< Księga Sędziów 11 >

1 Ale Jefte Galaadczyk był człowiekiem bardzo mężnym, a był synem niewiasty nierządnej, z którą spłodził Galaad tegoż Jeftego.
Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
2 Ale i żona Galaadowa narodziła mu synów; a dorósłszy synowie tej żony, wygnali Jeftego, mówiąc mu: Nie będziesz brał dziedzictwa w domu ojca naszego, boś ty jest synem inszej niewiasty.
Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
3 Uciekł tedy Jefte przed bracią swoją, a mieszkał w ziemi Tob: i zebrali się do niego ludzie ogołoceni, i poszli z nim.
Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
4 I stało się potem, że walczyli synowie Ammonowi z Izraelem.
Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
5 A gdy poczęli walczyć Ammonitowie z Izraelem, tedy poszli starsi z Galaad, aby wzięli Jeftego z ziemi Tob.
Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
6 I rzekli do niego: Pójdź, a bądź nam za hetmana, a będziemy walczyli przeciwko synom Ammonowym.
Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
7 Ale Jefte odpowiedział starszym Galaad: Izażeście wy mnie nie mieli w nienawiści, i wygnaliście mię z domu ojca mego? przeczżeście przyszli teraz do mnie, gdy ucisk przyszedł na was?
Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
8 Tedy rzekli starsi z Galaad do Jeftego: Dla tegośmy się teraz wrócili do ciebie, abyś szedł z nami, a walczył przeciwko synom Ammonowym, a był nam za hetmana, wszystkim mieszkającym w Galaad.
Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
9 I odpowiedział Jefte starszym z Galaad: Ponieważ wy mnie przywracacie, a chcecie, abym walczył przeciwko synom Ammonowym, a jeźli mi je poda Pan, będęż wam za hetmana?
Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
10 I rzekli starsi z Galaad do Jeftego: Pan będzie świadkiem między nami, jeźliż tak według słowa twego nie uczynimy.
Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
11 Tedy szedł Jefte z starszymi z Galaad, i postanowił go lud hetmanem i książęciem nad sobą; i mówił Jefte wszystkie te słowa przed Panem w Masfa.
Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
12 Potem wyprawił Jefte posły do króla synów Ammonowych, mówiąc: Co ja mam z tobą, żeś przyciągnął na mię, abyś walczył przeciwko ziemi mojej?
Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
13 Na co odpowiedział król synów Ammonowych posłom Jeftego: Że wziął Izrael ziemię moję, gdy szedł z Egiptu, od Arnon aż do Jabok i aż do Jordanu: przetoż teraz wróć mi ją w pokoju.
Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
14 Po wtóre jeszcze Jefte wyprawił posły do króla synów Ammonowych.
Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
15 I rzekł mu: Tak mówi Jefte: Nie wziął Izrael ziemi Moabskiej, ani ziemi synów Ammonowych.
kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
16 Ale gdy z Egiptu szedł Izrael przez puszczą aż ku morzu czerwonemu, a przyszedł do Kades.
Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
17 Skąd wyprawił Izrael posły do króla Edomskiego, mówiąc: Proszę niech przejdę przez ziemię twoję, i nie pozwolił król Edomski, także i do króla Moabskiego posłał, i nie pozwolił; a tak został Izrael w Kades.
Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
18 A gdy szedł przez puszczą, obszedł ziemię Edomską, i ziemię Moabską, a przyszedł od wschodu słońca ziemi Moabskiej, i położyli się obozem za Arnon, a nie wszedł w granice Moabskie; bo Arnon jest granicą Moabską.
“Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
19 Dlategoż wyprawił Izrael posły do Sehona, króla Amorejskiego, króla w Hesebon, i rzekł mu Izrael: Niech przejdę proszę przez ziemię twoję aż do miejsca mego.
“Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
20 Ale nie dowierzał Sehon Izraelowi, aby iść miał przez granicę jego; owszem zebrał Sehon wszystek lud swój, i położył się obozem w Jasa, i zwiódł bitwę z Izraelem.
Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
21 I dał Pan, Bóg Izraelski, Sehona, i wszystek lud jego w ręce Izraelowe, i poraził je, a posiadł Izrael wszystkę ziemię Amorejczyka, który mieszkał w onej ziemi.
“Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
22 A tak posiedli wszystkie granice Amorejskie od Arnon aż do Jabok, a od puszczy aż do Jordanu.
Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
23 Ponieważ tedy Pan, Bóg Izraelski wypędził Amorejczyka przed ludem swym Izraelskim, przecz ty chcesz panować nad nim?
“Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
24 Azaż, coć dał posieść Kamos, bóg twój, tego nie posiędziesz? tak, kogo Pan, Bóg nasz, wygnał przed oblicznością naszą, tego też dziedzictwo posiadamy.
Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
25 Do tego czemżeś ty lepszy nad Balaka syna Seferowego, króla Moabskiego? zaż się on kiedy wadził z Izrealem? zaż kiedy walczył przeciwko niemu?
Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
26 Oto przez trzy sta lat mieszkał Izrael w Hesebon, i we wsiach jego, także w Aroer, i we wsiach jego, i we wszystkich miastach, które są przy granicy Arnon; czemużeście ich nie odjęli przez ten czas?
Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
27 A tak nie jam tobie winien, ale ty mnie źle czynisz, że walczysz przeciwko mnie; niech Pan, który jest Sędzią, rozsądzi dziś między syny Izraelskimi i między syny Ammonowymi.
Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
28 Ale nie usłuchał król synów Ammonowych słów Jeftego, które wskazał do niego.
Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
29 I był nad Jeftem duch Pański, a przeszedł przez Galaad, i przez Manase; przeszedł też przez Masfa w Galaad, a z Masfy w Galaad ciągnął przeciw synom Ammonowym.
Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
30 Tamże uczynił Jefte ślub Panu, mówiąc: Jeźli pewnie podasz syny Ammonowe w ręce moje,
Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
31 Tedy to, cobykolwiek wyszło ze drzwi domu mego przeciwko mnie, gdy się wrócę w pokoju od synów Ammonowych, to mówię będzie Panu, albo ofiarować je będę na całopalenie.
aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
32 A tak Jefte ciągnął przeciwko synom Ammonowym, aby walczył z nimi, i podał je Pan w ręce jego.
Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
33 I poraził je od Aroer aż idąc do Menit, dwadzieścia miast, i aż do równiny winnic porażką bardzo wielką, a poniżeni są synowie Ammonowi przed syny Izraelskimi.
Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
34 A gdy się wracał Jefte do Masfa do domu swego, oto, córka jego wyszła przeciw niemu, z bębny, i z muzyką; a ta była jedynaczka, bo nie miał żadnego syna ani innej córki.
Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
35 I stało się, gdy ją ujrzał, rozdarł odzienie swoje, i rzekł: Ach, córko moja, bardzoś mię poniżyła! i tyś jest z tych, którzy mię frasują, gdyżem ślub uczynił Panu, a nie będę mógł odmienić.
Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
36 Któremu ona odpowiedziała: Ojcze mój, uczyniłeś ślub Panu, uczyńże ze mną tak, jakoś wyrzekł usty twojemi, gdyć tylko dał Pan pomstę nad nieprzyjacioły twemi, nad syny Ammonowymi.
Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
37 Nadto rzekła do ojca swego: To mi tylko uczyń: puść mię na dwa miesiące, że pójdę a wstąpię na góry i opłakiwać będę panieństwo moje, ja i towarzyszki moje.
Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
38 A on rzekł: Idź; i puścił ją na dwa miesiące. Poszła tedy ona i towarzyszki jej, a opłakiwała panieństwo swoje na górach.
Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
39 A gdy wyszły dwa miesiące, wróciła się od ojca swego, i wypełnił nad nią ślub swój, który był uczynił; a tak ona nie poznała męża. I weszło to w zwyczaj w Izraelu,
Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
40 Iż na każdy rok schodziły się córki Izraelskie aby się rozmawiały z córką Jeftego Galaadczyka, przez cztery dni w rok.
kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.

< Księga Sędziów 11 >