< Jozuego 8 >

1 Potem rzekł Pan do Jozuego: Nie bój się, ani się lękaj; weźmij z sobą wszystek lud wojenny, a wstawszy ciągnij do Haj, otom dał w ręce twoje króla Haj, i lud jego, i ziemię jego.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
2 A uczynisz Hajowi i królowi jego, jakoś uczynił Jerychu i królowi jego, wszakże łupy jego, i bydła jego rozbierzecie między się; uczyńże zasadzkę na miasto z tyłu jego.
Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
3 A tak wstał Jozue i wszystek lud waleczny, aby ciągnęli ku Haj; i przebrał Jozue trzydzieści tysięcy mężów bardzo mocnych, i posłał je nocą.
Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
4 I rozkazał im, mówiąc: Patrzajcie wy, abyście uczynili zasadzkę za miastem; nie oddalajcie się od miasta daleko bardzo, a bądźcie wszyscy pogotowiu.
nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
5 A ja, i wszystek lud, który ze mną jest, przyciągniemy pod miasto; a gdy oni wynijdą przeciwko nam, jako pierwej ucieczemy przed nimi.
Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
6 A oni pójdą za nami, aż je uwiedziemy od miasta; bo rzeką: Uciekają przed nami, jako i pierwej, gdyż uciekać będziemy przed nimi.
Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
7 Tedy wy wstaniecie z zasadzki, i wyprzecie ostatek ludu z miasta, i da je Pan, Bóg wasz, w rękę waszę.
inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
8 A wziąwszy miasto, zapalicie je ogniem, według słowa Pańskiego uczynicie; patrzajcież, rozkazałem wam.
Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
9 Posłał je tedy Jozue, i szli na zasadzkę; a zostali między Betel, i między Haj na zachód Hajowi; a Jozue przez onę noc został w pośrodku ludu.
Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
10 Potem wstawszy Jozue bardzo rano, obliczył lud, a szedł sam i starsi z Izraela przed ludem przeciw Haj.
Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
11 Wszystek też lud wojenny, który z nim był, ruszyli się, i przyciągnąwszy przyszli pod miasto, i położyli się obozem na stronie północnej ku Haj; a była dolina między nim, i między Haj.
Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
12 Nadto wziął około pięciu tysięcy mężów, które postawił na zasadzce między Betel, i między Haj, od strony zachodniej miasta.
Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
13 I przybliżył się lud, to jest, wszystko wojsko, które było od północy miasta, i którzy byli na zasadzce jego od zachodu miasta; i przyciągnął Jozue onej nocy w pośrodek doliny.
Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
14 I stało się, gdy je ujrzał król Haj, pospieszyli się i wstali rano, i wyszli ludzie z miasta przeciw Izraelowi ku bitwie, sam król, i wszystek lud jego, na czas naznaczony przed równinę, nie wiedząc, że zasadzka była uczyniona nań za miastem.
Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
15 Tedy Jozue i wszystek Izrael, jakoby od nich porażeni, uciekali drogą ku puszczy.
Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
16 I zwołany jest wszystek lud, który był w mieście, aby je gonili, i gonili Jozuego; i tak uwiedzieni byli od miasta.
Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
17 I nie został nikt w Haj i w Betel, któryby nie wyszedł za Izraelem; i zostawili miasto otworzone, a gonili Izraela.
Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
18 Tedy rzekł Pan do Jozuego: Podnieś chorągiew, którą masz w ręce swej, przeciwko Haj; bo je w ręce twoje dam. I podniósł Jozue chorągiew, którą miał w ręce swej, przeciwko miastu.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
19 A oni, co byli na zasadzce, wstawszy prędko z miejsca swego; bieżali, gdy on podniósł rękę swą, a ubieżawszy miasto, wzięli je, i zaraz je zapalili ogniem.
Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
20 A obejrzawszy się mężowie miasta Haj ujrzeli, a oto, wstępował dym miasta ku niebu, i nie mieli miejsca do uciekania, ani tam, ani sam; bo lud, który uciekał ku puszczy, obrócił się na one, co je gonili.
Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
21 Tedy Jozue i wszystek lud Izraelski, widząc, iż oni, co byli na zasadzce, wzięli miasto, a iż wychodził dym z miasta, obrócili się i pobili męże miasta Haj.
Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
22 Oni też drudzy wyszli z miasta przeciwko nim, i obtoczyli je Izraelczycy, jedni stąd, a drudzy zowąd, i porazili je tak, iż z nich żaden nie został, ani uszedł.
Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
23 Tamże króla Haj pojmali żywo, i przywiedli go przed Jozuego.
kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
24 Gdy tedy Izraelczycy pobili wszystkie obywatele Haj na polu przy puszczy, tedy za nimi szli w pogoń, a polegli oni wszyscy od miecza, aż wygładzeni są; obrócili się wszyscy Izraelczycy do Haj, i wysiekli je ostrzem miecza.
Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
25 I było wszystkich, którzy polegli dnia onego, od męża aż do niewiasty dwanaście tysięcy, wszystkich obywateli Haj.
Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
26 A Jozue nie spuścił ręki swej, którą był podniósł z chorągwią, aż pobił wszystkie obywatele Haj.
Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
27 Tylko bydło, i łupy miasta onego rozebrali między się Izraelczycy według słowa Pańskiego, które rozkazał Jozuemu.
Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
28 Tedy zapalił Jozue Haj, i uczynił je mogiłą wieczną, i pustynią aż do dnia tego.
Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
29 A króla Haj obwiesił na drzewie aż do wieczora; a gdy słońce zaszło, rozkazał Jozue, aby zdjęto trupa jego z drzewa, a porzucono go w samem wejściu bramy miejskiej, i namiotali nań kupę wielką kamieni, która jest aż do dnia tego.
Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
30 Tedy Jozue zbudował ołtarz Panu, Bogu Izraelskiemu, na górze Hebal.
Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
31 Jako był rozkazał Mojżesz, sługa Pański, synom Izraelskim, a jako napisano w księgach zakonu Mojżeszowego, ołtarz z całego kamienia, na którym żadne żelazo nie postało; i sprawowali na nim całopalenia Panu, ofiarowali też spokojne ofiary.
Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
32 Tamże napisał na kamieniach powtórzenie zakonu Mojżeszowego, który napisał przed oblicznością synów Izraelskich.
Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
33 A wszystek Izrael, i starsi jego, i przełożeni, i sędziowie jego, stali po obu stronach skrzyni przed kapłanami Lewitami, którzy nosili skrzynię przymierza Pańskiego, tak przychodzień, jako w domu zrodzony, połowa ich przeciw górze Garyzym, a połowa ich przeciw górze Hebal, jako był przedtem rozkazał Mojżesz, sługa Pański, aby błogosławiono ludowi Izraelskiemu.
Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
34 A potem czytał wszystkie słowa zakonu, błogosławieństwo, i przeklęstwo, według wszystkiego, co napisano w księgach zakonu.
Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
35 Nie było i słowa ze wszystkiego, co rozkazał Mojżesz, czego by nie czytał Jozue przed wszystkiem zgromadzeniem Izraelskiem, przed niewiastami, i przed dziatkami, i przed przychodniami, którzy mieszkali między nimi.
Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.

< Jozuego 8 >