< Jeremiasza 9 >

1 Kto mi to da, aby głowa moja wodą była, a oczy moje źródłem łez, abym we dnie i w nocy płakał pomordowanych córki ludu mego!
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 Któż mi da na puszczy gospodę podróżnych, abym opuścił lud mój, i odszedł od nich? bo wszyscy są cudzołożnicy, zgraja przestępników;
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 I naciągają języka swego do kłamstwa jako łuku swego, zmocnili się na ziemi, ale nie ku prawdzie; bo ze złego w złe postępują, a mnie nie znają, mówi Pan.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 Każdy niech się strzeże bliźniego swego, a nie każdemu bratu dowierza; bo każdy brat jest na tem jakoby podszedł, a każdy bliźni zdradliwie postępuje.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 Każdy też bliźniego swego oszukuje, a prawdy nie mówi; naucza języka swego mówić kłamstwo, źle czyniąc ustawają
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Mieszkanie twoje, o proroku! jest w pośrodku ludu zdradliwego; dla zdrad nie chcą mię poznać, mówi Pan.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 A przetoż tak mówi Pan zastępów: Oto Ja pławiąc ich próbowałem ich; jakoż się tedy już mam obchodzić z córką ludu mego?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 Strzałą śmiertelną jest język ich, zdradę mówi; usty swemi o pokoju z przyjacielem swym mówi, ale w sercu swem zakłada nań sidła swoje.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Izali dlatego nienawidzę ich? mówi Pan; izali nad narodem takowym nie pomści się dusza moja?
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 Dla tych gór udam się na płacz i na narzekanie, i dla pastwisk, które są na puszczy, na kwilenie; bo spalone będą, tak, że nie będzie, ktoby je przechodził, ani tam głosu bydlęcia słychać będzie; ptastwo niebieskie i bydlęta rozbieżą się i odejdą.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 I obrócę Jeruzalem w gromady rumu, w mieszkanie smoków; a miasta Judzkie obrócę w pustynię, tak, iż nie będzie obywatela.
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 Któż jest tak mądry, coby to wyrozumiał? a do kogo mówiły usta Pańskie, coby to oznajmił, dlaczego zginąć ma ta ziemia, i wypalona być ma jako pustynia, tak aby nie było, ktoby ją przeszedł?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 Bo Pan mówi: Iż opuścili zakon mój, którym im przedłożył, a nie słuchali głosu mojego, ani chodzili za nim;
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 Ale chodzili za uporem serca swego i za Baalem, czego ich nauczyli ojcowie ich.
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 Dlatego tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Oto Ja nakarmię ich, to jest lud ten, piołunem, a napoję ich wodą żółci.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 Albowiem rozproszę ich między narody, których nie znali oni i ojcowie ich, i poślę za nimi miecz, aż ich do końca wygładzę.
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 Tak mówi Pan zastępów: Uważcie to, a przyzówcie narzekających niewiast, niech przyjdą, a do tych, które są w tem wyćwiczone, poślijcie, aby przyszły;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Niech się pospieszą, a niech uczynią nad nami narzekanie, aby oczy nasze łzy wylewały, a powieki nasze opływały wodą.
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 Głos zaiste narzekania słyszeć z Syonu: O jakośmy spustoszeni! bardzośmy zelżeni; bośmy stracili ziemię, bo rozrzucone są przybytki nasze.
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Owszem, słuchajcie niewiasty! słowa Pańskiego, a niech przyjmie ucho wasze wyrok ust jego, abyście uczyły córek swoich lamentu, a każda z was towarzyszkę swoję narzekania;
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 Bo wlazła śmierć oknami naszemi, weszła na pałace nasze, aby wytraciła dzieci z rynku, a młodzieńce z ulic.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 (Mów i to: Tak mówi Pan: ) I padły trupy ludzkie jako gnój po polu, a jako snopy za żeńcami, a niemasz ktoby pochował.
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 Tak mówi Pan: Niech się nie chlubi mądry z mądrości swojej, i niech się nie chlubi mocarz z mocy swojej, i niech się nie chlubi bogaty z bogactw swoich;
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 Ale w tem niechaj się chlubi, kto się chlubi, że rozumie a zna mię, żem Ja jest Pan, który czynię miłosierdzie, sąd i sprawiedliwość na ziemi; bo mi się to podoba, mówi Pan.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 Oto dni idą, mówi Pan, w których nawiedzę każdego obrzezańca i nieobrzezańca:
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 Egipczanów, i Judę, i Edomczyków, i Amonitczyków, i Moabczyków, i wszystkich, którzy w ostatnim kącie mieszkają na puszczy; bo te wszystkie narody nieobrzezane są, a wszystek dom Izraelski jest nieobrzezany sercem.
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

< Jeremiasza 9 >