< Jozuego 17 >

1 Padł też los pokoleniu Manasesowemu (bo on jest pierworodny Józefów.) Machyrowi pierworodnemu Manasesowemu, ojcu Galaada, przeto, że był mężem walecznym, i dostał mu się Galaad i Basan.
Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
2 Dostało się też innym synom Manasesowym według domów ich, synom Abiezer, i synom Helek, i synom Esryjel, i synom Sychem, i synom Hefer, i synom Semida. Cić są synowie Manasesowi, syna Józefowego, mężczyzny według domów ich.
Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
3 Ale Salfaad, syn Heferów, syna Galaadowego, syna Machyrowego, syna Manasesowego, nie miał synów, jedno córki, a te imiona córek jego: Machla, i Noa, Hegla, Melcha, i Tersa.
Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
4 Te przyszedłszy przed Eleazara kapłana, i przed Jozuego, syna Nunowego, i przed książęta, rzekły: Pan rozkazał Mojżeszowi, aby nam dał dziedzictwo w pośród braci naszych; i dał im Jozue według rozkazania Pańskiego dziedzictwo w pośrodku braci ojca ich.
Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
5 I przypadło sznurów na Manasesa dziesięć, oprócz ziemi Galaad i Basan, które były za Jordanem.
Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
6 Albowiem córki Manasesowe otrzymały dziedzictwo między syny jego, a ziemia Galaad dostała się drugim synom Manasesowym.
chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
7 I była granica Manasesowa od Aser do Machmatat, które jest przeciwko Sychem, a idzie granica ta po prawej stronie do mieszkających w En Tafua.
Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
8 (Manasesowa była ziemia Tafua; ale Tafua przy granicy Manasesowej była synów Efraimowych.)
(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
9 I bieży ta granica do potoku Kana na południe tegoż potoku; a miasta Efraimitów są między miasty Manasesowemi; ale granica Manasesowa idzie od północy onego potoku, a kończy się u morza.
Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
10 Na południe był dział Efraimów, a na północy Manasesów, a morze jest granica jego; a w pokoleniu Aser schodzą się na północy, a w Isaschar na wschód słońca.
Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
11 I dostało się Manasesowi w pokoleniu Isaschar i w Aser, Betsan i miasteczka jego, i Jeblaam i miasteczka jego; przytem mieszkający w Dor i miasteczka ich, także mieszkający w Endor i miasteczka ich; i mieszkający też w Tanach i miasteczka ich, i mieszkający w Magiedda i miasteczka ich; trzy powiaty.
Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
12 Ale nie mogli synowi Manasesowi wypędzić z onych miast obywateli; przetoż począł Chananejczyk mieszkać w onej ziemi.
Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
13 A gdy się zmocnili synowie Izraelscy, uczynili Chananejczyka hołdownikiem: ale go nie wygnali do szczętu.
Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
14 Tedy rzekli synowie Józefowi do Jozuego, mówiąc: Przeczżeś nam dał w dziedzictwo los jeden, i sznur jeden? a myśmy lud wielki i dotąd błogosławił nam Pan.
Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
15 I rzekł do nich Jozue: Jeźliś jest ludem wielkiem, idźże do lasu, a wysiecz sobie tam miejsca w ziemi Ferezejskiej, i Refaimskiej, jeźlić ciasna góra Efraimowa.
Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
16 Któremu odpowiedzieli synowie Józefowi: Nie dosyć nam na tej górze; do tego wozy żelazne są u wszystkich Chananejczyków, którzy mieszkają w ziemi nadolnej, i u tych, którzy mieszkają w Betsan i w miasteczkach jego, także u tych, którzy mieszkają w dolinie Jezreel.
Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
17 RZekł tedy Jozue do domu Józefowego, do Efraima i do Manasesa, mówiąc: Ludeś ty wielki, i moc twoja wielka, nie będziesz miał tylko losu jednego.
Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
18 Ale górę będziesz miał; a iż tam jest las, tedy go wyrąbiesz, i będziesz miał granice jego; bo wypędzisz Chananejczyka, choć ma wozy żelazne i choć jest potężny.
dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”

< Jozuego 17 >