< Hioba 7 >

1 Izali czas nie jest zamierzony człowiekowi na ziemi? a jako dni najemnicze nie są dni jego?
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 Jako sługa pragnie cienia, a jako najemnik czeka końca pracy swojej:
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 Takiem ja prawem dziedzicznem wziął miesiące próżne, a nocy boleśne są mi naznaczone.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 Układęli się, tedy mówię: Kiedyż wstanę? a rychło pominie noc? i pełen bywam myślenia aż do świtania.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 Obleczone jest ciało moje w robaki i w plugastwo z prochu; skóra moja popadała się, i rozsiadła się.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 Dni moje prędsze są, niż czółnek tkacki, i strawione są bez nadziei.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 Wspomnij, o Panie! iż wiatrem jest żywot mój, nie wróci się oko moje, aby widziało dobre rzeczy.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 Ani mię ogląda oko, które mię widywało; oczy twoje obrócone będą na mię, a mnie nie będzie.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 Jako niszczeje obłok i przemija, tak zstępujący do grobu nie wynijdzie; (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 Nie wróci się więcej do domu swego, ani go więcej pozna miejsce jego.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Przetoż ja nie mogę zawściągnąć ust moich; mówić będę w utrapieniu ducha mego, będę rozmawiał w gorzkości duszy mojej.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Izażem ja jest morze, albo wieloryb, zasię mię osadził strażą?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 Gdym rzekł: Pocieszy mię łoże moje, i ulży mi narzekania mego pościel moja:
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 Tedy mię straszysz przez sny, i przez widzenia trwożysz mną.
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 A przetoż obrała sobie powieszenie dusz moja, a śmierć raczej, niż zostać w kościach.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Sprzykrzyłem sobie żywot, nie wiecznie będę żyw. Zaniechajże mię, bo marnością są dni moje.
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 Cóż jest człowiek, że go tak wielce ważysz? a że przykładasz ku niemu serce twoje?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 A że go nawiedzasz na każdy zaranek? i na każdą chwilę doświadczasz go?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Pokądże się nie odwrócisz odemnie? a nie zaniechasz mię, ażbym przełknął ślinę moję?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Zgrzeszyłem, cóż mam czynić? o stróżu ludzki! czemuś mię sobie za cel położył, abym był sam sobie ciężarem?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Przecz nie odejmiesz przestępstwa mego, i nie przepuścisz nieprawości mojej? Bo się teraz w prochu położę, a choćbyś mię szukał rano, nie będzie mię.
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Hioba 7 >