< Hioba 5 >

1 Zawołajże tedy, jeźli kto jest, coćby odpowiedział? a do któregoż się z świętych obrócisz?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Zaiste głupiego zabija gniew, a prostaka umarza zawiść.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Jam widział głupiego, iż się rozkorzenił; alem wnet źle tuszył mieszkaniu jego.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Oddaleni będą synowie jego od zbawienia, i starci będą w bramie, a nie będzie, ktoby ich wyrwał.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Żniwo jego głodny pożre, i z samego ciernia wybierze je; a połknie chciwy bogactwa takowych.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Albowiem nie z prochu wychodzi utrapienie, ani z ziemi wyrasta kłopot.
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 Ale człowiek na kłopot się rodzi jako iskry z węgla latają w górę.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 Zaiste jabym szukał Boga, Bogubym przełożył sprawę swoję;
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Który czyni rzeczy wielkie i niewybadane, dziwne, którym liczby niemasz;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Który daje deszcz na ziemię, i spuszcza wody na pola;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Który sadza pokornych wysoko, a smutnych wywyższa ku zbawieniu;
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Który w niwecz obraca myśli chytrych, tak, iż ręce ich nie sprawią nic skutecznego;
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Który chwyta mądrych w chytrości ich, a radę przewrotnych prędko niszczy.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 We dnie taczają się jako w ciemnościach, a jako w nocy macają w południe.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Który zachowuje ubogiego od miecza, od ust ich, i od ręki gwałtownika.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Mać uciśniony nadzieje; ale nieprawość stuli usta swe.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Oto błogosławiony człowiek, którego Bóg karze; przetoż karaniem Wszechmocnego nie pogardzaj,
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Bo on zrania i zawiązuje; uderza, a ręce jego uzdrawiają.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Z sześciu ucisków wyrwie cię, a w siódmym nie tknie się ciebie złe.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 W głodzie wybawi cię od śmierci, a na wojnie z rąk miecza.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Przed biczem języka ukryty będziesz, a nie ulękniesz się w spustoszeniu, gdy przyjdzie.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 W spustoszeniu i w głodzie śmiać się będziesz, a zwierząt ziemskich bać się nie będziesz.
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Bo z kamieniem polnym będzie przymierze twoje, a okrutny zwierz polny spokojnym ci się stawi.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 I poznasz, że jest spokojny przybytek twój, i nawiedzisz mieszkanie twoje, a nie zgrzeszysz.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Doznasz też, iż rozmnożone będzie nasienie twoje, a potomstwo twoje będzie jako ziele ziemi.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Wnijdziesz w sędziwości do grobu, jako znoszone bywa zboże w stóg czasu swego.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Otośmy tego doszli, że tak jest: słuchajże tego, a uważaj to sam u siebie.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Hioba 5 >