< Jana 7 >

1 A potem chodził Jezus po Galilei; bo się nie chciał bawić w ziemi Judzkiej, przeto że Żydowie szukali, aby go zabili.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 I było blisko święto żydowskie kuczek.
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 Tedy rzekli do niego bracia jego: Odejdź stąd, a idź do Judzkiej ziemi, żeby uczniowie twoi widzieli sprawy twoje, które czynisz.
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 Albowiem żaden nic w skrytości nie czyni, kto chce być widziany; przetoż ty, jeźli takie rzeczy czynisz, objaw się światu.
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 Bo i bracia jego nie wierzyli weń.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 I rzekł im Jezus: Czas mój jeszcze nie przyszedł; ale czas wasz zawsze jest w pogotowiu.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 Nie możeć was świat nienawidzieć, ale mnie nienawidzi; bo ja świadczę o nim, iż sprawy jego złe są.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 Idźcież wy na to święto, jać jeszcze nie pójdę na to święto; bo mój czas jeszcze się nie wypełnił.
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 A to im powiedziawszy, został w Galilei.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 A gdy poszli bracia jego, tedy i on szedł na święto, nie jawnie, ale jakoby potajemnie.
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 A Żydowie szukali go w święto i mówili: Gdzież on jest?
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 I było o nim wielkie szemranie między ludem; bo jedni mówili: Że jest dobry; a drudzy mówili: Nie, ale zwodzi lud.
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 Wszakże o nim żaden jawnie nie mówił, dla bojaźni żydowskiej.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 A gdy już było w pół święta, wstąpił Jezus do kościoła i uczył.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 I dziwowali się Żydowie, mówiąc: Jakoż ten umie Pismo, gdyż się nie uczył?
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 Odpowiedział im Jezus i rzekł: Nauka moja nie jestci moja, ale tego, który mię posłał.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 Jeźliby kto chciał czynić wolę jego, ten będzie umiał rozeznać, jeźli ta nauka jest z Boga, czyli ja sam od siebie mówię.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 Ktoć z samego siebie mówi, chwały własnej szuka; ale kto szuka chwały tego, który go posłał, ten jest prawdziwy, a nie masz w nim niesprawiedliwości.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 Izali wam Mojżesz nie dał zakonu? a żaden z was nie przestrzega zakonu. Przeczże szukacie, abyście mię zabili?
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 Odpowiedział lud i rzekł: Dyjabelstwo masz; któż cię szuka zabić?
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 Odpowiedział Jezus i rzekł im: Jedenem uczynek uczynił, a wszyscy się temu dziwujecie!
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 Wszak Mojżesz wydał wam obrzezkę, (nie iżby była z Mojżesza, ale z ojców), a w sabat obrzezujecie człowieka.
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 Ponieważ człowiek przyjmuje obrzezkę w sabat, aby nie był zgwałcony zakon Mojżeszowy, przecz się na mię gniewacie, żem całego człowieka uzdrowił w sabat?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Nie sądźcie według widzenia, ale sprawiedliwy sąd sądźcie.
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Mówili tedy niektórzy z Jeruzalemczyków: Izali to nie jest ten, którego szukają zabić?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 A oto jawnie mówi, a nic mu nie mówią. Izali prawdziwie poznali książęta, iż ten jest prawdziwie Chrystus?
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 Ale o tym wiemy, skąd jest: ale gdy Chrystus przyjdzie, nikt nie będzie wiedział, skąd by był.
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 Wołał tedy Jezus w kościele ucząc a mówiąc: I mnie znacie, i skądem jest, wiecie; a nie przyszedłem sam od siebie, ale jest prawdziwy, który mię posłał, którego wy nie znacie.
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 Lecz go ja znam; bom od niego jest, a on mię posłał.
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 I szukali, jakoby go pojmać; ale żaden nie ściągnął nań ręki; bo jeszcze nie przyszła godzina jego.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 A wiele ich z ludu uwierzyli weń i mówili: Chrystus gdy przyjdzie, izaż więcej cudów uczyni nad te, które ten uczynił?
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 A słyszeli Faryzeuszowie, iż to lud o nim szemrał; i posłali Faryzeuszowie i przedniejsi kapłani sługi, aby go pojmali.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 Rzekł im tedy Jezus: Jeszcze na mały czas jestem z wami; potem odejdę do tego, który mię posłał.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 Szukać mię będziecie, ale nie znajdziecie; a gdzie ja będę, wy przyjść nie możecie.
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 Mówili tedy Żydowie między sobą: Dokądże ten pójdzie, że my go nie znajdziemy? czyli do rozproszonych poganów pójdzie i będzie uczył pogany?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 Cóż to za mowa, którą wyrzekł: Szukać mię będziecie, ale nie znajdziecie, i gdzie ja będę, wy przyjść nie możecie?
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 A w on ostateczny dzień wielki święta onego stanął Jezus i wołał mówiąc: Jeźli kto pragnie, niech do mnie przyjdzie, a pije.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 Kto wierzy w mię, jako mówi Pismo, rzeki wody żywej popłyną z żywota jego.
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 (A to mówił o Duchu, którego wziąć mieli wierzący weń; albowiem jeszcze nie był dany Duch Święty, przeto że jeszcze Jezus nie był uwielbiony.)
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 Wiele ich tedy z owego ludu słysząc te słowa, mówili: Tenci jest prawdziwie on prorok.
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 A drudzy mówili: Ten jest Chrystus; ale niektórzy mówili: Azaż z Galilei przyjdzie Chrystus?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 Azaż nie mówi Pismo, iż z nasienia Dawidowego i z Betlehemu miasteczka, gdzie był Dawid, przyjdzie Chrystus?
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 A tak stało się rozerwanie dla niego między ludem.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 I chcieli go niektórzy z nich pojmać; ale żaden nie ściągnął nań rąk swoich.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 Przyszli tedy słudzy do przedniejszych kapłanów i do Faryzeuszów; którzy im rzekli: Przeczżeście go nie przywiedli?
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 Odpowiedzieli oni słudzy: Nigdy tak nie mówił człowiek jako ten człowiek.
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 I odpowiedzieli im Faryzeuszowie: Alboście i wy zwiedzeni?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Izali kto uwierzył weń z książąt albo z Faryzeuszów?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 Tylko ten gmin, który nie zna zakonu; przeklęci są.
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 I rzekł do nich Nikodem, który był przyszedł w nocy do niego, będąc jeden z nich:
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 Izali zakon nasz sądzi człowieka, jeźliby pierwej nie słyszał od niego i nie poznałby, co czyni?
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 A oni mu odpowiedzieli i rzekli: Izaliś i ty Galilejczyk? Badajże się, a obacz, żeć prorok z Galilei nie powstał.
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
53 I poszedł każdy do domu swego.
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.

< Jana 7 >