< Joela 2 >

1 Trąbcie w trąbę na Syonie, a krzyczcie na świętej górze mojej! niechaj zadrżą wszyscy obywatele ziemi; bo przychodzi dzień Pański, bo już bliski jest;
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 Dzień ciemności i mroku, dzień obłoku i chmury, jako ranna zorza rozciągniona po górach; lud wielki a mocny, któremu równego nie było od wieku, i nie będzie po nim nigdy aż do lat rodzaju i rodzaju.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Przed obliczem jako ogień pożerający, a za nim płomień pałający; ta ziemia jest przed nim jako ogród Eden, ale po nim będzie pustynią pustą i nie ujdzie nikt przed nim.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Kształt ich jest jako kształt koni, a tak pobieżą jako jezdni.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Po wierzchu gór skakać będą jako grzmot wozów, a jako szum płomienia ognistego pożerającego ściernisko, jako lud możny uszykowany do bitwy.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Ulękną się narody przed obliczem jego, wszystkie twarze ich jako garniec poczernieją.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Pobieżą jako mocarze, a wbieżą na mury jako mężowie waleczni; każdy z nich drogą swoją pójdzie, a nie ustąpią z ścieżek swoich.
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 Jeden drugiego nie ściśnie, każdy drogą swoją pójdzie; a choć i na miecz upadną, nie będą zranieni.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Po mieście chodzić będą, po murze biegać, na domy wstąpią, a oknami wlezą jako złodziej.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Przed obliczem jego ziemia zadrży, niebiosa się poruszą, słońce i miesiąc się zaćmi, a gwiazdy zawściągną jasność swoję.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 A Pan wyda głos swój przed wojskiem swojem, przeto, że bardzo wielki będzie obóz jego, przeto, że mocny ten, co wykona słowo jego; wielki bowiem dzień Pański będzie i straszliwy bardzo, i któż go zniesie?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 A przetoż jeszcze i teraz mówi Pan: Nawróćcie się do mnie samego całem sercem swojem, i w poście i w płaczu i w kwileniu.
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 Rozedrzyjcie serce wasze a nie szaty wasze, i nawróćcie się do Pana, Boga waszego; boć on jest łaskawy i miłosierny, nierychły ku gniewu, a hojny w miłosierdziu, i żałujący złego.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Któż wie, nie obrócili się, a nie będzieli mu żal, i nie zostawili po sobie błogosławieństwa na śniedną i mokrą ofiarę Panu, Bogu waszemu.
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Trąbcie w trąbę na Syonie, poświęćcie post, zwołajcie zgromadzenie.
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Zgromadźcie lud, poświęćcie zgromadzenie, zbierzcie starców, znieście maluczkie i ssące piersi; niech wynijdzie oblubieniec z łożnicy swojej, a oblubienica z pokoju swego.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Kapłani, słudzy Pańscy, między przysionkiem a ołtarzem niech płaczą i mówią: Przepuść, Panie! ludowi twemu, a nie daj dziedzictwa swego na pohańbienie, aby nad nimi poganie panować mieli. Przeczżeby mówiono między narodami: Gdzież jest Bóg ich?
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 I zapali się Pan miłością ku ziemi swojej, a zmiłuje się nad ludem swoim.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 I ozwie się Pan, a rzecze do ludu swego: Oto Ja poślę wam zboże, i moszcz, i oliwę, a będziecie niemi nasyceni, i nie podam was więcej na pohańbienie między pogan.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 Bo północne wojsko oddalę od was, a zapędzę je do ziemi suchej i spustoszonej; przedni huf jego obróci się ku morzu wschodniemu, a koniec jego ku morzu ostatecznemu, i wynijdzie z niego smród i zgniłość, choć sobie hardzie poczyna.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Nie bój się, ziemio! wesel się a raduj się; bo Pan wielkie rzeczy uczyni.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Nie bójcie się zwierzęta pól moich; boć wzrosło pastwisko na pustyni, a drzewa przyniosą owoce swoje, figowe drzewo i macica winna wydadzą moc swoję.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 I wy, synowie Syońscy! weselcie się i radujcie się w Panu, Bogu waszym; bo wam da deszcz wczesny, a ześle wam deszcz obfity w jesieni i na wiosnę.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 I będą gumna zbożem napełnione, a prasy opływać będą moszczem i oliwą.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 A tak nagrodzę wam lata, które zjadła szarańcza, czerw, chrząszcze i gąsienice, wojsko moje wielkie, którem posyłał na was.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Tedy jedząc jeść będziecie, a nasyceni będąc chwalić będziecie imię Pana, Boga swego, który uczynił z wami dziwne rzeczy, i nie będzie pohańbiony lud mój na wieki.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 I dowiecie się, żem Ja jest w pośród Izraela, a żem Ja Panem, Bogiem waszym, a że niemasz inszego; boć nie będzie pohańbiony lud mój na wieki.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 A potem wyleję Ducha mego na wszelkie ciało, a prorokować będą synowie wasi i córki wasze; starcom waszym sny się śnić będą, a młodzieńcy wasi widzenia widzieć będą.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Nawet i na sługi i na służebnice wyleję w one dni Ducha mego.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 I dam cuda na niebie i na ziemi, krew i ogień i słupy dymowe.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Słońce obróci się w ciemność, a miesiąc w krew, pierwej niż dzień Pański wielki a straszny przyjdzie.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Wszakże stanie się, że ktobykolwiek wzywał imienia Pańskiego, wybawiony będzie; bo na górze Syon i w Jeruzalemie będzie wybawienie, jako rzekł Pan, to jest w ostatkach, które Pan powoła.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Joela 2 >