< Hioba 36 >

1 Do tego przydał Elihu, i rzekł:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Poczekaj mię maluczko, a ukażęć; bo jeszcze mam, cobym za Bogiem mówił.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Zacznę umiejętność moję z daleka, a Stworzycielowi memu przywłaszczę sprawiedliwość.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Boć zaprawdę bez kłamstwa będą mowy moje, a mąż doskonały w umiejętności jest przed tobą.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Oto Bóg mocny jest, a nie odrzuca nikogo; on jest mocny w sile serca.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Nie żywi niepobożnego, a u sądu ubogim dopomaga.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Nie odwraca od sprawiedliwego oczów swoich; ale z królmi na stolicy sadza ich na wieki, i bywają wywyższeni.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 A jeźliby byli okowani w pęta, albo uwikłani powrozami utrapienia:
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Tedy przez to im oznajmuje sprawy ich, i przestępstwa ich, że się zmocniły;
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 I otwiera im ucho, aby przyjęli karanie, a mówi, aby się nawrócili od nieprawości.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Jeźli będą posłuszni, a będą mu służyć, dokończą dni swoich w dobrem, a lat swych w rozkoszach.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Ale jeźli nie usłuchają, od miecza zejdą, a pomrą bez umiejętności.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Bo ludzie obłudnego serca obalają na się gniew, a nie wołają, kiedy ich wiąże.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Umrze w młodości dusza ich, a żywot ich między nierządnikami.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Wyrwie utrapionego z utrapienia jego, a otworzy w uciśnieniu ucho jego.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Takby i ciebie wyrwał z miejsca ciasnego na przestronne, gdzie niemasz ucisku, a spokojny stół twój byłby pełen tłustości.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Aleś ty sąd niepobożnego zasłużył, przetoż prawo i sąd będą cię trzymać.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Zaisteć gniew Boży jest nad tobą; patrzże, aby cię nie poraził plagą wielką, tak, żeby cię nie wybawił żaden okup.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Izali sobie będzie ważył bogactwa twoje? Zaiste ani złota, ani jakiejkolwiek siły, albo potęgi twojej.
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Nie kwapże się tedy ku nocy, w którą zstępują narody na miejsca swoje.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Strzeż, abyś się nie oglądał na nieprawość, obierając ją sobie nad utrapienia.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Oto Bóg jest najwyższy w mocy swojej, któż tak nauczyć może jako on?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Któż mu wymierzył drogę jego? albo kto mu rzecze: Uczyniłeś nieprawość?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Pamiętajże, abyś wysławiał sprawę jego, której się przypatrują ludzie.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Wszyscy ludzie widzą ją, a człowiek przypatruje się jej z daleka.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Oto Bóg jest wielki, a poznać go nie możemy, ani liczba lat jego dościgniona być może.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Bo on wyciąga krople wód, które wylewają z obłoków jego deszcz,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Który spuszczają obłoki, a spuszczają na wiele ludzi.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 (Nadto, któż zrozumie rozciągnienie obłoków, i grzmot namiotu jego.
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Jako rozciąga nad nim światłość swoję, a głębokości morskie okrywa?
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Bo przez te rzeczy sądzi narody, i daje pokarm w hojności.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Obłokami nakrywa światłość, i rozkazuje jej ukrywać się za obłok następujący.)
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Daje o nim znać szum jego, także i bydło i para w górę wstępująca.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Hioba 36 >