< Hioba 21 >

1 A odpowiadając Ijob rzekł:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Słuchajcież z pilnością słów moich, a będzie mi to od was pociechą.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Znoście mię, a ja będę mówił; a gdy domówię, naśmiewajcie się.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Izaż do człowieka obracam narzekanie moje? a ponieważ mam o co, jakoż się niema trapić duch mój?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Wejrzyjcież na mię, a zdumiewajcie się, a połóżcie rękę na usta wasze.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Bo co sobie wspomnę, tedy się lękam, a strach zdejmuje ciało moje.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Przeczże niepobożni żyją, starzeją się, i wzmagają się w bogactwa?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Nasienie ich trwałe jest przed obliczem ich z nimi, a rodzina ich przed oczyma ich.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Domy ich bezpieczne od strachu, a niemasz rózgi Bożej nad nimi.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Byk ich przypuszczon bywa, a nie traci nasienia; krowa ich rodzi, a nie pomiata.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Wypuszczają maluczkie dziatki swoje jako trzodę, a synowie ich wyskakują.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Wykrzykają przy bębnie i przy harfie, a weselą się przy głosie muzyki.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Trawią w dobrem dni swoje, a we mgnieniu oka do grobu zstępują. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Którzy mawiają Bogu: Odejdź od nas; bo dróg twoich znać nie chcemy.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Któż jest Wszechmocny, abyśmy mu służyli? a cóż nam to pomoże, choćbyśmy mu się modlili?
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Ale oto, dobra ich nie są w rękach ich; przetoż rada niepobożnych daleka jest odemnie.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 Częstoż pochodnia niepobożnych gaśnie? a zginienie ich przychodzi na nich? Oddziela im Bóg boleści w gniewie swoim.
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Stawają się jako plewa przed wiatrem, i jako perz, który wicher porywa.
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Bo Bóg chowa synom jego pomstę jego; nadgradza mu, aby to poczuł.
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Oglądają oczy jego nieszczęście swoje, a z popędliwości Wszechmocnego pić będzie.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 Co za staranie jego o domu jego po nim, gdyż liczba miesięcy jego umniejszona jest?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Izali Boga kto nauczy umiejętności, gdyż on wysokich sądzi?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Ten umiera w doskonałej sile swojej, gdy zewsząd bezpieczny i spokojny jest;
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 Gdy piersi jego pełne są mleka, a szpik kości jego odwilża się,
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Inny zaś umiera w gorzkości ducha, który nie jadał z uciechą.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Spólnie w prochu leżeć będą, a robaki ich okryją.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Oto ja znam myśli wasze i zamysły, które przeciwko mnie złośliwie zmyślacie.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 Bo mówicie: Gdzież jest dom książęcy? gdzie namiot przybytków niepobożnych?
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Izaliście nie pytali podróżnych? a znaków ich izali znać nie chcecie?
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 Że w dzień zatracenia zły zachowany bywa, w dzień, którego gniew przywiedziony bywa.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Któż mu oznajmi w oczy drogę jego? a to, co czynił, kto mu odpłaci?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Wszakże i on do grobów zaprowadzony będzie, a w kupie umarłych zawżdy zostanie.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Słodnieją mu bryły grobowe, i ciągnie za sobą wszystkich ludzi; a tych, którzy go poprzedzili, niemasz liczby.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 Jakoż mię tedy próżno cieszycie, gdyż w odpowiedziach waszych zostaje kłamstwo?
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Hioba 21 >