< Jeremiasza 50 >

1 Słowo, które mówł Pan przeciwko Babilonowi, i przeciwko ziemi Chaldejskiej przez Jeremijasza proroka;
Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
2 Opowiadajcie między narodami, a rozgłaszajcie, podnieście chorągiew, rozgłaszajcie, nie tajcie, mówcie: Wzięty będzie Babilon, pohańbiony będzie Bel, potarty będzie Merodach, pohańbione będą bałwany jego, pokruszeni będą plugawi bogowie jego.
“Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
3 Bo przyciągnie przeciwko niemu naród z północy, który ziemię jego obróci w pustynię, tak, że nie będzie, coby mieszkał w niej; tak ludzie jako i bydlęta ruszą się i odejdą.
Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
4 W onych dniach, i w onych czasach, mówi Pan, przyjdą synowie Izraelscy, oni i synowie Judzcy; płacząc społem ochotnie pójdą, a Pana, Boga swego, szukać będą.
“Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
5 O drodze do Syonu pytać się będą, a obuciwszy się tam twarzą, rzekną: Pójdźcie, a przyłączcie się do Pana przymierzem wiecznem, które nie przyjdzie w zapamiętanie.
Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
6 Lud mój jest jako trzoda owiec straconych, pasterze ich zawiedli ich w błąd, po górach rozegnali ich: z góry na pagórek chodziły, zapomniawszy legowiska swego.
“Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
7 Wszyscy, którzy ich znajdują, pożerają ich, a nieprzyjaciele ich mówią: Nie będziemy nic winni, przeto, że zgrzeszyli Panu w przybytku sprawiedliwości, Panu, który jest nadzieją ojców ich.
Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
8 Uchodźcie z pośrodku Babilonu, a z ziemi Chaldejskiej wychodzcie, i będźcie jako kozły przed trzodą.
“Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
9 Bo oto Ja wzbudzę i przywiodę na Babilon zgromadzenie narodów wielkich z ziemi północnej; którzy się uszykują przeciwko niemu, a stamtąd go wezmą; których strzały są jako mocarza osieracającego, z których żadna się nie wróci próżno.
Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
10 I będzie Chaldejska ziemia na łup, a wszyscy, którzy ją złupią, nasyceni będą, mówi Pan.
Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
11 Przeto, że się weselicie, przeto, że się radujecie, rozchwytając dziedzictwo moje, przeto, żeście nabrali ciała jako jałowica utuczona, a wyskakujecie jako mocarze.
“Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
12 Zawstydzona będzie matka wasza bardzo; zapłonie się rodzicielka wasza; oto najpośledniejszą będzie z narodów, pustą ziemią, suchą i bezdrożną.
Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
13 Dla gniewu Pańskiego nie bądą w niej mieszkać, ale ona wszystka obróci się w pustynię; ktokolwiek pójdzie mimo Babilonu, zdumieje się, i zaświśnie nad wszystkiemi plagami jego.
Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
14 Szykujcie wojska przeciw Babilonowi zewsząd wszyscy, co ciągniecie łuk, strzelajcie do niego, nie żałujcie strzał; bo przeciwko Panu zgrzeszył.
“Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
15 Wołajcie przeciwko niemu zewsząd; poddał się, upadły grunty jego, skażone są mury jego; bo pomsta Pańska jest. Pomścijcież się nad nim; jako on czynił innym, tak mu też uczyńcie.
Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
16 Wytraćcie siejącego z Babilonu, i tego, który trzyma śierp czasu żniwa; przed ostrzem miecza burzącego każdy niech się do ludu swego obróci, i każdy do ziemi swojej niech uciecze.
Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
17 Izrael jest jako bydlądko zagnane, które lwy zapłoszyły. Król Assyryjski najpierwszy był, który go żreć począł, a ten ostateczny, Nabuchodonozor, król Babiloński, kości jego pokruszył.
“Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
18 Przetoż tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Oto Ja nawiedzę króla Babilońskiego i ziemię jego, jakom nawiedził króla Assyryskiego;
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 I przywrócę zaś Izraela do mieszkania jego, a paść się będzie na Karmelu, i na Basanie, i na górze Efraimowej, a w Galaadzie nasycona będzie dusza jego.
Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 W onych dniach i w onych czasach, mówi Pan, będą szukać nieprawości Izraelowej, ale żadnej nie będzie; i grzechów Judzkich, ale nie będą znalezione; bo odpuszczę tym, których pozostawię.
Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
21 Wyciągnij przeciwko tej ziemi odpornych, przeciwko niej, mówię, a obywateli jej nawiedź; spustosz a wygładź, goniąc ich, mówi Pan; uczyńże według wszystkiego, jakoć rozkazuje.
“Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
22 Niech będzie głos wojenny w tej ziemi, i spustoszenie wielkie.
Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
23 Jakożby posiekany i połamany być miał młot wszystkiej ziemi? Jakożby się Babilon stał zdumienie między narodami?
Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
24 Sidłom zastawił na cię, i będziesz pojmany, o Babilonie! nim się obaczysz; znaleziony nawet i pojmany będziesz, ponieważeś z Panem zwadę zaczął.
Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
25 Otworzył Pan skarb swój, a wyniósł naczynia gniewu swego; bo to jest sprawa Pana, Pana zastępów w ziemi Chaldejskiej.
Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
26 Pójdźcież przeciwko niej od kończyn ziemi, otwórzcież szpichlerze jej podepczcie ją jako stogi, a wygładźcie ją tak, aby jaj nic nie zostało;
Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
27 Pozabijajcie wszystkie cielce jej, niech zstępują na zabicie. Biada im! bo przyszedł dzień ich, czas nawiedzenia ich.
Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
28 Głos uciekających, i tych, co uchodzą, z ziemi Babilońskiej, aby oznajmili na Syonie pomstę Pana, Boga naszego, pomstę kościoła jego.
Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
29 Zgromadzcie przeciwko Babilonowi wszystkich strzelców, którzy łuk ciągną; połóżcie się obozem przeciw niemu w około, aby nikt nie uszedł; oddajcie mu według spraw jego, według wszystkiego, co innym czynił, uczyńcie mu; bo się przeciwko Panu wynosił, przeciwko Świętemu Izraelskiemu.
“Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
30 Przetoż polegną młodzieńcy jego na ulicach jego, i wszyscy mężowie waleczni jego wygładzeni będą dnia onego, mówi Pan.
Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
31 Otom ja przeciwko tobie, o hardy! mówi Pan, Pan zastępów; bo już przyszedł dzień twój i czas, abym cię nawiedził.
“Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
32 Potknie się zaiste hardy, i upadnie, a nie będzie, ktoby go podniósł; i rozniecę ogień w miastach jego, który pożre wszystko około niego.
Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
33 Tak mówi Pan zastępów: Gwałt się dzieje synom Izraelskim i synom Judzkim społem, a wszyscy, którzy ich pojmali, trzymają ich, nie chcą ich puścić.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
34 Ale odkupiciel ich możny, Pan zastępów imię jego, pewnie że się ujmie o krzywdę ich, aby sprawił pokój tej ziemi, i poruszył obywateli Babilońskich.
Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
35 Miecz przyjdzie na Chaldejczyków, mówi Pan, i na obywateli Babilońskich, i na książąt jego, i na mędrców jego;
Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
36 Miecz na kłamców, aby zgłupieli, miecz na mocarzy jego, aby skruszeni byli;
Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
37 Miecz na konie jego, i na wozy jego, i na wszystko pospólstwo, które jest w pośrodku jego, aby byli jako niewasty; miecz na skarby jego, aby były rozchwycone;
Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
38 Susza na wody jego, aby wyschły; bo ziemia jest pełna obrazów rytych, a przy bałwanach swoich szaleją.
Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
39 Przeto tam mieszkać będą bestyje i straszne zwierzęta, mieszkać w nim będą młode sowy; a nie będą w nim mieszkać więcej na wieki, i nie będą w nim mieszkać od narodu do narodu.
“Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
40 Jako Pan podwrócił Sodomę i Gomorę, i przyległości ich, mówi Pan, tak się tam nikt nie osadzi, ani będzie mieszkał w niej syn człowieczy.
Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
41 Oto lud przyciągnie od północy, i naród wielki, i królowie wielcy wzbudzeni będą ze stron ziemi.
“Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
42 Łuk i włóczni pochwycą, okrutnymi będą, a nie zmiłują się; głos ich jako morze zaszumi, a na koniach pojadą, uszykowani jako mąż do bitwy przeciwko tobie, o córko Babilońska!
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
43 Jako usłyszy król Babiloński wieść o nich, osłabieją ręce jego, a ucisk ogarnie go, i boleść jako rodzącą.
Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
44 Oto aczkolwiek jako lew występuje, i bardzej niż nadętość Jordanu się podnosi przeciwko przybytkowi mocnego, wszakże go w okamgnieniu wypędzę z niej, a tego, który jest wybrany, przełożę nad nią; bo któż jest mnie podobnym; i kto mi da rok? a kto jest tym pasterzem, któryby się postawił przeciwko mnie?
Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
45 Przetoż słuchajcie rady Pańskiej, którą uradził przeciwko Babilonowi; i zamysłów jego, które umyślił przeciwko ziemi Chaldejskiej; zaiste żeć ich wywloką najmniejsi z tej trzody, zaiste poburzą ich i przybytek ich.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
46 Od huku przy dobywaniu Babilonu poruszy się ta ziemia, a krzyk między narodami słyszany będzie.
Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.

< Jeremiasza 50 >