem znowu synowie Izraelscy czynili złe przed oczyma Pańskiemi, i podał je Pan w ręce Filistynów przez czterdzieści lat.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
2 Tedy był mąż niektóry z Saraa, z pokolenia Dan, imieniem Manue, a żona jego była niepłodną, i nie rodziła.
Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
3 I ukazał się Anioł Pański onej niewieście, a rzekł do niej: Otoś teraz niepłodną, aniś rodziła; ale poczniesz i porodzisz syna.
Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
4 Przetoż się teraz strzeż, abyś nie piła wina, i napoju mocnego, i abyś nie jadła nic nieczystego;
Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
5 Bo oto poczniesz i porodzisz syna, a brzytwa nie postoi na głowie jego, bo Nazarejczykiem Bożym będzie to dziecię zaraz z żywota; a on pocznie wybawiać Izraela z ręki Filistynów.
chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
6 Tedy przyszła niewiasta, i powiedziała to mężowi swemu, mówiąc: Mąż Boży przyszedł do mnie, którego oblicze było jako oblicze Anioła Bożego, bardzo straszne, i nie pytałam go, skąd był, ani mi imienia swego oznajmił.
Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
7 Tylko mi rzekł: Oto, poczniesz i porodzisz syna; przetoż teraz nie pij wina, ani napoju mocnego, ani jedz co nieczystego; bo Nazarejczykiem Bożym będzie to dziecię zaraz z żywota aż do dnia śmierci swojej.
Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
8 Tedy się modlił Manue Panu, mówiąc: Proszę Panie mój, mąż Boży, któregoś posłał, niech przyjdzie proszę znowu do nas, a nauczy nas, co czynić mamy z dziecięciem, które się narodzi?
Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
9 I wysłuchał Bóg głos Manuego; bo przyszedł Anioł Boży znowu do niewiasty onej, gdy siedziała na polu; ale Manue, mąż jej, nie był z nią.
Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
10 Tedy kwapiąc się ona niewiasta, bieżała, i opowiedziała mężowi swemu, i rzekła mu: Oto mi się ukazał mąż on, który był przyszedł przedtem do mnie.
Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
11 A wstawszy Manue szedł za żoną swoją; a przyszedłszy do onego męża, rzekł mu: Tyżeś jest ten mąż, któryś mówił z żoną moją? A on rzekł: Jam jest.
Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
12 I rzekł Manue: Niech się teraz spełni słowo twoje; ale cóż będzie za obyczaj dziecięcia, i co za sprawa jego?
Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
13 I odpowiedział Anioł Pański Manuemu: Wszystkiego, com powiedział żonie twojej, niech się strzeże.
Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
14 Żadnej rzeczy, która pochodzi z winnej macicy, niechaj nie je; także wina ani napoju mocnego, niech nie pije, ani żadnej rzeczy nieczystej niech nie je, a com jej kolwiek przykazał, tego niech przestrzega.
Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
15 Tedy rzekł Manue do Anioła Pańskiego: Daj się proszę zatrzymać, a nagotujemy przed cię koźlątko z stada.
Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
16 Ale Anioł Pański odpowiedział Manuemu: Choćbyś mię zatrzymał, nie będę jadł chleba twego; ale jeźli będziesz chciał sprawić całopalenie, ofiarujże je Panu; bo nie wiedział Manue, żeby on był Anioł Pański.
Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
17 Tedy rzekł Manue do Anioła Pańskiego: Cóż za imię twoje? abyśmy, gdy się spełni słowo twoje, uczcili cię.
Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
18 Któremu odpowiedział Anioł Pański: Przeczże pytasz o imię moje, które jest dziwne?
Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
19 Wziął tedy Manue koźlę z stada, i ofiarę śniedną, i ofiarował to na opoce Panu, i uczynił cud, a Manue i żona jego patrzyli na to.
Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
20 A gdy wstępował płomień z ołtarza ku niebu, tedy wstąpił Anioł Pański w płomieniu ołtarzowym, a Manue, i żona jego widząc to, upadli na twarze swe na ziemię.
Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
21 A potem nie ukazał się więcej Anioł Pański Manuemu, ani żonie jego; i poznał Manue, że to był Anioł Pański.
Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
22 I rzekł Manue do żony swojej: Koniecznie pomrzemy, bośmy Boga widzieli.
Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
23 Któremu odpowiedziała żona jego: Gdyby nas chciał Pan zabić, nie przyjąłby z rąk naszych całopalenia, i ofiary śniednej, aniby nam był okazał tego wszystkiego, aniby nam na ten czas był objawił takowych rzeczy.
Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
24 Porodziła tedy ona niewiasta syna, i nazwała imię jego Samson; i rosło dziecię, a błogosławił mu Pan.
Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
25 I począł go Duch Pański umacniać w obozie Dan między Saraa i między Estaol.
Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.

< Księga Sędziów 13 >