< Jozuego 9 >

1 A gdy usłyszeli wszyscy królowie, którzy byli za Jordanem na górach, i na równinach, i nad wszystkiem brzegiem morza wielkiego przeciw Libanowi, Hetejczyk, i Amorejczyk, i Chananejczyk, Ferezejczyk, Hewejczyk, i Jebuzejczyk;
Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
2 Zebrali się pospołu, aby walczyli przeciw Jozuemu, i przeciw Izraelowi, jednomyślnie.
anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
3 Ale obywatele Gabaon, usłyszawszy, co uczynił Jozue Jerychowi i Hajowi,
Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
4 Postąpili sobie i oni chytrze, a poszedłszy zmyślili się być posłami, i wzięli wory stare na osły swe, i łagwie winne stare, i potarte, i łatane;
anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
5 I obuwie stare i łatane na nogi swoje, i szaty stare na się, a wszystek chleb, co go z sobą nabrali w drogę, suchy był i spleśniały.
Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
6 Tedy przyszli do Jozuego, do obozu w Galgal, i rzekli do niego, i do mężów Izraelskich: Z ziemiśmy dalekiej przyszli; przetoż teraz uczyńcie z nami przymierze.
Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
7 Ale odpowiedzieli mężowie Izraelscy Hewejczykowi: Podobno ty mieszkasz między nami, a jakoż z tobą możemy uczynić przymierze?
Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
8 A oni rzekli do Jozuego: Słudzy twoi jesteśmy. I rzekł do nich Jozue: Coście wy zacz, a skądeście przyszli?
Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
9 I odpowiedzieli mu: Z ziemi dalekiej bardzo przyszli słudzy twoi w imieniu Pana, Boga twego; bośmy słyszeli sławę jego, i wszystko, co uczynił w Egipcie;
Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
10 I wszystko, co uczynił dwom królom Amorejskim, którzy byli za Jordanem, Sehonowi królowi Hesebon, i Ogowi królowi Basan, którzy mieszkali w Astarot.
ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
11 I rozkazali nam starsi nasi, i wszyscy obywatele ziemi naszej, mówiąc: Nabierzcie sobie żywności na drogę, a idźcie przeciwko nim, i mówcie im: Słudzy wasi jesteśmy, przetoż teraz uczyńcie z nami przymierze.
Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
12 Ten chleb nasz ciepłyśmy na drogę wzięli z domów naszych tego dnia, gdyśmy wyszli, abyśmy szli do was; a teraz oto wysechł, i popleśniał.
Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
13 I te łagwie winne, któreśmy byli napełnili, były nowe, a oto się popękały; także te szaty nasze, i obuwie nasze zwiotszały dla bardzo dalekiej drogi.
Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
14 A tak wzięli oni mężowie Izraelscy z onej żywności ich, a ust się Pańskich nie pytali.
Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
15 Tedy z nimi uczynił Jozue pokój, i postanowił z nimi przymierze, aby ich zachował przy żywocie; także przysięgły im książęta zgromadzenia.
Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
16 Ale po trzech dniach po uczynieniu z nimi przymierza, usłyszeli, że blisko ich byli, a iż w pośrodku ich mieszkali.
Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
17 A ruszywszy się synowie Izraelscy przyciągnęli do miast ich dnia trzeciego, a miasta ich te były: Gabaon, i Kafira, i Beerot, i Karyjatyjarym.
Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
18 I nie wytracili ich synowie Izraelscy; albowiem przysięgły im były książęta zgromadzenia przez Pana, Boga Izraelskiego, skąd szemrało wszystko zgromadzenie przeciw książętom.
Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
19 I rzekły wszystkie książęta do całego zgromadzenia: Myśmy im przysięgli przez Pana, Boga Izraelskiego; przetoż teraz nie możemy się ich tknąć.
Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
20 To im uczynimy, a zachowamy je żywo, iżby nie przyszło na nas rozgniewanie dla przysięgi, którąśmy im przysięgli.
Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
21 Nadto rzekły do nich książęta: Niech żyją, a niech rąbią drwa, i niech noszą wodę wszystkiemu zgromadzeniu; i przestali na tem, jako im powiedziały książęta.
Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
22 Potem wezwał ich Jozue, i rzekł do nich, mówiąc: Przeczżeście nas oszukali, powiadając: Dalekimiśmy od was bardzo, a wy w pośrodku nas mieszkacie?
Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
23 A tak teraz przeklęci jesteście, i nie ustaną z was słudzy, i rąbiący drwa, i noszący wodę do domu Boga mego.
Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
24 Którzy odpowiedzieli Jozuemu, i rzekli: Zapewne oznajmiono było sługom twoim, jako był rozkazał Pan, Bóg twój, Mojżeszowi słudze swemu, aby wam dał wszystkę ziemię, a iżby wygładził wszystkie mieszkające w tej ziemi przed twarzą waszą; przetoż baliśmy się bardzo o żywot nasz przed wami, i uczyniliśmy tę rzecz.
Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
25 A teraz otośmy w rękach twoich; coć się dobrego i słusznego widzi uczynić z nami, uczyń.
Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
26 I uczynił im tak, a wybawił je z rąk synów Izraelskich, że ich nie pobili.
Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
27 I postanowił je Jozue dnia onego, aby rąbali drwa, i nosili wodę zgromadzeniu, i do ołtarza Pańskiego aż do tego dnia, na miejscu, które by obrał.
Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.

< Jozuego 9 >