< Hioba 39 >

1 Izali wiesz czas rodzenia kóz skalnych, a kiedy rodzą łanie, postrzegłżeś?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Możeszże zliczyć miesiące, jako długo płód noszą? a czas rodzenia ich wieszże?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Jako się kurczą, płód swój wyciskają, a rozstępując się z boleścią go pozbywają;
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Jako moc biorą dzieci ich, i odchowywują się po zbożach, a odszedłszy nie wracają się do nich.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Któż wypuścił osła dzikiego na wolność? a pęta osła dzikiego któż rozwiązał?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Któremu dał pustynię miasto domu jego, a miasto mieszkania jego miejsca słone.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 On się naśmiewa ze zgrai miejskiej, a na głos tego, co go goni, nic niedba.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Patrzy po górach pastwy, a wszelkiej zielonej trawy szuka.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Izalić będzie chciał jednorożec służyć, albo będzie nocował u jaśli twoich?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Izali możesz zaprządz w powróz swój jednorożca do orania? izali powleka będzie brózdy za tobą?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Izali się spuścisz nań, przeto, że wielka moc jego? albo poruczyszli mu robotę twoję?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Powierzyszże mu się, żeby zwiózł nasienie twoje, a do gumna twojego zgromadził?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 Izaliś dał pawiowi piękne skrzydła, a pierze bocianowi i strusiowi?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Który niesie na ziemi jajka swoje, a w prochu ogrzewa je.
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 A nie pomni na to, że je noga zetrzeć, a zwierzę polne zdeptać może.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Zatwardza się przeciwko dzieciom swoim, jakoby nie były jego, a żeby nie była próżna praca jego, nie obawia się.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Bo mu nie dał Bóg mądrości, i nie udzielił mu wyrozumienia.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Według czasu podnosi się ku górze, a naśmiewa się z konia i z jeźdźca jego.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Izali możesz dać koniowi moc? izali rzaniem ozdobisz szyję jego?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Izali go ustraszysz jako szarańczę? i owszem chrapanie nozdrzy jego jest straszne.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Kopie dół, a weseli się w mocy swej, i bieży przeciwko zbrojnym.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Śmieje się z postrachu, a ani się lęka, ani nazad ustępuje przed ostrzem miecza.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Choć na nim chrzęści sajdak, i błyszczy się oszczep, i drzewce.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Z grzmotem i z gniewem kopie ziemię, a nie stoi spokojnie na głos trąby.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Między trąbami poryza, a z daleka czuje bitwę, krzyk książąt, i wołanie.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Izali według twego rozumu lata jastrząb, i rozciąga skrzydła swe ku południowi?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Izali na twoje rozkazanie wzbija się orzeł w górę, i składa na wysokich miejscach gniazdo swoje?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Na opoce mieszka, i bawi się na ostrej skale, jako na zamku.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Stamtąd upatruje sobie pokarm, a daleko oczy jego widzą.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Dzieci też jego piją krew, a gdzie są pobici, tam on jest.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< Hioba 39 >