< Jozuego 24 >

1 Tedy zebrał Jozue wszystkie pokolenia Izraelskie do Sychem, i zwołał starszych z Izraela, i przedniejszych z nich, i sędziów ich, i przełożonych ich, i stanęli przed obliczem Bożem.
Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
2 I rzekł Jozue do wszystkiego ludu: Tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Za rzeką mieszkali ojcowie wasi od dawnych czasów, Tare, ojciec Abrahamów, i ojciec Nachorów, i służyli bogom obcym.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
3 I wziąłem ojca waszego Abrahama z miejsca, które jest za rzeką, i prowadziłem go przez wszystkę ziemię Chananejską, i rozmnożyłem nasienie jego, dawszy mu Izaaka.
Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
4 Dałem też Izaakowi Jakóba i Ezawa, a podałem Ezawowi górę Seir, aby ją posiadł; ale Jakób i synowie jego zaszli do Egiptu.
ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
5 I posłałem Mojżesza i Aarona, a trapiłem Egipt; a gdym to uczynił w pośród niego, potemem was wywiódł.
“‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
6 I wywiodłem ojce wasze z Egiptu, a przyszliście aż do morza, i gonili Egipczanie ojce wasze z wozami i z jezdnymi aż do morza czerwonego.
Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
7 Tedy wołali do Pana, a on położył ciemności między wami i między Egipczany, i przywiódł na nie morze, a okryło je; i widziały oczy wasze, com uczynił w Egipcie, i mieszkaliście na puszczy przez długi czas.
Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
8 Potemem przywiódł was do ziemi Amorejczyka, mieszkającego za Jordanem, i walczyli przeciwko wam; alem je podał w rękę waszę, i posiedliście ziemię ich, a wygładziłem je przed wami.
“‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
9 Powstał też Balak, syn Seforów, król Moabski, aby walczył przeciw Izraelowi; a posławszy przyzwał Balaama, syna Beorowego, aby was przeklinał.
Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
10 I nie chciałem słuchać Balaama; przetoż błogosławiąc błogosławił wam, a tak wybawiłem was z rąk jego.
Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
11 Przeprawiliście się potem przez Jordan, i przyszliście do Jerycha, i walczyli przeciwko wam mężowie z Jerycha, Amorejczyk, i Ferezejczyk, i Chananejczyk, i Hetejczyk, i Gargiezejczyk, i Hewejczyk, i Jebuzejczyk; alem je podał w ręce wasze.
“‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
12 I posłałem przed wami sierszenie, którzy je wypędzili przed obliczem waszem, dwu królów Amorejskich, nie mieczem twoim ani łukiem twoim.
Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
13 I dałem wam ziemię, w którejście nie robili, i miasta, którycheście nie budowali, w których mieszkacie, a winnic i oliwnic, którycheście nie sadzili, pożywacie.
Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
14 Przetoż teraz bójcie się Pana, a służcie mu w doskonałości i w prawdzie, a znieście bogi, którym służyli ojcowie wasi za rzeką, i w Egipcie, a służcie Panu.
“Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
15 A jeźli się wam zda źle służyć Panu, obierzcież sobie dziś, komu byście służyli, chociaż bogi, którym służyli ojcowie wasi, co byli za rzeką, chociaż bogi Amorejskie, w których wy ziemi mieszkacie; aleć ja i dom mój będziemy służyli Panu.
Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
16 I odpowiedział lud mówiąc: Nie daj Boże, abyśmy mieli odstąpić Pana, a służyć bogom cudzym:
Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
17 Albowiem Pan, Bóg nasz, on jest, który nas wywiódł, i ojce nasze z ziemi Egipskiej, z domu niewoli, a który uczynił przed oczyma naszemi te znaki wielkie, i strzegł nas we wszystkiej drodze, którąśmy szli, i między wszystkimi narody, przez któreśmy przeszli;
Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
18 I wypędził Pan wszystkie narody, i Amorejczyka mieszkającego w ziemi przed twarzą naszą. A tak my będziemy służyli Panu; bo on jest Bóg nasz.
Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
19 Tedy rzekł Jozue do ludu: Nie możecie wy służyć Panu; bo Bóg święty jest, Bóg zapalczywy jest, nie przepuści złościom waszym, ani grzechom waszym.
Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
20 Jeźliż opuścicie Pana, a będziecie służyli bogom cudzym, obróci się, i utrapi was, i zniszczy was, choć wam przedtem dobrze czynił.
Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
21 I odpowiedział lud Jozuemu: Nie tak; ale Panu służyć będziemy.
Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
22 Tedy rzekł Jozue do ludu: Świadkami będziecie sami przeciwko, sobie, iżeście sobie obrali Pana, abyście mu służyli; a oni rzekli: Świadkami jesteśmy.
Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
23 I rzekł: Terazże znieście bogi cudze, którzy są w pośrodku was, a nakłońcie serca wasze ku Panu, Bogu Izraelskiemu.
Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
24 I odpowiedział lud Jozuemu: Panu, Bogu naszemu, służyć będziemy, i głosowi jego posłuszni być chcemy.
Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
25 A tak uczynił Jozue przymierze z ludem dnia onego, i przełożył im rozkazanie i sąd w Sychem.
Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
26 I napisał Jozue słowa te w księgi Zakonu Bożego; wziął też kamień wielki, i postawił go tam pod dębem, który był u świątnicy Pańskiej.
Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
27 Tedy rzekł Jozue do wszystkiego ludu: Oto kamień ten będzie nam świadectwem; albowiem on słyszał wszystkie słowa Pańskie, które mówił z nami i będzie przeciwko wam na świadectwo, byście snać nie skłamali przeciwko Bogu waszemu.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
28 Zatem rozpuścił Jozue lud, każdego do dziedzictwa swego.
Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
29 I stało się potem, że umarł Jozue, syn Nunów, sługa Pański, we stu i w dziesięciu lat.
Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
30 I pogrzebali go na granicy dziedzictwa jego w Tamnat Sare, które jest na górze Efraim, ku północy góry Gaas.
ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
31 I służył Izrael Panu po wszystkie dni Jozuego, i po wszystkie dni starszych, którzy długo żyli po Jozuem, a którzy wiedzieli o wszystkich sprawach Pańskich, które czynił Izraelowi.
Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
32 Kości też Józefowe, które byli przenieśli synowie Izraelscy z Egiptu, pogrzebali w Sychem, na części pola, które był kupił Jakób od synów Hemora, ojca Sychemowego, za sto jagniąt; i były u synów Józefowych w dziedzictwie ich.
Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
33 Eleazar także, syn Aaronów, umarł; i pogrzebali go na pagórku Fineesa, syna jego, który mu był dany na górze Efraim.
Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.

< Jozuego 24 >