< Hioba 28 >

1 Mać w prawdzie srebro początki żył swoich, a złoto miejsce, kędy bywa pławione.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Żelazo z ziemi biorą, a z kamienia zlewają miedź.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Celu ciemnościom ułożonego i końca wszystkich rzeczy on dochodzi, i kamieni, które w ciemności i cieniu śmierci leżą.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Wyleje rzeka z miejsca swojego, tak, iż jej nikt przebyć nie może, bywa jednak zahamowana przemysłem nędznego człowieka, i odchodzi.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 Z ziemi wychodzi chleb, chociaż pod nią coś różnego, podobnego ogniowi.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 W niektórych miejscach jest kamień Safir, i piasek złoty;
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 A tej ścieszki ani ptak nie wie, ani jej widzało oko sępie.
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 Nie depczą po niej zwierzęta srogie, ani lew przeszedł przez nię.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 Na krzemień ściągnął rękę swoję, wywrócił góry z korzenia;
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Z skał wywodzi strumienie, a każdą rzecz kosztowną widzi oko jego.
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 Wylewać się rzekom nie dopuszcza, a rzeczy skryte wywodzi na jaśnię.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Ale mądrość gdzież może być znaleziona? a kędy jest miejsce roztropności?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Nie wie człowiek śmiertelny ceny jej, ani bywa znaleziona w ziemi żyjących.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 Przepaść mówi: Niemasz jej we mnie; i morze też powiada: Niemasz jej u mnie.
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Nie dawają szczerego złota za nię; ani odważają srebra, za odmianę jej.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 Nie może być oszacowana za złoto Ofir, ani za Onychyn drogi, ani za Safir.
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Nie porówna z nią złoto, ani kryształ, ani odmiana jej może być za klejnot złota szczerego.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Koralów i pereł nie wspomina, bo nabycie mądrości kosztowniejsze jest nad perły.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 Nie zrówna z nią i szmaragd z ziemi etyjopskiej; ani za złoto najczystsze szacowana być może.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Skądże tedy mądrość pochodzi? albo gdzie jest miejsce rozumu?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Gdyż zakryta jest od oczu wszystkich żyjących, i przed ptastwem niebieskim zatajona jest.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 Zginienie i śmierć rzekły: Uszyma swemi słyszałyśmy sławę jej.
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 Bóg sam rozumie drogę jej, a on wie miejsce jej.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 Bo on na kończyny ziemi patrzy, a wszystko, co jest pod niebem, widzi.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Wiatrom uczynił wagę, a wody odważył pod miarą.
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 On też prawo dżdżom postanowił, a drogę błyskawicom gromów.
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 W ten czas ją widział, i głosił ją: zgotował ją, i doszedł jej.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 Ale człowiekowi rzekł: Oto bojaźń Pańska jest mądrością, a warować się złego, jest rozumem.
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”

< Hioba 28 >