< Hioba 15 >

1 A odpowiadając Elifas Temańczyk rzekł:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Izali mądry ma na wiatr mówić? albo napełniać wschodnim wiatrem myśl swoję?
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Przytaczając słowa niepożyteczne, i mowy, z których nie masz pożytku?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Zaiste ty psujesz bojaźń Bożą i znosisz modlitwy do Boga.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Albowiem pokazują nieprawość twą usta twoje, chociażeś sobie obrał język chytrych,
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Potępiają cię usta twoje, a nie ja; a wargi twoje świadczą przeciwko tobie.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Czyś się najpierwszym człowiekiem urodził? czyś przed pagórkami utworzony?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Izażeś tajemnic Bożych słuchał, a nie masz mądrości jedno w tobie?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Cóż ty umiesz, czego my nie wiemy? albo cóż ty rozumiesz, czegobyśmy my nie rozumieli?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 I sędziwyć i starzec między nami jest starszy w latach niż ojciec twój.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 I lekceż sobie ważysz pociechy Boskie? i maszże jeszcze co tak skrytego w sobie?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Czemuż cię tak uniosło serce twoje? Czemu mrugają oczy twoje?
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 Że tak odpowiada Bogu duch twój, a wypuszczasz z ust twoich takowe mowy?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 Cóż jest człowiek, aby miał być czystym, albo żeby miał być sprawiedliwym, urodzony z niewiasty?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Oto i w świętych jego niemasz doskonałości, i niebiosa nie są czyste w oczach jego.
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Daleko więcej obrzydły jest, i nieużyteczny człowiek, który pije nieprawość jako wodę.
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 Okażęć, tylko mię słuchaj; a com widział, oznajmięć,
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Co mędrzy powiedzieli, a nie zataili, co mieli od przodków swoich;
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 Którym samym dana była ziemia, a żaden obcy nie przeszedł przez nię.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Po wszystkie dni swoje sam siebie niepobożny boleśnie trapi, a nie wiele lat zamierzono okrutnikowi.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Głos straszliwy brzmi w uszach jego, że czasu pokoju pustoszący przypadnie nań.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Nie wierzy, żeby się miał nawrócić z ciemności, obawiając się zewsząd miecza.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Tuła się za chlebem, szukając gdzieby był; wie, że zgotowany jest dla niego dzień ciemności.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Straszą go utrapienie i ucisk, i zmocnią się przeciwko niemu jako król gotowy do boju.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Bo wyciągną przeciw Bogu rękę swą, a przeciwko Wszechmocnemu zmocnił się.
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 Natrze nań na szyję jego z gęstemi i wyniosłemi tarczami swemi.
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 Bo okrył twarz swą tłustością swoją, a fałdów mu się naczyniło na słabiźnie.
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 I mieszka w miastach popustoszonych, i w domach, w których nie mieszkano, które się miały obrócić w kupę rumu.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Nie zbogaci się, i nie ostoi się majętność jego, ani się rozszerzy na ziemi doskonałość takowych.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Nie wynijdzie z ciemności; świeżą jego latorośl ususzy płomień, a zginie od ducha ust jego.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Nie wierzy, że w próżności jest, który błądzi; a że próżność będzie nagrodą jego.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Przed wypełnieniem dni swoich wycięty będzie, a różdżka jego nie zakwitnie.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Jako winna macica utraci niedojrzałe grona swoje, a jako oliwa kwiat swój zrzuci.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Albowiem zgromadzenie obłudnych spustoszone będzie, a ogień pożre przybytki pobudowane za dary.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Poczęli kłopot, a porodzili nieprawość; a żywot ich gotuje zdradę.
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Hioba 15 >