< Hioba 33 >

1 A przetoż, Ijobie! słuchaj proszę mów moich, a wszystkie słowa moje przyjmij w uszy.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Oto teraz otworzę usta moje, a język mój będzie mówił w podniebieniu mojem.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Szczerością serca mego będą słowa moje, a czyste zdania wargi moje mówić będą.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 Duch Boży uczynił mię, a tchnienie Wszechmocnego ożywiło mię.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Możeszli, odpowiedz mi; sporządź się, a stań przeciwko mnie.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Oto ja według słów twoich odpowiem ci za Boga, chociażem ja też z błota utworzony.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Oto strach mój nie zatrwoży cię, a ręka moja nie obciąży cię.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 A wszakżeś rzekł w uszy moje, i słyszałem głos słów moich.
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Czystym ja bez przestępstwa; niewinnym ja, i nie masz we mnie nieprawości.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Oto znajduje Bóg przyczyny przeciwko mnie, a poczytuje mię za nieprzyjaciela swego.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Podaje w okowy nogi moje, a podstrzega wszystkich ścieżek moich.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Otości na to tak odpowiadam: W tem nie jesteś sprawiedliwy; bo większy jest Bóg, niż człowiek.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Przeczże się z nim spierasz, żeć wszystkich spraw swoich nie objawia?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Wszak Bóg mówi i raz i drugi, a człowiek tego nie uważa.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 We śnie w widzeniu nocnem, gdy twardy sen przypada na ludzie gdy śpią na łożu:
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Tedy otwiera ucho ludzkie, a to, czem ich ćwiczy, pieczętuje,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 Aby człowieka odwiódł od złej sprawy jego, i pychę od męża aby odjął;
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 Aby zahamował duszę jego od dołu, a żywot jego aby na miecz nie trafił.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Każe go też boleścią na łożu jego, a we wszystkich kościach jego ciężką niemocą.
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Tak, że sobie żywot jego chleb obrzydzi, a dusza jego pokarm wdzięczny.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Zniszczeje znacznie ciało jego, i wysadzą się kości jego, których nie widać było;
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 I przybliża się do grobu dusza jego a żywot jego do rzeczy śmierć przynoszących.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Jeźli będzie u niego jaki Anioł wymowny, jeden z tysiąca, aby opowiedział człowiekowi powinność jego:
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Tedy się nad nim Bóg zmiłuje, a rzecze: Wybaw go, aby nie zstępował do grobu, bom znalazł ubłaganie.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 I odmłodnieje ciało jego jako dziecięce, a nawróci się do dni młodości swojej.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Będzie się modlił Bogu, i przyjmie go łaskawie, i ogląda z weselem oblicze jego, i przywróci człowiekowi sprawiedliwość jego;
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Który poglądając na ludzi, rzecze: Zgrzeszyłem był, i co było prawego, podwróciłem; ale mi to nie było pożyteczno.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Lecz Bóg wybawił duszę moję, aby nie zstąpiła do dołu, a żywot mój aby oglądał światłość.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Oto wszystko to czyni Bóg po dwakroć i po trzykroć z człowiekiem,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 Aby odwrócił duszę jego od dołu, a żeby oświecon był światłością żyjących.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Uważaj to, Ijobie, słuchaj mię; milcz, a ja będę mówił.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Wszakże maszli co mówić, a odpowiedzże mi; mów, bobym cię rad usprawiedliwił.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 A jeźli niemasz, słuchajże mię, a nauczę cię mądrości.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Hioba 33 >