< Jeremiasza 49 >

1 Przeciwko synom Amonowym. Tak mówi Pan: Izali Izrael nie ma synów? Izali żadnego dziedzica nie ma? czemuż król ich dziedzicznie opanował Gad, a lud jego czemu mieszka w miastach jego?
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 Przetoż oto dni idą, mówi Pan, sprawię, że usłyszą trąbienie wojenne przeciwko Rabbie synów Amonowych, i będzie obrócona w kupę rumu, a inne miasta jego ogniem spalone będą, i posiędzie Izrael dzierżawców swoich, mówi Pan.
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 Rozrzewnij się, Hesebonie! bo Haj spustoszone będzie; krzyczcie, o córki Rabby! przepaszcie się worami, narzekajcie, a tułajcie się około płotów; bo król wasz do więzienia pójdzie, także kapłani jego, i książęta jego społem.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 Cóż się przechwalasz dolinami? Spłynęła dolina twoja, o córko uporna! która ufasz w skarbach twoich, mówiąc: Któż przyciągnie przeciwko mnie?
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 Oto Ja przywiodę na cię strach, mówi Pan, Pan zastępów od wszystkich, którzy są około ciebie, przez który rozegnani będziecie jeden od drugiego, a nie będzie, ktoby zebrał tułających się.
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 Wszakże potem przywiodę zaś więźniów synów Amonowych, mówi Pan.
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 Przeciwko Edomczykom. Tak mówi Pan zastępów: Izali niemasz więcej mądrości w Teman? Izali zginęła rada od roztropnych, a wniwecz się obróciła mądrość ich?
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 Uciekajcie, obróćcie się, zstąpcie w głębokość na mieszkanie, obywatele Dedan! bo przywiodę zatracenie na Ezawa czasu nawiedzenia jego.
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 Gdyby ci, którzy zbierają wino, przyszli na cię, izaliby nie zostawili jakich gron? gdyby się wkradli złodzieje w nocy, azażby szkodzili więcej nad potrzebę swoję?
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Lecz Ja obnażę Ezawa, odkryję skrytości jego, tak, iż się ukryć nie będzie mógł: zniszczone będzie nasienie jego, i bracia jego, i sąsiedzi jego, tak, że zgoła nie będzie, ktoby rzekł:
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 Zaniechaj sierotek twoich, ja je żywić będę, a wdowy twoje we mnie ufać będą.
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 Tak zaiste mówi Pan: Oto ci, którym nie przysądzono pić z kubka tego, przecie piją z niego, a tybyś miał zgoła tego ujść?
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 Nie ujdziesz, ale koniecznie pić będziesz; bo przez się przysięgam, mówi Pan, iż na spustoszenie, na pohańbienie, na zburzenie, i na przeklęstwo Bocra przyjdzie, i wszystkie miasta jego będą pustemi na wieki.
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 Słyszałem wieść od Pana, że do narodów posłany jest poseł mówiący: Zgromadźcie się, a ciągnijcie, przeciwko niemu, wstańcież do bitwy.
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 Bo oto sprawię, abyś był najlichszym między narodami, i wzgardzonym miedzy ludźmi.
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Hardość twoja zdradzi cię, i pycha serca twego, ty, który mieszkasz w rozsiadlinach skalnych, który się trzymasz wysokich pogórków; byś też wywyższył jako orzeł gniazdo swoje, i stamtąd cię stargnę, mówi Pan.
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 I będzie ziemia Edomska pustynią, i ktokolwiek pójdzie przez nię, zdumieje się, i świstać będzie nad wszystkiemi plagami jej.
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Jako podwrócona jest Sodoma i Gomora z przyległościami swojemi, mówi Pan, tak się tam nikt nie osadzi, ani w niej syn człowieczy mieszkać będzie.
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 Oto aczkolwiek jako lew występuje, i bardziej niż nadęcie Jordanu się podnosi przeciwko przybytkowi Mocnego: wszakże go nagle wypędzę z tej ziemi, a tego, który jest obrany, przełożę nad nią: bo któż mnie jest podobny? i kto mi da rok; a kto jest tym pasterzem, któryby się postawił przeciwko mnie?
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Przetoż słuchajcie rady Pańskiej, którą uradził przeciwko Edomczykom; i zamysłów jego, które umyślił przeciwko obywatelom Temańskim; zaiste żeć ich wywleką najmniejsi z tej trzody, zaiste pobudzą ich, i przybytki ich.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Od grzmotu upadku ich wzruszy się ziemia; głos i krzyk ich słyszeć będą na morzu Czerwonem.
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Oto jako orzeł przypadnie i przyleci, a rozciągnie skrzydła swe nad Bocrą, i stanie się serce mocarzów z Edom dnia onego, jako serce niewiasty bolejącej.
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 Przeciwko Damaszkowi. Zawstydzi się Emat i Arfad; bo wieść złą usłyszą, i zatrwożą się, tak że się i morze wzruszy, a nie będzie się mogło uspokoić.
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Osłabieje Damaszek, uda się do uciekania, a strach go ogarnie; uciski i boleści ogarną go, jako rodzącą.
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Ale rzeką: Jakożby się nie miało ostać miasto sławne, miasto wesela mego?
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Przetoż upadną młodzieńcy jego na ulicach jego, a wszyscy mężowie waleczni dnia onego wytraceni będą, mówi Pan zastępów.
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 I rozniecę ogień w murze Damaszku, który strawi pałace Benadadowe.
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 Przeciwko Kiedar, i przeciwko królestwom Hasor, które wytracić ma Nabuchodonozor, król Babiloński; tak mówi Pan: Wstańcie, ciągnijcie przeciwko Kiedar, a zburzcie narody wschodnie.
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Namioty ich i trzody ich zabiorą; opony ich ze wszystkiem naczyniem ich i wielbłądy ich wezmą ze sobą, i zawołają na nich: Strach zewsząd.
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 Uciekajcie, rozpierzchnijcie się prędko, zstąpcie w głębokości na mieszkanie, obywatele Hasor! mówi Pan; bo zawarł radę przeciwko wam Nabuchodonozor, król Babiloński, i umyślił przeciwko wam zdradę.
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 Wstańcie, ciągnijcie przeciwko narodowi spokojnemu, mieszkającemu bezpiecznie, mówi Pan: nie ma ani wrót, ani zawór, samotni mieszkają.
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 Będą zaiste wielbłądy ich podane na łup, a mnóstwo dobytku ich na korzyść; i rozproszę na wszystkie wiatry tych, którzy i w najostateczniejszych kątach mieszkają, i ze wszystkich stron złe na nich przywiodę, mówi Pan.
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 I stanie się Hasor mieszkaniem smoków, pustynią aż na wieki; nie osadzi się tam nikt, ani mieszkać będzie w nim syn człowieczy.
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 Słowo Pańskie, które się stało do Jeremijasza proroka przeciwko Elamczykom na początku królowania Sedekijasza, króla Judzkiego, mówiąc:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 Tak mówi Pan zastępów: Oto ja złamię łuk Elamczyków, największą siłę ich;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 A przywiodę przeciwko Elamczykom cztery wiatry ze czterech stron świata, i rozproszę ich na wszystkie one wiatry, tak, iż nie będzie narodu, do któregoby się nie dostali wygnańcy z Elam;
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 I zatrwożę Elamczyków przed obliczem nieprzyjaciół ich, i przed obliczem tych, którzy szukają duszy ich; przywiodę, mówię, na nich złe, gniew popędliwości mojej, mówi Pan, a posyłać za nimi będę miecz, dokąd ich nie wyniszczę;
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 I postawię stolicę moję między Elamczykami, a wytracę stamtąd króla i książąt, mówi Pan.
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 Wszakże stanie się, że w ostateczne dni przywrócę zaś więźniów Elam, mówi Pan.
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.

< Jeremiasza 49 >