< Hioba 38 >

1 Tedy odpowiedział Pan Ijobowi z wichru, i rzekł:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 Któż to jest, co zaciemnia radę Bożą mowami nieroztropnemi?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Przepasz teraz jako mąż biodra swoje, a będę cię pytał, a ty mi daj sprawę.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 Gdzieżeś był, kiedym Ja zakładał grunty ziemi? Powiedz, jeźliże nasz rozum.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Któż uczynił rozmierzenie jej? powiedz, jeżli wiesz; albo kto sznur nad nią rozciągnął?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Na czem są podstawki jej ugruntowane? albo kto założył kamień jej węgielny?
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 Gdy wespół śpiewały gwiazdy zaranne, a weselili się wszyscy synowie Boży.
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 Któż zamknął drzwiami morze, gdy się wyrywało, jakoby z żywota wychodząc?
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 Gdym położył obłok za szatę jego, a ciemność za pieluchy jego;
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 Gdym postanowił o niem dekret mój, a przyprawiłem zaworę i drzwi do niego,
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 I rzekłem: Aż dotąd wychodzić będziesz, a dalej nie postąpisz, a tu położysz nadęte wały twoje.
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Izażeś za dni twoich rozkazywał świtaniu, i ukazałeś zorzy miejsce jej?
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 Aby ogarnęła kończyny ziemi, a iżby byli z niej wyrzuceni niepobożni.
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 Aby się odmieniała jako glina, do której pieczęć przykładają, a oni aby się stali jako szatą nakryci.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 I aby była zawściągniona od niepobożnych światłość ich, a ramię wysokie było pokruszone.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 Izażeś przyszedł aż do źródeł morskich, a po dnie przepaści przechodziłeś się?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Azaż odkryte są tobie bramy śmierci? bramy cienia śmierci widziałżeś?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Izaliś rozumem twym doszedł szerokości ziemi? Powiedz mi, jeźli to wszystko wiesz?
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Gdzież jest ta droga do miejsca światłości? a ciemności gdzie mają miejsce swoje?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 Abyś ją ująwszy odprowadził do granicy jej, ponieważ zrozumiewasz ścieszki do domu jej.
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Wiedziałżeś na on czas, żeś się miał urodzić? i liczba dni twoich jak wielka być miała?
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 Izaliś przyszedł do skarbów śniegów? aby skarby gradu widzałeśli?
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 Które zatrzymywam na czas ucisku, na dzień bitwy i wojny.
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 Którąż się drogą dzieli światłość, i gdzie się rozchodzi wiatr wschodni po ziemi?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Któż rozdzielił stok powodziom? a drogę błyskawicy gromów?
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 Aby szedł deszcz na ziemię, w której nikt nie mieszka, i na pustynię, gdzie niemasz człowieka;
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 Aby nasycił miejsce puste i niepłodne, a wywiódł z niego zieloną trawę.
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Izali ma deszcz ojca? a krople rosy kto płodzi?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 Z czyjegoż żywota wychodzi mróz? a szron niebieski któż płodzi?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Jakoż się kamieniem wody nakrywają, gdy wierzch przepaści zamarza.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Możeszże związać jasne gwiazdy Bab? albo związek Oryjona rozerwać?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Izali wywiedziesz gwiazdy południowe czasu swego, albo Wóz niebieski z gwiazdami jego powiedziesz?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 I znaszże porządek nieba? a możeszże rozrządzić panowanie jego na ziemi?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Izali podniesiesz ku obłokowi głos twój, aby cię wielkość wód okryła?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Izali możesz wypuścić błyskawice, aby przyszły, i rzekłyć: Otośmy?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Któż złożył we wnętrznościach ludzkich mądrość, a kto dał rozumowi bystrość?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Któż obrachował niebiosa mądrością swoją? a co się leje z nieba, któż uspokoi?
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 Aby polany proch stężał, a bryły aby się społu zelgnęły?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Izali lwowi łup łowisz, a lwiąt żywot napełniasz?
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 Gdy się tulą w jaskiniach swoich, i czyhają w cieniu jam swoich?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Któż gotuje krukowi pokarm jego, gdy dzieci jego do Boga wołają a tułają się, nie mając pokarmu?
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Hioba 38 >