< Jeremiasza 6 >

1 Zgromadźcie się, synowie Benjaminowi! z pośrodku Jeruzalemu, a w Tekue trąbcie w trąbę, i nad Betcherem podnieście chorągiew! bo złe ukazało się z północy, i zburzenie wielkie.
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2 Pięknej, rozkosznej pannie przypodobałem był córkę Syońską;
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3 Ale do niej przyciągną pasterze i trzody ich; rozbiją przeciwko niej namioty w około, spasie każdy miejsce swoje, i rzeką:
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4 Podnieście przeciwko niej wojnę, wstańcie, a wtargniemy w południe; biada nam, że się nachylił dzień, że się rozciągnęły cienie wieczorne!
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5 Wstańcie, a wtargniemy w nocy, i rozwalmy pałace jej.
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
6 Bo tak mówi Pan zastępów: Narąbcie drzewa, a usypcie przeciw Jeruzalemowi szańce; toć to miasto jest, które ma być nawiedzione; jakożkolwiek wielkie, niemasz jedno ucisk w pośrodku jego.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
7 Jako źródło wylewa wody swe, tak ono wylewa złość swoję; ucisk i spustoszenie słychać w niem przed obliczem mojem ustawicznie, boleść i bicie.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8 Ćwicz się Jeruzalemie! by snać nie odstąpiła dusza moja od ciebie, bym cię snać nie obrócił w pustynię ziemi do mieszkania niesposobną,
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
9 Tak mówi Pan zastępów: Ostatek Izraela aż do grona wyzbierają, jako winnicę, i rzeką: Sięgaj ręką twoją, jako ten, co zbiera wino do kosza.
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10 Do kogoż mówić będę, i kim oświadczę, aby słyszeli? Oto nieobrzezane są uszy ich, tak, że słuchać nie mogą; oto słowo Pańskie mają za hańbę i nie kochają się w niem.
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
11 Przetoż pełenem zapalczywości Pańskiej, upracowałem się, zawściągając ją w sobie. Wylana będzie tak na maluczkiego na ulicy, jako i na zebranie młodzieńców; owszem, i mąż z żoną, a starzec ze zgrzybiałym pojmany będzie.
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 I przypadną domy ich na inszych, także pola i żony ich, gdyż wyciągnę rękę moję na obywateli tej ziemi, mówi Pan.
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
13 Zaiste, od najmniejszego z nich aż do największego z nich, wszyscy się udali za łakomstwem; od proroka aż do kapłana, wszyscy zgoła bawią się kłamstwem.
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
14 I leczą skruszenie córki ludu mego tylko po wierzchu, mówiąc: Pokój, pokój! choć niemasz pokoju.
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
15 Izali się zawstydzili, przeto że obrzydłość czynili? Zaiste ani się lud wstydził, ani ich prorocy do wstydu przywieść mogli; przetoż upadną między padającymi; czasu, którego ich nawiedzę, upadną, mówi Pan.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
16 Gdy tak Pan mawiał: Zastanówcie się na drogach, a spojrzyjcie i pytajcie się o ścieszkach starych, któraby była droga dobra, a chodźcie nią, a znajdziecie odpocznienie duszy waszej: tedy odpowiadali: Nie będziemy chodzili.
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 A gdym postanawiał nad wami stróżów, mówiąc: Słuchajcie głosu trąby! tedy mawiali: Nie będziemy słuchać.
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 Przetoż słuchajcie, o narody! a poznaj, o zgromadzenie! co się dzieje między nimi.
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Słuchaj, o ziemio! Oto Ja przywiodę złe na ten lud, owoce myśli ich, przeto, że nie słuchają słów moich, ani zakonu mego, ale go odrzucają.
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
20 Na cóż mi kadzidło z Saby przychodzi, a cynamon wonny wyborny z ziemi dalekiej? Całopalenia wasze nie są mi przyjemne, i ofiary wasze nie podobają mi się.
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21 Przetoż tak mówi Pan: Oto ja nakładę ludowi temu zawad, o które się otrącać będą ojcowie, także i synowie, sąsiad i bliźni jego, i poginą.
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22 Tak mówi Pan: Oto lud przyciągnie z ziemi północnej, a naród wielki powstanie od kończyn ziemi;
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Łuk i włócznię pochwyci, okrutny będzie, a nie zlituje się. Głos ich jako morze zahuczy, a na koniach jeździć będą, naród uszykowany jako mąż do boju przeciwko tobie, o córko Syońska!
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24 Skoro usłyszymy wieść o nim, osłabieją ręce nasze, ucisk nas ogarnie, i boleść jako rodzącą.
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Nie wychodźcie na pole, i w drogę nie chodźcie; bo miecz nieprzyjacielski a strach w około.
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 O córko ludu mojego! przepasz się worem a walaj się w popiele; uczyń sobie żal jako po jedynaku, żal gorzki; bo na nas nagle burzyciel przypadnie.
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
27 Dałem cię za basztę i za wieżę w ludu moim, abyś upatrywał i doświadczał drogi ich.
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
28 Wszyscy są między krnąbrnymi najkrnąbrniejsi, chodzą jako obmowca, są jako miedź i żelaza; wszyscy zgoła są skażonymi.
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Murzszeją miechy, ołów od ognia niszczeje, próżno ustawicznie złotnik pławi; bo złe rzeczy nie mogą być oddalone.
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 Srebrem fałszywem będą nazwani; bo ich Pan odrzucił.
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”

< Jeremiasza 6 >