< Hioba 14 >

1 Człowiek, narodzony z niewiasty, dni krótkich jest, i pełen kłopotów;
“Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 Wyrasta jako kwiat, i bywa podcięty, a ucieka jako cień, i nie ostoi się.
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 Wszakże i na takiego otwierasz oczy twoje, a przywodzisz mię do sądu z sobą.
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 Któż pokaże czystego z nieczystego? Ani jeden;
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 Gdyż zamierzone są dni jego, liczba miesięcy jego u ciebie; zamierzyłeś mu kres, którego nie może przestąpić.
Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 Odstąpże od niego, aż odpocznie, aż przejdzie jako najemniczy dzień jego.
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 Albowiem i o drzewie jest nadzieja, choć je wytną, że się jeszcze odmłodzi, a latorośl jego nie ustanie.
“Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 Choć się zstarzeje w ziemi korzeń jego, i w prochu obumrze pień jego:
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 Wszakże gdy uczuje wilgotność, puści się, i rozpuści gałęzie, jako szczep młody.
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 Ale człowiek umiera, zemdlony będąc, a umarłszy człowiek gdzież jest?
Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 Jako uchodzą wody z morza, a rzeka opada i wysycha.
Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 Tak człowiek, gdy się układzie, nie wstanie więcej, a pokąd stoją nieba, nie ocuci się, ani będzie obudzony ze snu swego.
momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 Obyżeś mię w grobie ukrył i utaił, ażby się uciszył gniew twój, a iżbyś mi zamierzył kres, kędy chcesz wspomnieć na mię! (Sheol h7585)
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
14 Gdy umrze człowiek, izali żyć będzie? Po wszystkie dni wymierzonego czasu mego będę oczekiwał przyszłej odmiany mojej.
Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Zawołasz, a ja tobie odpowiem; a spraw rąk twoich pożądasz.
Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 Aczkolwiekeś teraz kroki moje obliczył, ani odwłóczysz karania za grzech mój.
Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
17 Zapięczętowane jest w wiązance przestępstwo moje, a zgromadzasz nieprawości moje.
Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
18 Prawdziwie jako góra padłszy rozsypuje się, a skała przenosi się z miejsca swego.
“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 Jako woda wzdrąża kamienie, a powodzią zalane bywa, co samo od siebie rośnie z prochu ziemi: tak nadzieję ludzką w niwecz obracasz.
monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Przemagasz go ustawicznie, a on schodzi; odmieniasz postać jego, i wypuszczasz go.
Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 Będąli zacni synowie jego, tego on nie wie; jeźli też wzgardzeni, on nie baczy.
Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 Tylko ciało jego, póki żyw, boleje, a dusza jego w nim kwili.
Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”

< Hioba 14 >